< 1 Mafumu 2 >

1 Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
Insuku zikaDavida zokuthi afe zasezisondela, waselaya uSolomoni indodana yakhe esithi:
2 “Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
Sengihamba indlela yomhlaba wonke. Ngakho qina, ube yindoda,
3 ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
ugcine imfanelo yeNkosi uNkulunkulu wakho, ukuhamba ngezindlela zayo, ukugcina izimiso zayo, imithetho yayo, lezahlulelo zayo, lobufakazi bayo, njengokubhaliweyo emlayweni kaMozisi, ukuze uphumelele kukho konke okwenzayo, laloba ngaphi lapho ophendukela khona,
4 Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
ukuze iNkosi iqinise ilizwi layo eyalikhuluma mayelana lami isithi: Uba amadodana akho eqaphelisa indlela yawo, ukuhamba ngobuqotho phambi kwami ngenhliziyo yonke yawo langomphefumulo wonke wawo, (isithi) kakuyikusweleka kuwe indoda esihlalweni sobukhosi sikaIsrayeli.
5 “Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
Futhi-ke wena uyakwazi ukuthi uJowabi indodana kaZeruya wenzani kimi, ukuthi wenzani kuzinduna ezimbili zamabutho akoIsrayeli, kuAbhineri indodana kaNeri, lakuAmasa indodana kaJetheri, owababulala wachitha igazi lempi ekuthuleni, wafaka igazi lempi ebhantini lakhe elalisekhalweni lwakhe lemanyathelweni asenyaweni zakhe.
6 Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
Ngakho yenza njengenhlakanipho yakho, ungayekeli ikhanda lakhe elilezimvu lehlele engcwabeni ngokuthula. (Sheol h7585)
7 “Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
Kodwa kumadodana kaBarizilayi umGileyadi wenze umusa, njalo kawabe phakathi kwabadla etafuleni lakho, ngoba ngokunjalo asondela kimi ekubalekeleni kwami ubuso bukaAbisalomu umfowenu.
8 “Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
Futhi khangela, kukhona kuwe uShimeyi indodana kaGera umBhenjamini weBahurimi, owangithuka ngesethuko esibuhlungu mhla ngisiya eMahanayimi; kodwa wehla ukungihlangabeza eJordani, ngasengifunga kuye ngeNkosi ngathi: Kangiyikukubulala ngenkemba.
9 Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
Ngakho-ke ungamyekeli abe ngongelacala, ngoba ungumuntu ohlakaniphileyo, ngoba uyakwazi ozakwenza kuye, njalo uzakwehlisela ikhanda lakhe eliyimpunga lilegazi engcwabeni. (Sheol h7585)
10 Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
UDavida waselala laboyise, wangcwatshelwa emzini kaDavida.
11 Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
Njalo insuku uDavida abusa ngazo phezu kukaIsrayeli zaziyiminyaka engamatshumi amane; eHebroni wabusa iminyaka eyisikhombisa, leJerusalema wabusa iminyaka engamatshumi amathathu lantathu.
12 Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
USolomoni wasehlala esihlalweni sobukhosi sikaDavida uyise, lombuso wakhe waqiniswa kakhulu.
13 Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
UAdonija indodana kaHagithi wasesiza kuBathisheba unina kaSolomoni; wasesithi: Ukuza kwakho kuyikuthula yini? Wasesithi: Ukuthula.
14 Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
Wathi: Ngilelizwi kuwe. Wasesithi: Khuluma.
15 Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
Wasesithi: Wena uyakwazi ukuthi umbuso wawungowami, lokuthi uIsrayeli wonke babebeke ubuso babo kimi ukuthi ngizabusa; kodwa umbuso waphendulwa, waba ngowomfowethu, ngoba waba ngowakhe uvela eNkosini.
16 Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
Khathesi-ke, ngicela isicelo esisodwa kuwe, ungafulathelisi ubuso bami. Wasesithi kuye: Khuluma.
17 Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
Wasesithi: Ake ukhulume loSolomoni inkosi (ngoba kayikufulathelisa ubuso bakho) ukuthi anginike uAbishagi umShunami abe ngumkami.
18 Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
UBathisheba wasesithi: Kulungile; mina ngizakukhulumela enkosini.
19 Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
Ngakho uBathisheba wasesiya enkosini uSolomoni ukukhulumela uAdonija kuyo. Inkosi yasisukuma ukumhlangabeza, yakhothama kuye, yahlala esihlalweni sayo sobukhosi, yathi kubekelwe unina wenkosi isihlalo sobukhosi; wasehlala ngakwesokunene sayo.
20 Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
Wasesithi: Ngicela isicelo esisodwa esincinyane kuwe, ungafulathelisi ubuso bami. Inkosi yasisithi kuye: Cela, mama, ngoba kangiyikufulathelisa ubuso bakho.
21 Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
Wasesithi: UAbishagi umShunami kanikwe uAdonija umfowenu abe ngumkakhe.
22 Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
Inkosi uSolomoni yasiphendula yathi kunina: Usumcelelelani uAdonija uAbishagi umShunami? Umcelele lombuso, ngoba ungumfowethu omdala kulami, yebo yena loAbhiyatha umpristi loJowabi indodana kaZeruya.
23 Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
Inkosi uSolomoni yasifunga ngeNkosi isithi: Kenze njalo uNkulunkulu kimi lokunjalo engezelele, uba uAdonija engakhulumanga lelilizwi emelene lempilo yakhe.
24 Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
Ngakho-ke, kuphila kukaJehova ongimisileyo wangibeka esihlalweni sobukhosi sikaDavida ubaba, wangenzela indlu njengokukhuluma kwakhe, isibili lamuhla uAdonija uzabulawa.
25 Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
Inkosi uSolomoni yasithuma ngesandla sikaBhenaya indodana kaJehoyada, owamsukelayo, wasesifa.
26 Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
LakuAbhiyatha umpristi inkosi yathi: Yana eAnathothi emasimini akho, ngoba ungumuntu wokufa; kodwa lamuhla kangiyikukubulala ngoba wawuthwala umtshokotsho weNkosi uJehova phambi kukaDavida ubaba, langoba wahlupheka kukho konke ubaba ahlupheka ngakho.
27 Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
Ngakho uSolomoni wamxotsha uAbhiyatha ekubeni ngumpristi weNkosi, ukugcwalisa ilizwi leNkosi eyalikhuluma mayelana lendlu kaEli eShilo.
28 Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
Kwathi umbiko ufika kuJowabi, ngoba uJowabi wayephenduke walandela uAdonija lanxa wayengaphendukanga walandela uAbisalomu, uJowabi wabalekela ethenteni leNkosi, wabamba impondo zelathi.
29 Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
Kwasekubikelwa inkosi uSolomoni ukuthi uJowabi usebalekele ethenteni leNkosi, khangela-ke, useceleni kwelathi. USolomoni wasethuma uBhenaya indodana kaJehoyada esithi: Hamba umsukele.
30 Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
Ngakho uBhenaya waya ethenteni leNkosi, wathi kuye: Itsho njalo inkosi: Phuma! Kodwa wathi: Hatshi, kodwa ngizafela lapha. UBhenaya wasebuyisela ilizwi enkosini, esithi: Utsho njalo uJowabi, ungiphendule njalo.
31 Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
Inkosi yasisithi kuye: Yenza njengokutsho kwakhe, umsukele, umngcwabe; ukuze ususe kimi lendlini kababa igazi elingelacala uJowabi alichithayo.
32 Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
Njalo iNkosi izabuyisela igazi lakhe ekhanda lakhe, owasukela amadoda amabili ayelungile engcono kulaye, wawabulala ngenkemba, ubaba uDavida engazi: UAbhineri indodana kaNeri induna yebutho lakoIsrayeli, loAmasa indodana kaJetheri induna yebutho lakoJuda.
33 Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
Ngakho igazi labo lizabuyela ekhanda likaJowabi lekhanda lenzalo yakhe kuze kube nininini; kodwa kuDavida lenzalweni yakhe, lendlini yakhe, lembusweni wakhe, kuzakuba lokuthula kuze kube nininini okuvela eNkosini.
34 Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
UBhenaya indodana kaJehoyada wasesenyuka, wamsukela wambulala; wasengcwatshelwa endlini yakhe enkangala.
35 Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
Inkosi yasibeka uBhenaya indodana kaJehoyada esikhundleni sakhe phezu kwebutho, loZadoki umpristi inkosi yambeka esikhundleni sikaAbhiyatha.
36 Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
Inkosi yasithuma yabiza uShimeyi, yathi kuye: Zakhele indlu eJerusalema, uhlale khona, ungaphumi lapho uye ngaphi langaphi.
37 Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
Ngoba kuzakuthi mhla uphumayo, uchaphe isifula iKidroni, yazi lokwazi ukuthi uzakufa lokufa; igazi lakho lizakuba phezu kwekhanda lakho.
38 Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
UShimeyi wasesithi enkosini: Lelolizwi lihle; njengokutsho kwenkosi yami, inkosi, inceku yakho izakwenza njalo. UShimeyi wasehlala eJerusalema insuku ezinengi.
39 Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
Kwasekusithi ekupheleni kweminyaka emithathu inceku ezimbili zikaShimeyi zabalekela kuAkishi indodana kaMahaka inkosi yeGathi. Basebebikela uShimeyi besithi: Khangela, inceku zakho ziseGathi.
40 Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
Wasesukuma uShimeyi, wabophela isihlalo kubabhemi wakhe, waya eGathi kuAkishi ukudinga inceku zakhe; uShimeyi wahamba waletha inceku zakhe zivela eGathi.
41 Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
Kwasekubikelwa uSolomoni ukuthi uShimeyi wayesukile eJerusalema waya eGathi, njalo wabuyela.
42 mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
Inkosi yasithuma yabiza uShimeyi yathi kuye: Kangikufungisanga yini ngeNkosi, ngafakaza kuwe ngathi: Mhla uphumayo ukuya ngaphi langaphi yazi lokwazi ukuthi uzakufa lokufa? Wasusithi kimi: Lihle ilizwi engilizwileyo.
43 Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
Pho, kungani ungasigcinanga isifungo seNkosi lomlayo engakulaya ngawo?
44 Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
Inkosi yasisithi kuShimeyi: Wena uyazi bonke ububi inhliziyo yakho ebaziyo owabenza kuDavida ubaba; ngakho iNkosi izabuyisela ububi bakho phezu kwekhanda lakho.
45 Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
Kodwa inkosi uSolomoni ibusisiwe, lesihlalo sobukhosi sikaDavida sizaqiniswa phambi kweNkosi kuze kube nininini.
46 Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.
Ngakho inkosi yalaya uBhenaya indodana kaJehoyada, owaphuma wamsukela waze wafa. Ngakho umbuso waqiniswa esandleni sikaSolomoni.

< 1 Mafumu 2 >