< 1 Mafumu 21 >

1 Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
Stalo se pak po těch věcech, měl Nábot Jezreelský vinici, kteráž byla v Jezreel podlé paláce Achaba krále Samařského.
2 Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
I mluvil Achab k Nábotovi, řka: Dej mi vinici svou, ať ji mám místo zahrady k zelinám, poněvadž jest blízko podlé domu mého, a dámť za ni vinici lepší, než ta jest, aneb jestližeť se vidí, dámť stříbra cenu její.
3 Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
Odpověděl Nábot Achabovi: Nedejž mi toho Hospodin, abych měl dáti dědictví otců mých tobě.
4 Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
Tedy přišel Achab do domu svého, smutný jsa a hněvaje se pro řeč, kterouž mluvil jemu Nábot Jezreelský, řka: Nedám tobě dědictví otců svých. I lehl na lůžko své, a odvrátiv tvář svou, ani chleba nejedl.
5 Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
V tom přišedši k němu Jezábel žena jeho, řekla jemu: Proč tak smutný jest duch tvůj, že ani nejíš chleba?
6 Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
Kterýž odpověděl jí: Proto že jsem mluvil s Nábotem Jezreelským, a řekl jsem jemu: Dej mi vinici svou za peníze, aneb jestliže raději chceš, dámť jinou vinici za ni. On pak odpověděl: Nedám tobě své vinice.
7 Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
I řekla mu Jezábel žena jeho: Takliž bys ty nyní spravoval království Izraelské? Vstaň, pojez chleba a buď dobré mysli, já tobě dám vinici Nábota Jezreelského.
8 Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
Zatím napsala list jménem Achabovým, kterýž zapečetila jeho pečetí, a poslala ten list k starším a předním města jeho, spoluobyvatelům Nábotovým.
9 Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
Napsala pak v tom listu takto: Vyhlaste půst, a posaďte Nábota mezi předními z lidu,
10 Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
A postavte dva muže nešlechetné proti němu, kteříž by svědčili na něj, řkouce: Zlořečil jsi Bohu a králi. Potom vyveďte ho a ukamenujte jej, ať umře.
11 Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
Učinili tedy muži města toho, starší a přední, kteříž bydlili v městě jeho, jakž rozkázala jim Jezábel, tak jakž psáno bylo v listu, kterýž jim byla poslala.
12 Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
Vyhlásili půst, a posadili Nábota mezi předními z lidu.
13 Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
Potom přišli ti dva muži nešlechetní, a posadivše se naproti němu, svědčili proti němu muži ti nešlechetní, proti Nábotovi před lidem, řkouce: Zlořečil Nábot Bohu a králi. I vyvedli ho za město a kamenovali jej, až umřel.
14 Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
A poslali k Jezábel, řkouce: Ukamenovánť jest Nábot a umřel.
15 Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
I stalo se, jakž uslyšela Jezábel, že by ukamenován byl Nábot, a že by umřel, řekla Achabovi: Vstaň, vládni vinicí Nábota Jezreelského, kteréžť nechtěl dáti za peníze; neboť není živ Nábot, ale umřel.
16 Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
A tak uslyšev Achab, že by umřel Nábot, vstal, aby šel do vinice Nábota Jezreelského, a aby ji ujal.
17 Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
Tedy stala se řeč Hospodinova k Eliášovi Tesbitskému, řkoucí:
18 “Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
Vstana, vyjdi vstříc Achabovi králi Izraelskému, kterýž bydlí v Samaří, a hle, jest na vinici Nábotově, do níž všel, aby ji ujal.
19 Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
A mluviti budeš k němu těmito slovy: Takto praví Hospodin: Zdaliž jsi nezabil, ano sobě i nepřivlastnil? Mluv tedy k němu, řka: Takto praví Hospodin: Proto že lízali psi krev Nábotovu, i tvou krev také lízati budou.
20 Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
I řekl Achab Eliášovi: Což jsi mne našel, nepříteli můj? Kterýž odpověděl: Našel, nebo jsi prodal se, abys činil to, což zlého jest před oblíčejem Hospodinovým.
21 Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
Aj, já uvedu na tebe zlé, a odejmu potomky tvé, a vypléním z domu Achabova močícího na stěnu, i zajatého i zanechaného v Izraeli.
22 Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
A učiním s domem tvým jako s domem Jeroboáma syna Nebatova, a jako s domem Bázy syna Achiášova, pro zdráždění, kterýmž jsi mne popudil, a že jsi k hřešení přivodil Izraele.
23 “Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
Ano i proti Jezábel mluvil Hospodin, řka: Psi žráti budou Jezábel mezi zdmi Jezreelskými.
24 “Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
Toho, kdož umře z domu Achabova v městě, psi žráti budou, a kdož umře na poli, ptáci nebeští jísti budou.
25 (Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
Nebo nebylo podobného Achabovi, kterýž by se prodal, aby činil to, což zlého jest před oblíčejem Hospodinovým, proto že ho ponoukala Jezábel žena jeho.
26 Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
Dopouštěl se zajisté věcí velmi ohavných, následuje modl vedlé všeho toho, čehož se dopouštěli Amorejští, kteréž vyplénil Hospodin od tváři synů Izraelských.
27 Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
I stalo se, když uslyšel Achab slova tato, že roztrhl roucho své, a vzav žíni na tělo své, postil se a léhal na pytli, a chodil krotce.
28 Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
Tedy stala se řeč Hospodinova k Eliášovi Tesbitskému, řkoucí:
29 “Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”
Viděl-lis, jak se ponížil Achab před tváří mou? Poněvadž se tak ponížil před tváří mou, neuvedu toho zlého za dnů jeho, ale za dnů syna jeho uvedu to zlé na dům jeho.

< 1 Mafumu 21 >