< 1 Mafumu 21 >
1 Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
Sedan detta skedt var, begaf sig, att Naboth, en Jisreelit, hade en vingård i Jisreel, vid Achabs palats, Konungens i Samaria.
2 Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
Och Achab talade med Naboth, och sade: Låt mig få din vingård; jag vill göra mig der en kålgård af, efter han ligger så när mitt hus; jag vill gifva dig en bättre vingård igen; eller, om dig så täckes, vill jag gifva dig der silfver före, så mycket han är värd.
3 Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
Men Naboth sade till Achab: Det låte Herren vara långt ifrå mig, att jag skulle låta dig få mina fäders arf.
4 Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
Då kom Achab hem, illa tillfrids och vred, för det ordets skull, som Naboth den Jisreeliten till honom talat hade, och sagt: Jag vill icke låta dig få mina fäders arf. Och han lade sig uppå sin säng, och vände sitt anlete, och åt intet bröd.
5 Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
Då kom Isebel hans hustru in till honom, och sade till honom: Hvad är det, att din ande är så illa tillfrids, och du intet bröd äter?
6 Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
Han sade till henne: Jag hafver talat till Naboth den Jisreeliten, och sagt: Låt mig få din vingård för penningar; eller, om du hafver der lust till, vill jag gifva dig en annan igen; men han sade: Jag vill icke låta dig få min vingård.
7 Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
Då sade Isebel hans hustru till honom: Hvad vore för ett rike i Israel, om du gjordet? Statt upp, och ät bröd, och var vid godt mod; jag vill skaffa dig Naboths den Jisreelitens vingård.
8 Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
Och hon skref bref under Achabs namn, och beseglade det med hans signet, och sände till de äldsta och öfversta i hans stad, de som bodde med Naboth;
9 Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
Och skref brefvet alltså: Låter utropa en fasto, och sätter Naboth främst ibland folket;
10 Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
Och låter komma två Belials män fram för honom, som vittna, och säga: Du hafver välsignat Gud och Konungen; och förer honom ut, och stener honom till döds.
11 Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
De äldste och hans stads öfverstar, som i hans stad bodde, gjorde såsom Isebel dem budit hade, såsom i brefvet skrifvet var, det hon till dem sändt hade;
12 Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
Och läto utropa en fasto, och läto Naboth sitta öfverst ibland folket.
13 Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
Då kommo de två Belials män, och ställde sig framför honom, och vittnade emot Naboth inför folket, och sade: Naboth hafver välsignat Gud och Konungen. Då förde de honom ut för staden, och stenade honom ihjäl.
14 Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
Och de bådade Isebel, och sade: Naboth är stenad, och död.
15 Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
Då nu Isebel hörde, att Naboth var stenad, och död, sade hon till Achab: Statt upp, och tag in Naboths vingård den Jisreelitens, den han dig nekat hafver för penningar; förty Naboth lefver icke, utan är död.
16 Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
Då Achab hörde, att Naboth var död, stod han upp, att han skulle gå ned till Naboths den Jisreelitens vingård, och taga honom in.
17 Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
Men Herrans ord kom till Elia den Thisbiten, och sade:
18 “Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
Statt upp, och gack ned emot Israels Konung, som är i Samarien; si, han är i Naboths vingård, dit han nedergången är, till att taga honom in.
19 Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
Och tala med honom, och säg: Så säger Herren: Du hafver dräpit, dertill ock intagit. Och du skall tala med honom, och säga: Detta säger Herren: På den staden, der hundar hafva slekt Naboths blod, skola ock hundar sleka ditt blod.
20 Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
Och Achab sade till Elia: Hafver du ju funnit mig för din fienda? Han sade: Ja, hafver jag så funnit dig; derföre, att du såld äst till att intet annat göra, än det ondt är för Herranom.
21 Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
Si, jag skall låta komma ondt öfver dig, och borttaga dina efterkommande, och skall utrota utaf Achab ock den som på väggena pissar, och den som innelyckt och igenlefd är i Israel;
22 Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
Och skall göra ditt hus såsom Jerobeams hus, Nebats sons, och såsom Baesa hus, Ahia sons, för det retandets skull, der du mig med förtörnat hafver, och kommit Israel till att synda.
23 “Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
Och om Isebel talade Herren desslikes, och sade: Hundar skola uppäta Isebel vid murarna i Jisreel.
24 “Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
Hvilken af Achab dör i stadenom, den skola hundar äta; och hvilken som dör på markene, den skola foglar under himmelen äta.
25 (Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
Alltså var ingen, den, så alldeles såld var till att göra det ondt var för Herranom, såsom Achab; ty hans hustru Isebel eggade honom dertill.
26 Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
Och han gjorde sig till en stor styggelse, så att han vandrade efter afgudar, såsom de Amoreer gjort hade, hvilka Herren för Israels barn fördrifvit hade.
27 Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
Då Achab dessa orden hörde, ref han sönder sin kläder, och drog en säck på sin kropp, och fastade, och sof i säckenom, och gick luto.
28 Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
Och Herrans ord kom till Elia den Thisbiten, och sade:
29 “Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”
Hafver du icke sett, huru Achab bugar sig för mig? Efter han nu bugar sig för mig, vill jag icke låta komma det onda i hans dagar; men i hans sons tid skall jag låta komma det onda öfver hans hus.