< 1 Mafumu 20 >

1 Tsono Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu inasonkhanitsa magulu ake onse a ankhondo. Iye pamodzi ndi mafumu 32, akavalo awo ndi magaleta awo, anapita kukawuzungulira mzinda wa Samariya ndi kuwuthira nkhondo.
Cependant Ben-Hadad, roi de Syrie, ayant trente-deux rois pour auxiliaires, rassembla toutes ses forces, et chevaux et chars, et il s'avança, et mit le siège devant Samarie et l'attaqua.
2 Iye anatuma amithenga ake mu mzindamo kwa Ahabu mfumu ya Israeli, kukanena kuti,
Et il envoya des messagers à Achab, roi d'Israël, dans la ville
3 “Beni-Hadadi akuti, ‘Siliva wako ndi golide wako ndi wanga, ndipo akazi ako okongola ndi ana ako ndi anganso.’”
et lui tint ce langage: Ainsi parle Ben-Hadad: Je suis maître de ton argent et de ton or, maître de tes femmes et de tes fils, de tes meilleurs biens.
4 Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Monga mmene mwanenera, mbuye wanga mfumu, ine pamodzi ndi zonse zomwe ndili nazo ndi zanu.”
Et le roi d'Israël répondit et dit: Comme tu le dis, roi mon seigneur, tu es maître de ma personne et de tout ce que j'ai.
5 Amithenga aja anabwereranso kwa Ahabu ndipo anamuwuza kuti, “Beni-Hadadi akuti, ‘Ine ndinakulamula kuti undipatse siliva wako ndi golide wako, akazi ako ndi ana ako.
Et les messagers revinrent et dirent: Ainsi parle Ben-Hadad: Si je t'ai envoyé dire: Livre-moi ton argent et ton or, et tes femmes et tes fils,
6 Koma mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzatuma atumiki anga kudzafufuza mʼnyumba yako yaufumu ndi nyumba za akuluakulu ako. Iwo adzatenga chilichonse chimene umachidalira ndi kupita nacho.’”
c'est que demain à pareille heure j'enverrai chez toi mes serviteurs pour fouiller ta maison et les maisons de tes serviteurs et mettre la main sur tout ce qui charme tes yeux et l'enlever.
7 Pamenepo mfumu ya Israeli inayitanitsa akuluakulu a mʼdzikomo niwawuza kuti, “Taonani momwe munthuyu akufunira kutibweretsera mavuto! Atatumiza mawu oti ndimupatse akazi anga ndi ana anga, siliva wanga ndi golide wanga, ine sindinamukanize.”
Alors le roi d'Israël fit assembler tous les Anciens du pays et dit: Sachez donc et considérez qu'il cherche [notre] ruine, puisqu'il m'a envoyé une sommation par rapport à mes femmes et à mes fils, et à mon argent et à mon or que je ne lui ai point refusé.
8 Akuluakulu onse ndi anthu onse anayankha kuti, “Musamumvere kapena kuvomereza zofuna zake.”
Et tous les Anciens et tout le peuple lui dirent: N'obéis point et ne consens point!
9 Tsono Ahabu anayankha amithenga a Beni-Hadadi kuti, “Kamuwuzeni mbuye wanga mfumu kuti, ‘Mtumiki wanu adzachita zonse zimene munazifuna nthawi yoyamba ija, koma izi mwazifunazi sindingazikwanitse.’” Iwo anachoka nakapereka yankho kwa Beni-Hadadi.
Il dit donc aux messagers de Ben-Hadad: Dites à mon seigneur le roi: Je ferai tout ce que tu as demandé à ton serviteur en premier lieu, mais ceci, je ne saurais le faire.
10 Pamenepo Beni-Hadadi anatumizanso uthenga wina kwa Ahabu kuti, “Milungu indilange koopsa, ngati mu Samariya mudzakhale fumbi loti nʼkudzaza dzanja la aliyense wa anthu anga.”
Et les messagers partirent et reportèrent la réponse. Alors Ben-Hadad députa vers lui pour lui dire: Qu'ainsi me fassent les dieux et pis encore, si la poussière de Samarie suffit à remplir les mains de tout le monde qui me suit!
11 Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Kamuwuzeni kuti, ‘Mwamuna mnzako nʼpachulu, nʼkulinga utakwerapo.’”
Et le roi d'Israël répondit et dit: Celui qui se ceint ne doit pas se vanter comme celui qui se déceint.
12 Beni-Hadadi anamva uthenga umenewu pamene iye ankamwa ndi mafumu anzake mʼmatenti awo, ndipo analamula anthu ake kuti, “Konzekerani kukathira nkhondo.” Choncho anakonzekera kukathira nkhondo mzindawo.
Et Ben-Hadad entendant cette réponse (or il était à boire avec les rois dans les pavillons) dit à ses serviteurs: Faites les dispositions! Et ils firent les dispositions pour l'assaut de la ville.
13 Ndipo taonani, mneneri wina anabwera kwa Ahabu mfumu ya Israeli nadzalengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi ukuchiona chigulu chachikulu cha ankhondochi? Taona, ndikuchipereka chimenechi lero mʼdzanja lako, ndipo pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Et voilà qu'un prophète s'approcha d'Achab, roi d'Israël, et dit: Ainsi parle l'Éternel: As-tu vu toute cette grande multitude? Eh bien! Je vais aujourd'hui la livrer à tes mains, afin que tu saches que je suis l'Éternel.
14 Ahabu anafunsa kuti, “Koma ndani adzachita zimenezi?” Mneneri anayankha kuti, “Yehova akuti, ‘Adzachita zimenezi ndi asilikali a nduna za mʼzigawo.’” Ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndani adzayambe nkhondoyi?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndinu.”
Et Achab dit: Par qui? Et il reprit: Ainsi parle l'Éternel: Par les valets des chefs des provinces. Et Achab dit: Qui engagera le combat? Et il répondit: Toi.
15 Choncho Ahabu anawerenga asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndipo onse analipo 232. Ndipo anawerenganso ankhondo a ku Israeli ndipo onse analipo 7,000.
Alors il passa en revue les valets des chefs des provinces et il s'en trouva deux cent trente-deux. Et après eux il passa en revue toutes les troupes, tous les enfants d'Israël, au nombre de sept mille.
16 Iwo ananyamuka nthawi yamasana pamene Beni-Hadadi ndi mafumu 32 othandizana naye ankamwa mpaka kuledzera mʼmatenti awo.
Et ils firent leur sortie à midi. Cependant Ben-Hadad buvait à être ivre dans les pavillons avec les trente-deux rois, ses auxiliaires.
17 Asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndiwo amene anayamba kupita ku nkhondo. Nthawi imeneyi Beni-Hadadi nʼkuti atatumiza anthu oti akazonde, amene anadzafotokoza kuti, “Anthu ankhondo akubwera kuchokera ku Samariya.”
Et les valets des chefs des provinces sortirent les premiers. Alors Ben-Hadad fit aller aux informations, et il reçut ce rapport: Des gens ont fait une sortie de Samarie.
18 Iye anati, “Kaya akubwera mwamtendere kapena mwankhondo, muwagwire amoyo.”
Et il dit: S'ils sont sortis pour la paix, saisissez-les vivants, et, s'ils sont sortis pour le combat, saisissez-les vivants.
19 Choncho asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo anatuluka mu mzinda, gulu lankhondo lili pambuyo pawo.
Ceux-là donc sortirent de la place, les valets des chefs des provinces, puis l'armée qui les suivait.
20 Ndipo aliyense wa iwo anapha munthu wake. Ataona izi, Aaramu anathawa Aisraeli ali pambuyo pawo kuwapirikitsa. Koma Beni-Hadadi mfumu ya ku Aaramu anathawa atakwera pa kavalo pamodzi ndi ankhondo ena okweranso pa akavalo.
Et ils battirent chacun son homme, et les Syriens prirent la fuite, et les Israélites les poursuivirent, et Ben-Hadad, roi de Syrie, se sauva sur son cheval avec des cavaliers.
21 Mfumu ya Israeli inapita chitsogolo ndi kugwira akavalo ndi magaleta ndipo Aaramu ambiri anaphedwa.
Et le roi d'Israël se mit en mouvement, et mit en déroute les chevaux et les chars, et fit essuyer aux Syriens une grande défaite.
22 Zitachitika izi, mneneri wina anabwera kwa mfumu ya Israeli ndipo anati, “Mulimbike ndipo muganize bwino zoti mudzachite, chifukwa chaka chikudzachi mfumu ya Aramu idzakuthiraninso nkhondo.”
Alors le prophète s'approcha du roi d'Israël et lui dit: Allons! sois résolu! songe et avise à ce que tu feras; car, au retour de l'année, le roi de Syrie marchera contre toi.
23 Nthawi imeneyi, akuluakulu a mfumu ya Aramu anamulangiza kuti, “Milungu ya anthu a ku Israeli ndi milungu ya mʼmapiri. Nʼchifukwa chake anali ndi mphamvu zotipambana ife. Koma ngati tidzamenyana nawo ku chigwa, ndithudi ife tidzakhala ndi mphamvu kuposa iwo.
Et les serviteurs du roi de Syrie lui dirent: Leurs dieux sont les dieux des montagnes; c'est pourquoi ils l'ont emporté sur nous; mais peut-être nous battant avec eux dans la plaine l'emporterons-nous sur eux.
24 Inu chitani izi: chotsani mafumu onse pa maudindo awo ndipo mʼmalo mwawo muyikemo atsogoleri a ankhondo.
Or, voici ce que tu as à faire: ôte chacun des rois de sa position, et mets les gouverneurs à leur place,
25 Musonkhanitsenso gulu lankhondo lofanana ndi lomwe linaphedwa lija, akavalo monga omwe anaphedwa aja, ndi magaleta monga omwe anawonongedwa aja, kuti tikamenyane ndi Israeli ku chigwa. Pamenepo, ife tidzapambana iwowo.” Beni-Hadadi anagwirizana nawo ndipo anachita momwemo.
et toi, lève une armée égale à celle que tu as perdue, et autant de cavalerie que tu avais de cavalerie, et autant de chars que tu avais de chars, et fais-nous combattre avec eux dans la plaine; peut-être l'emporterons-nous sur eux. Et il écouta leurs avis et fit ainsi.
26 Chaka chinacho Beni-Hadadi anasonkhanitsa Aaramu, napita ku Afeki kukamenyana ndi Israeli.
Et, au retour de l'année, Ben-Hadad passa les Syriens en revue et s'avança jusqu'à Aphek pour se mesurer avec Israël.
27 Aisraeli atasonkhananso, napatsidwa zakudya zawo anapita kukakumana nawo. Aisraeli anamanga misasa yawo moyangʼanana ndi Aaramu ndipo ankaoneka ngati timagulu tiwiri ta mbuzi, pomwe Aaramu anali atakuta dera lonselo.
Et les enfants d'Israël furent aussi passés en revue et avitaillés, et ils marchèrent à leur rencontre, et les enfants d'Israël campèrent en face d'eux, pareils à deux petits troupeaux de chèvres, tandis que les Syriens remplissaient le pays.
28 Munthu wa Mulungu anabwera, nawuza mfumu ya Israeli kuti, “Yehova akuti, ‘Popeza Aaramu akuganiza kuti Yehova ndi mulungu wa ku mapiri, osati wa ku zigwa, Ine ndidzapereka chigulu chonsechi kwa iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Alors l'homme de Dieu s'approcha et parla au roi d'Israël en ces termes: Ainsi parle l'Éternel: Parce que les Syriens ont dit: L'Éternel est Dieu des montagnes, mais non Dieu des vallées, je livrerai toute cette grande multitude-là à tes mains, afin que vous sachiez que je suis l'Éternel.
29 Kwa masiku asanu ndi awiri anakhala moyangʼanana mʼmisasa yawo, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri nkhondo inayambika. Aisraeli anapha Aaramu okwana 100,000 tsiku limodzi lokha.
Et ils furent campés les uns vis-à-vis des autres pendant sept jours, et le septième jour il y eut rencontre en bataille, et les enfants d'Israël tuèrent aux Syriens cent mille hommes de pied en une journée.
30 Ena onse otsala anathawira ku Afeki, kumene khoma linagwera anthu 27,000. Ndipo Beni-Hadadi anathawira mu mzinda, nakabisala mʼchipinda chamʼkati.
Et les survivants s'enfuirent à Aphek dans la ville, et la muraille croula sur vingt-sept mille hommes, les survivants, et Ben-Hadad s'enfuit, et étant entré dans la ville, il allait de chambre en chambre.
31 Atumiki ake anamuwuza kuti, “Taonani, ife tamva kuti mafumu a fuko la Israeli ndi achifundo. Tiyeni tipite kwa mfumu ya ku Israeli titavala ziguduli mʼchiwuno mwathu ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwathu. Mwina iye sakakuphani.”
Alors ses serviteurs lui dirent: Voici, nous avons appris que les rois de la maison d'Israël sont des rois cléments; entourons donc nos reins de cilices et nos têtes de cordes, et présentons-nous au roi d'Israël; peut-être te laissera-t-il la vie.
32 Atavala ziguduli mʼchiwuno mwawo ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwawo, anapita kwa mfumu ya ku Israeli ndipo anayiwuza kuti, “Mtumiki wanu Beni-Hadadi akunena kuti, ‘Chonde loleni kuti ndikhale moyo.’” Mfumu inayankha kuti, “Kodi iye akanali ndi moyo? Iye ujatu ndi mʼbale wanga.”
Et ils ceignirent leurs reins de cilices, et leurs têtes de cordes, et ils parurent devant le roi d'Israël et dirent: Ton serviteur Ben-Hadad dit: Laisse-moi la vie! Et il répondit: Est-il encore vivant? Il est mon frère!
33 Anthuwo ankaganiza kuti mawuwo anali abwino ndipo anavomereza mawuwa mofulumira. Iwo anati, “Inde, Beni-Hadadi ndi mʼbale wanu!” Mfumu inati, “Pitani kamutengeni.” Beni-Hadadi atatuluka, Ahabu anamukweza mʼgaleta lake.
Et ces hommes reçurent cela comme un bon augure, et ils se hâtèrent de le prendre au mot et dirent: Ben-Hadad est donc ton frère! Et il répondit: Venez! amenez-le. Alors Ben-Hadad se présenta à lui et il le fit monter à côté de lui sur son char.
34 Beni-Hadadi anawuza Ahabu kuti, “Ndidzabweza mizinda imene abambo anga analanda abambo anu. Ndipo mutha kumanga nyumba zanu zamalonda mu Damasiko, monga anachitira abambo anga ku Samariya.” Ahabu anati, “Chifukwa cha mgwirizano umenewu, ine ndidzakumasula.” Choncho anachita naye mgwirizano, ndipo anamulola kuti apite.
Et [Ben-Hadad] lui dit: Je te restituerai les villes que mon père a enlevées à ton père, et tu auras tes rues à Damas, comme mon père avait ses rues à Samarie. Et moi [dit Achab], je te laisserai aller sous la foi d'une alliance. Et il lui accorda une capitulation et le laissa partir.
35 Molamulidwa ndi Yehova, mmodzi mwa ana a aneneri anawuza mnzake kuti, “Chonde, menye ndi chida chako,” koma mnzakeyo anakana.
Or, l'un des fils des prophètes dit à son condisciple par ordre de l'Éternel: Bats-moi donc! Mais l'autre refusa de le battre.
36 Choncho mneneriyo anati, “Chifukwa sunamvere Yehova, ukangochoka pano, mkango ukupha.” Ndipo munthuyo atangochoka pamenepo, mkango unamupeza ndi kumupha.
Alors il dit à celui-ci: Parce que tu n'as pas obéi à la voix de l'Éternel, voici, quand tu m'auras quitté, tu seras abattu par le lion. Et quand il l'eut quitté, le lion le rencontra et l'abattit.
37 Mneneriyo anapeza munthu wina ndipo anamuwuza kuti, “Chonde, menye.” Choncho munthuyo anamumenya ndi kumuvulaza.
Et il trouva un autre homme à qui il dit: Bats-moi donc! Et l'homme le battit et le blessa.
38 Pamenepo mneneriyo anapita nakayima pa msewu kudikirira mfumu. Iye anadzibisa nakulunga nsalu nkhope yake.
Alors le prophète alla se placer sur le chemin du roi, et il se déguisa en abaissant son turban sur ses yeux.
39 Mmene mfumu inkadutsa pamenepo, mneneriyo anafuwula kwa mfumuyo kuti, “Ine mtumiki wanu ndinalowa pakati pa nkhondo, ndipo munthu wina anabwera kwa ine atatenga mmodzi mwa anthu ogwidwa pa nkhondo, nandiwuza kuti, ‘Sunga munthu uyu. Ngati asowa, ndiye kuti ndidzakupha, kapena udzalipira ndalama 3,000 za siliva.’
Et au passage du roi il cria vers lui et dit: Ton serviteur faisait son service dans la mêlée du combat, lorsque, voilà qu'un homme tire de côté, m'amenant un homme et me dit: Garde cet homme-ci. S'il vient à manquer, ta vie répondra de sa vie, ou bien tu paieras un talent d'argent.
40 Pamene ine mtumiki wanu ndinali wotanganidwa apa ndi apa, munthuyo anasowa.” Mfumu ya Israeli inati, “Chimenechi ndiye chilango chako. Iwe wadziweruza wekha.”
Et comme ton serviteur était occupé çà et là, l'homme disparut. Et le roi d'Israël lui dit: C'est ton jugement! Tu as décidé toi-même.
41 Pamenepo mneneriyo anachotsa msangamsanga nsalu yomwe anakulunga pa nkhope yake, ndipo mfumu ya Israeli inamuzindikira kuti ndi mmodzi mwa aneneri.
Alors vite il releva son turban de dessus ses yeux, et le roi d'Israël reconnut en lui l'un des prophètes.
42 Iye anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chakuti mwamasula munthu amene Ine ndinati ndi woyenera kuphedwa, inuyo ndi amene mudzaphedwe mʼmalo mwa iyeyo, anthu anu mʼmalo mwa anthu ake.’”
Et il dit au roi: Ainsi parle l'Éternel: Parce que tu as laissé échapper de ta main l'homme que j'avais anathématisé, ta vie répondra de sa vie, et ton peuple, de son peuple.
43 Mwachisoni ndi mokwiya, mfumu ya Israeli inapita ku nyumba yake yaufumu ku Samariya.
Et le roi d'Israël rentra dans sa maison, chagrin et irrité, puis il gagna Samarie.

< 1 Mafumu 20 >