< 1 Mafumu 20 >
1 Tsono Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu inasonkhanitsa magulu ake onse a ankhondo. Iye pamodzi ndi mafumu 32, akavalo awo ndi magaleta awo, anapita kukawuzungulira mzinda wa Samariya ndi kuwuthira nkhondo.
Tedy Benadad král Syrský, shromáždiv všecka vojska svá, a maje s sebou třidceti a dva krále, též koně i vozy, vytáhl a oblehl Samaří a dobýval ho.
2 Iye anatuma amithenga ake mu mzindamo kwa Ahabu mfumu ya Israeli, kukanena kuti,
I poslal posly k Achabovi králi Izraelskému do města,
3 “Beni-Hadadi akuti, ‘Siliva wako ndi golide wako ndi wanga, ndipo akazi ako okongola ndi ana ako ndi anganso.’”
A vzkázal jemu: Takto praví Benadad: Stříbro tvé a zlato tvé mé jest, též ženy tvé i synové tvoji nejzdárnější moji jsou.
4 Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Monga mmene mwanenera, mbuye wanga mfumu, ine pamodzi ndi zonse zomwe ndili nazo ndi zanu.”
I odpověděl král Izraelský a řekl: Vedlé řeči tvé, pane můj králi, tvůj jsem i všecko, což mám.
5 Amithenga aja anabwereranso kwa Ahabu ndipo anamuwuza kuti, “Beni-Hadadi akuti, ‘Ine ndinakulamula kuti undipatse siliva wako ndi golide wako, akazi ako ndi ana ako.
Opět navrátivše se poslové, řekli: Takto praví Benadad: Poslal jsem k tobě, aťby řekli: Stříbro své a zlato své, ženy své i syny své dáš mi.
6 Koma mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzatuma atumiki anga kudzafufuza mʼnyumba yako yaufumu ndi nyumba za akuluakulu ako. Iwo adzatenga chilichonse chimene umachidalira ndi kupita nacho.’”
Ale však o tomto čase zítra pošli služebníky své k tobě, aby přehledali dům tvůj i domy služebníků tvých, a oniť všecko, cožkoli máš nejlepšího, vezmouce v ruce své, poberou.
7 Pamenepo mfumu ya Israeli inayitanitsa akuluakulu a mʼdzikomo niwawuza kuti, “Taonani momwe munthuyu akufunira kutibweretsera mavuto! Atatumiza mawu oti ndimupatse akazi anga ndi ana anga, siliva wanga ndi golide wanga, ine sindinamukanize.”
A tak povolav král Izraelský všech starších země té, řekl: Posuďte medle, a vizte, jakť ten zlého hledá; nebo poslal ke mně pro ženy mé a pro syny mé, též pro stříbro mé i pro zlato mé, a neodepřel jsem jemu.
8 Akuluakulu onse ndi anthu onse anayankha kuti, “Musamumvere kapena kuvomereza zofuna zake.”
I řekli jemu všickni starší a všecken lid: Neposlouchejž ho, ani mu povoluj.
9 Tsono Ahabu anayankha amithenga a Beni-Hadadi kuti, “Kamuwuzeni mbuye wanga mfumu kuti, ‘Mtumiki wanu adzachita zonse zimene munazifuna nthawi yoyamba ija, koma izi mwazifunazi sindingazikwanitse.’” Iwo anachoka nakapereka yankho kwa Beni-Hadadi.
Protož odpověděl poslům Benadadovým: Povězte pánu mému králi: Všecko to, o čež jsi poslal k služebníku svému prvé, učiním, ale této věci učiniti nemohu. Takž odešli poslové, a donesli mu tu odpověd.
10 Pamenepo Beni-Hadadi anatumizanso uthenga wina kwa Ahabu kuti, “Milungu indilange koopsa, ngati mu Samariya mudzakhale fumbi loti nʼkudzaza dzanja la aliyense wa anthu anga.”
Ještě poslal k němu Benadad a řekl: Toto ať mi učiní bohové a toto ať přidadí, dostane-li se prachu Samařského do hrstí všeho lidu, kterýž jest se mnou.
11 Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Kamuwuzeni kuti, ‘Mwamuna mnzako nʼpachulu, nʼkulinga utakwerapo.’”
Zase odpověděl král Izraelský a řekl: Povězte, ať se nechlubí ten, kterýž se strojí do zbroje, jako ten, kterýž svláčí zbroj.
12 Beni-Hadadi anamva uthenga umenewu pamene iye ankamwa ndi mafumu anzake mʼmatenti awo, ndipo analamula anthu ake kuti, “Konzekerani kukathira nkhondo.” Choncho anakonzekera kukathira nkhondo mzindawo.
I stalo se, když uslyšel tu řeč, (nebo pil on i králové v staních), že řekl služebníkům svým: Přitrhněte. I přitrhli k městu.
13 Ndipo taonani, mneneri wina anabwera kwa Ahabu mfumu ya Israeli nadzalengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi ukuchiona chigulu chachikulu cha ankhondochi? Taona, ndikuchipereka chimenechi lero mʼdzanja lako, ndipo pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
A hle, prorok nějaký přišed k Achabovi králi Izraelskému, řekl: Toto praví Hospodin: Zdaliž jsi neviděl všeho množství tohoto velikého? Hle, já dám je dnes v ruku tvou, abys poznal, že já jsem Hospodin.
14 Ahabu anafunsa kuti, “Koma ndani adzachita zimenezi?” Mneneri anayankha kuti, “Yehova akuti, ‘Adzachita zimenezi ndi asilikali a nduna za mʼzigawo.’” Ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndani adzayambe nkhondoyi?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndinu.”
A když řekl Achab: Skrze koho? odpověděl on: Tak praví Hospodin: Skrze služebníky knížat krajů. Řekl ještě: Kdo svede tu bitvu? Odpověděl: Ty.
15 Choncho Ahabu anawerenga asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndipo onse analipo 232. Ndipo anawerenganso ankhondo a ku Israeli ndipo onse analipo 7,000.
A protož sečtl služebníky knížat krajů, jichž bylo dvě stě třidceti a dva; po nich sečtl i všecken lid všech synů Izraelských, sedm tisíců.
16 Iwo ananyamuka nthawi yamasana pamene Beni-Hadadi ndi mafumu 32 othandizana naye ankamwa mpaka kuledzera mʼmatenti awo.
I vytáhli o poledni. Benadad pak pil a ožral se v staních, on i třidceti a dva králové pomocníci jeho.
17 Asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndiwo amene anayamba kupita ku nkhondo. Nthawi imeneyi Beni-Hadadi nʼkuti atatumiza anthu oti akazonde, amene anadzafotokoza kuti, “Anthu ankhondo akubwera kuchokera ku Samariya.”
A tak vytáhli služebníci knížat krajů nejprvé. I poslal Benadad, (když mu pověděli, řkouce: Muži vytáhli z Samaří),
18 Iye anati, “Kaya akubwera mwamtendere kapena mwankhondo, muwagwire amoyo.”
A řekl: Buď že vytáhli o pokoj, zjímejte je živé, buď že k bitvě vytáhli, zjímejte je živé.
19 Choncho asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo anatuluka mu mzinda, gulu lankhondo lili pambuyo pawo.
Tak, pravím, vytáhli z města ti služebníci knížat krajů, a vojsko za nimi táhlo.
20 Ndipo aliyense wa iwo anapha munthu wake. Ataona izi, Aaramu anathawa Aisraeli ali pambuyo pawo kuwapirikitsa. Koma Beni-Hadadi mfumu ya ku Aaramu anathawa atakwera pa kavalo pamodzi ndi ankhondo ena okweranso pa akavalo.
A porazili jeden každý muže svého, tak že utíkali Syrští, Izraelští pak honili je. Ale Benadad král Syrský utekl na koni s jízdnými.
21 Mfumu ya Israeli inapita chitsogolo ndi kugwira akavalo ndi magaleta ndipo Aaramu ambiri anaphedwa.
Potom vytáhl král Izraelský, a pobil koně i vozy zkazil, a tak porazil Syrské ranou velikou.
22 Zitachitika izi, mneneri wina anabwera kwa mfumu ya Israeli ndipo anati, “Mulimbike ndipo muganize bwino zoti mudzachite, chifukwa chaka chikudzachi mfumu ya Aramu idzakuthiraninso nkhondo.”
Opět přišel prorok ten k králi Izraelskému, a řekl jemu: Jdiž, zmužile se měj a věz i viz, co bys měl činiti; nebo zase po roce král Syrský vytáhne proti tobě.
23 Nthawi imeneyi, akuluakulu a mfumu ya Aramu anamulangiza kuti, “Milungu ya anthu a ku Israeli ndi milungu ya mʼmapiri. Nʼchifukwa chake anali ndi mphamvu zotipambana ife. Koma ngati tidzamenyana nawo ku chigwa, ndithudi ife tidzakhala ndi mphamvu kuposa iwo.
Tedy služebníci krále Syrského řekli jemu: Bohové hor jsouť bohové jejich, protož nás přemohli; ale bojujme proti nim na rovinách, zvíš, nepřemůžeme-li jich.
24 Inu chitani izi: chotsani mafumu onse pa maudindo awo ndipo mʼmalo mwawo muyikemo atsogoleri a ankhondo.
Protož učiň toto: Odbuď těch králů, jednoho každého z místa jeho, a postav vývody místo nich.
25 Musonkhanitsenso gulu lankhondo lofanana ndi lomwe linaphedwa lija, akavalo monga omwe anaphedwa aja, ndi magaleta monga omwe anawonongedwa aja, kuti tikamenyane ndi Israeli ku chigwa. Pamenepo, ife tidzapambana iwowo.” Beni-Hadadi anagwirizana nawo ndipo anachita momwemo.
Ty pak sečti sobě vojsko z svých jako vojsko oněch, kteříž padli, a koně jako ony koně, a vozy jako ony vozy; i budeme bojovati proti nim na rovinách, a zvíš, nepřemůžeme-liť jich. I uposlechl hlasu jejich a učinil tak.
26 Chaka chinacho Beni-Hadadi anasonkhanitsa Aaramu, napita ku Afeki kukamenyana ndi Israeli.
I stalo se po roce, že sečtl Benadad Syrské a vytáhl do Afeku, aby bojoval proti Izraelovi.
27 Aisraeli atasonkhananso, napatsidwa zakudya zawo anapita kukakumana nawo. Aisraeli anamanga misasa yawo moyangʼanana ndi Aaramu ndipo ankaoneka ngati timagulu tiwiri ta mbuzi, pomwe Aaramu anali atakuta dera lonselo.
Izraelští také sečteni jsou, a opatřivše se stravou, vytáhli jim v cestu. I položili se Izraelští proti nim jako dvě malá stáda koz, Syrští pak přikryli tu zemi.
28 Munthu wa Mulungu anabwera, nawuza mfumu ya Israeli kuti, “Yehova akuti, ‘Popeza Aaramu akuganiza kuti Yehova ndi mulungu wa ku mapiri, osati wa ku zigwa, Ine ndidzapereka chigulu chonsechi kwa iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
V tom přišel týž muž Boží, a mluvil králi Izraelskému a řekl: Takto praví Hospodin: Proto že pravili Syrští: Bohem hor jest Hospodin a ne Bohem rovin, dám všecko množství toto veliké v ruce tvé, abyste věděli, že já jsem Hospodin.
29 Kwa masiku asanu ndi awiri anakhala moyangʼanana mʼmisasa yawo, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri nkhondo inayambika. Aisraeli anapha Aaramu okwana 100,000 tsiku limodzi lokha.
A tak leželi oni proti nim za sedm dní; i stalo se dne sedmého, že svedli bitvu. I porazili synové Izraelští z Syrských sto tisíc pěších dne jednoho.
30 Ena onse otsala anathawira ku Afeki, kumene khoma linagwera anthu 27,000. Ndipo Beni-Hadadi anathawira mu mzinda, nakabisala mʼchipinda chamʼkati.
Jiní pak zutíkali do města Afeku, kdež padla zed na dvadceti a sedm tisíc mužů, kteříž byli pozůstali. Ale Benadad utíkaje, přišel do města, do nejtajnějšího pokoje.
31 Atumiki ake anamuwuza kuti, “Taonani, ife tamva kuti mafumu a fuko la Israeli ndi achifundo. Tiyeni tipite kwa mfumu ya ku Israeli titavala ziguduli mʼchiwuno mwathu ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwathu. Mwina iye sakakuphani.”
I řekli jemu služebníci jeho: Aj, toto jsme slýchali, že králové domu Izraelského jsou králové milosrdní. Medle, nechť vezmeme pytle na bedra svá a provazy na hlavy své, a vejdeme k králi Izraelskému; snad při životu zachová tebe.
32 Atavala ziguduli mʼchiwuno mwawo ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwawo, anapita kwa mfumu ya ku Israeli ndipo anayiwuza kuti, “Mtumiki wanu Beni-Hadadi akunena kuti, ‘Chonde loleni kuti ndikhale moyo.’” Mfumu inayankha kuti, “Kodi iye akanali ndi moyo? Iye ujatu ndi mʼbale wanga.”
A protož přepásali pytli bedra svá, a provazy vzali na hlavy své, a přišli k králi Izraelskému a řekli: Služebník tvůj Benadad praví: Prosím, nechť jsem zachován při životu. Kterýž řekl: Což jest ještě živ? Bratr tě můj.
33 Anthuwo ankaganiza kuti mawuwo anali abwino ndipo anavomereza mawuwa mofulumira. Iwo anati, “Inde, Beni-Hadadi ndi mʼbale wanu!” Mfumu inati, “Pitani kamutengeni.” Beni-Hadadi atatuluka, Ahabu anamukweza mʼgaleta lake.
Muži pak ti soudíc to za dobré znamení, rychle chytili ta slova od něho a řekli: Bratrť jest tvůj Benadad. I řekl: Jděte, přiveďte ho sem. Takž vyšel k němu Benadad, i kázal mu vstoupiti na svůj vůz.
34 Beni-Hadadi anawuza Ahabu kuti, “Ndidzabweza mizinda imene abambo anga analanda abambo anu. Ndipo mutha kumanga nyumba zanu zamalonda mu Damasiko, monga anachitira abambo anga ku Samariya.” Ahabu anati, “Chifukwa cha mgwirizano umenewu, ine ndidzakumasula.” Choncho anachita naye mgwirizano, ndipo anamulola kuti apite.
Tedy řekl jemu Benadad: Města, kteráž otec můj pobral otci tvému, navrátímť, a ulice zděláš sobě v Damašku, jako byl udělal otec můj v Samaří. I odpověděl: Já vedlé smlouvy této propustím tě. A tak učinil s ním smlouvu a propustil ho.
35 Molamulidwa ndi Yehova, mmodzi mwa ana a aneneri anawuza mnzake kuti, “Chonde, menye ndi chida chako,” koma mnzakeyo anakana.
Muž pak nějaký z synů prorockých řekl bližnímu svému z rozkazu Božího: Ubí mne medle. Ale muž ten nechtěl ho bíti.
36 Choncho mneneriyo anati, “Chifukwa sunamvere Yehova, ukangochoka pano, mkango ukupha.” Ndipo munthuyo atangochoka pamenepo, mkango unamupeza ndi kumupha.
Kterýž řekl jemu: Proto že jsi neuposlechl hlasu Hospodinova, aj teď, když půjdeš ode mne, udáví tě lev. A když šel od něho, trefil na něj lev a udávil ho.
37 Mneneriyo anapeza munthu wina ndipo anamuwuza kuti, “Chonde, menye.” Choncho munthuyo anamumenya ndi kumuvulaza.
Opět nalezl muže druhého, jemuž řekl: Medle, ubí mne. Kterýž ubil ho velice a ranil.
38 Pamenepo mneneriyo anapita nakayima pa msewu kudikirira mfumu. Iye anadzibisa nakulunga nsalu nkhope yake.
I odšed prorok ten, postavil se králi v cestě, a změnil se, zavěsiv sobě oči.
39 Mmene mfumu inkadutsa pamenepo, mneneriyo anafuwula kwa mfumuyo kuti, “Ine mtumiki wanu ndinalowa pakati pa nkhondo, ndipo munthu wina anabwera kwa ine atatenga mmodzi mwa anthu ogwidwa pa nkhondo, nandiwuza kuti, ‘Sunga munthu uyu. Ngati asowa, ndiye kuti ndidzakupha, kapena udzalipira ndalama 3,000 za siliva.’
A když král pomíjel, zvolal na něj a řekl: Služebník tvůj vyšel do bitvy, a hle, jeden odšed, přivedl ke mně muže a řekl: Ostříhej toho muže, jestliže se pak ztratí, budeť život tvůj za život jeho, aneb centnéř stříbra položíš.
40 Pamene ine mtumiki wanu ndinali wotanganidwa apa ndi apa, munthuyo anasowa.” Mfumu ya Israeli inati, “Chimenechi ndiye chilango chako. Iwe wadziweruza wekha.”
V tom když služebník tvůj toho i onoho hleděl, tožť se ztratil. Pročež řekl jemu král Izraelský: Takový buď soud tvůj, jakýž jsi sám vypověděl.
41 Pamenepo mneneriyo anachotsa msangamsanga nsalu yomwe anakulunga pa nkhope yake, ndipo mfumu ya Israeli inamuzindikira kuti ndi mmodzi mwa aneneri.
Tedy rychle odhradil tvář svou, a poznal ho král Izraelský, že by z proroků byl.
42 Iye anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chakuti mwamasula munthu amene Ine ndinati ndi woyenera kuphedwa, inuyo ndi amene mudzaphedwe mʼmalo mwa iyeyo, anthu anu mʼmalo mwa anthu ake.’”
I řekl jemu: Takto praví Hospodin: Poněvadž jsi z ruky pustil muže k smrti odsouzeného, budeť život tvůj za život jeho, a lid tvůj za lid jeho.
43 Mwachisoni ndi mokwiya, mfumu ya Israeli inapita ku nyumba yake yaufumu ku Samariya.
Protož odjel král Izraelský do domu svého, smutný jsa a hněvaje se, a přišel do Samaří.