< 1 Mafumu 21 >

1 Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
Og det skete efter disse Handeler, at Jisreeliteren Naboth havde en Vingaard, som var i Jisreel ved Akabs Palads, Kongens i Samaria.
2 Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
Og Akab talede til Naboth og sagde: Giv mig din Vingaard, at den maa være mig til en Urtehave, efterdi den er nær ved mit Hus, og jeg vil give dig en Vingaard for den, som er bedre end denne; eller om dig godt synes, vil jeg give dig Penge for den, saa meget som den er værd.
3 Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
Og Naboth sagde til Akab: Herren lade det være langt fra mig, at jeg skulde give dig mine Fædres Arv.
4 Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
Da kom Akab ilde tilfreds og vred til sit Hus for det Ords Skyld, søm Jisreeliteren Naboth havde talt til ham og sagt: Jeg vil ikke give dig mine Fædres Arv; og han lagde sig paa sin Seng og vendte sit Ansigt omkring og aad ikke Brød.
5 Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
Da kom Jesabel, hans Hustru, til ham, og hun sagde til ham: Hvad er det for noget, at din Aand er saa ilde tilfreds, at du ikke æder Brød?
6 Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
Og han sagde til hende: Fordi jeg talte til Jisreeliteren Naboth og sagde til ham: Giv mig din Vingaard for Penge, eller om du har Lyst dertil, da vil jeg give dig en anden Vingaard for den, og han sagde: Jeg vil ikke give dig min Vingaard.
7 Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
Da sagde Jesabel, hans Hustru, til ham: Du, jo, du skulde nu have Kongemagt over Israel! staa op, æd Brød og lad dit Hjerte være vel til Mode, jeg vil give dig Jisreeliteren Naboths Vingaard.
8 Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
Og hun skrev Breve i Akabs Navn og forseglede dem med hans Signet, og hun sendte Brevene til de ældste og til de ypperste, som vare i hans Stad, og som boede ved Naboth.
9 Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
Og hun skrev i Brevene og sagde: Lader udraabe en Faste, og sætter Naboth øverst iblandt Folket!
10 Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
Og sætter to Mænd, Belials Børn, tværs overfor ham, som skulle vidne imod ham og sige: Du har bandet Gud og Kongen; og fører ham ud og stener ham, at han dør.
11 Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
Og de ældste Mænd og ypperste i hans Stad, som boede i hans Stad, gjorde, ligesom Jesabel havde ladet sige til dem, ligesom der var skrevet i Brevene, som hun havde sendt til dem.
12 Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
Delode udraabe en Faste og satte Naboth øverst iblandt Folket.
13 Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
Og de to Mænd, de Belials Børn, kom og satte sig tværs overfor ham, og de Belials Mænd vidnede imod Naboth for Folket og sagde: Naboth bandede Gud og Kongen; og de førte ham ud uden for Staden og stenede ham med Stene, at han døde.
14 Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
Og de sendte til Jesabel og lode sige: Naboth er stenet og er død.
15 Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
Og det skete, der Jesabel hørte, at Naboth var stenet og var død, da sagde Jesabel til Akab: Staa op, tag til Eje Jisreeliteren Naboths Vingaard, som han vægrede sig ved at give dig for Penge; thi Naboth lever ikke, men er død.
16 Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
Og det skete, der Akab hørte, at Naboth var død, da stod Akab op at gaa ned i Jisreeliteren Naboths Vingaard for at tage den til Eje.
17 Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
Og Herrens Ord skete til Thisbiteren Elias og sagde:
18 “Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
Staa op, gak ned imod Akab, Israels Konge, som er i Samaria; se, han er i Naboths Vingaard, hvorhen han er gaaet ned for at tage den til Ejendom.
19 Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
Og du skal tale til ham og sige: Saaledes sagde Herren: Har du baade myrdet og tilmed taget en Ejendom? Fremdeles skal du tale til ham og sige: Saa siger Herren: Paa det Sted, hvor Hundene slikkede Naboths Blod, skulle Hundene slikke dit Blod, ja ogsaa dit.
20 Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
Og Akab sagde til Elias: Har du fundet mig, min Fjende? Og han sagde: Jeg har fundet dig, fordi du har solgt dig selv til at gøre det onde for Herrens Øjne.
21 Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
Se, jeg vil føre Ulykke over dig og borttage dine Efterkommere og udrydde af alt Akabs Hus enhver af Mandkøn og den bundne og den løsladte i Israel.
22 Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
Og jeg vil gøre dit Hus som Jeroboams, Nebats Søns, Hus, og som Baesas, Ahias Søns, Hus, for den Opirrelses Skyld, som du har opirret mig med, og fordi du kom Israel til at synde.
23 “Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
Og om Jesabel har Herren ogsaa talt og sagt: Hundene skulle æde Jesabel inden Jisreels Mure.
24 “Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
Hvo som dør i Staden af Akabs Hus, skulle Hundene æde, og hvo som dør paa Marken, skulle Fuglene under Himmelen æde.
25 (Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
Dog var der ingen som Akab, der havde solgt sig selv til at gøre det onde for Herrens Øjne, fordi hans Hustru Jesabel tilskyndte ham;
26 Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
og han handlede saare vederstyggeligt, idet han vandrede efter de stygge Afguder, aldeles ligesom Amoriterne gjorde, hvilke Herren fordrev for Israels Børns Ansigt.
27 Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
Og det skete, der Akab hørte disse Ord, da sønderrev han sine Klæder og lagde Sæk om sin Krop og fastede, og han laa i Sæk og gik sagtelig.
28 Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
Og Herrens Ord skete til Thisbiteren Elias og sagde:
29 “Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”
Har du set, at Akab har ydmyget sig for mit Ansigt? fordi han har ydmyget sig for mit Ansigt, vil jeg ikke lade det onde komme i hans Dage; i hans Søns Dage vil jeg føre det onde over hans Hus.

< 1 Mafumu 21 >