< 1 Mafumu 2 >

1 Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
Kad su se dani Davidovi približavali svome svršetku, zapovjedi David svome sinu Salomonu:
2 “Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
“Sada polazim na put sviju smrtnika. Ti budi hrabar i pokaži se čovjekom!
3 ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
Slušaj naredbe Jahve, Boga svoga, idi njegovim stazama, drži se njegovih zakona, zapovijedi, naredaba i njegovih pouka, kako je napisano u Zakonu Mojsijevu, da bi uspio u svemu što poduzmeš i svagdje kamo se okreneš;
4 Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
da bi Jahve ispunio svoje obećanje koje mi je dao: 'Ako sinovi tvoji budu pazili na svome putu, vjerno hodeći preda mnom, svim srcem svojim i svom dušom svojom, uvijek će jedan od njih sjediti na prijestolju Izraelovu.'
5 “Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
I sam znaš što mi je učinio Joab, sin Sarvijin, kako je učinio obojici vojskovođa Izraelovih: Abneru, sinu Nerovu, i Amasi, sinu Jeterovu, kad ih je ubio i time prolio krv u miru kao u ratu te omastio krvlju pojas oko bokova svojih i obuću na nogama svojim.
6 Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
Ti postupi po svom razboru i ne daj da mu sijeda kosa mirno počine u Podzemlju. (Sheol h7585)
7 “Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
A sinovima Barzilaja Gileađanina vrati ljubav: neka budu među onima koji jedu za tvojim stolom jer su mi pomogli kad sam bježao pred tvojim bratom Abšalomom.
8 “Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
Pred sobom imaš Šimeja, sina Gerina, Benjaminovca iz Bahurima, koji me užasnim kletvama proklinjao onoga dana kad sam bježao u Mahanajim. Ali mi je on sišao u susret na Jordan i zakleh mu se Jahvom: 'Neću te pogubiti mačem.'
9 Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
Ali mu ti toga ne opraštaj, jer si čovjek razborit, i već ćeš znati kako treba da postupiš te mu sijedu kosu s krvlju u Podzemlje spremiš.” (Sheol h7585)
10 Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
I potom počinu David kraj otaca svojih i bi pokopan u Davidovu gradu.
11 Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
David je kraljevao nad Izraelom četrdeset godina: u Hebronu je kraljevao sedam godina, u Jeruzalemu je kraljevao trideset i tri godine.
12 Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
Salomon sjede na prijestolje Davida, svoga oca, i njegova se vlast veoma učvrsti.
13 Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
Ali Adonija, sin Hagitin, dođe Bat-Šebi, majci Salomonovoj, i pade ničice pred njom. Ona ga upita: “Je li miroljubiv tvoj dolazak?” On odgovori: “Jest, miroljubiv je.”
14 Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
I nastavi: “Imam ti nešto reći.” Ona reče: “Govori.”
15 Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
Tada će on: “Znaš i sama da je kraljevstvo pripadalo meni i da je sav Izrael očekivao da ću ja biti kralj. Ali mi je kraljevstvo izmaklo i pripalo je mome bratu, jer mu ga je Jahve namijenio.
16 Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
Ja te sada samo jedno molim: nemoj me odbiti.” Ona reče: “Govori.”
17 Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
A on nastavi: “Reci, molim te, kralju Salomonu - jer tebe neće odbiti - neka mi dade za ženu Abišagu Šunamku!”
18 Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
A Bat-Šeba odgovori: “Dobro, govorit ću kralju o tebi.”
19 Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
Kada dakle uđe Bat-Šeba kralju Salomonu da govori o Adoniji, ustade kralj i pođe joj u susret, pokloni se pred njom, zatim sjede na svoje prijestolje i zapovjedi te namjestiše sjedalicu za kraljicu majku, i ona mu sjede s desne strane.
20 Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
Tada mu reče: “Nešto bih zaiskala od tebe, nemoj me odbiti.” Kralj joj odgovori: “Traži, majko, jer te neću odbiti.”
21 Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
Ona nastavi: “Neka se dade Abišaga Šunamka tvome bratu Adoniji za ženu.”
22 Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
Kralj Salomon odgovori i reče svojoj majci: “Zašto tražiš Abišagu Šunamku za Adoniju? Traži odmah i kraljevstvo za njega! Jer on je moj stariji brat, a uz njega je svećenik Ebjatar i Joab, sin Sarvijin!”
23 Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
Tada se kralj Salomon zakle Jahvom: “Neka mi Bog učini ovo zlo i neka mi doda drugo ako Adonija nije to izrekao danas po cijenu svoga života!
24 Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
Živoga mi Jahve, koji me potvrdio i posadio na prijestolje oca moga Davida i koji mi je dao dom kako je obećao: još danas će Adonija umrijeti.”
25 Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
I kralj Salomon posla Benaju, sina Jojadina, koji ga udari te Adonija umrije.
26 Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
Svećeniku Ebjataru kralj zatim naredi: “Idi u Anatot na svoj posjed. Zaslužio si smrt, ali te neću pogubiti danas jer si nosio Jahvin Kovčeg pred ocem mojim Davidom i podijelio si sve patnje s mojim ocem.”
27 Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
I Salomon isključi Ebjatara iz svećenstva Jahvina da tako ispuni Jahvinu riječ koju je izrekao protiv doma Elijeva u Šilu.
28 Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
Kada je glas stigao Joabu - Joab bijaše pristao uz Adoniju, premda se nije priključio Abšalomu - on uteče u Šator Jahvin i uhvati se za rogove žrtvenika.
29 Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
I dojaviše kralju Salomonu: “Joab je pobjegao u Šator Jahvin, eno ga pokraj žrtvenika.” Tada Salomon poruči Joabu: “Što se držiš žrtvenika?” Joab odgovori: “Uplašio sam se tebe i pobjegao sam pred Jahvu.” Tada Salomon naredi Benaji, sinu Jojadinu: “Idi i ubij ga!”
30 Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
Benaja ode u Šator Jahvin i reče Joabu: “Po naredbi kraljevoj: iziđi!” On odgovori: “Neću, želim ovdje umrijeti!” Benaja javi kralju: “Eto što mi je rekao Joab i što mi je odgovorio.”
31 Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
Kralj mu reče: “Učini kako je rekao: ubij ga, zatim pokopaj. Tako ćeš danas skinuti s mene i doma oca moga nevinu krv koju je Joab prolio.
32 Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
Jahve će učiniti da krv njegova padne na njegovu glavu, jer je ubio dva čovjeka pravednika i bolja od sebe; ubio ih je mačem bez znanja moga oca Davida: Abnera, sina Nerova, vođu vojske Izraelove, i Amasu, sina Jeterova, vojvodu judejskoga.
33 Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
Neka njihova krv padne na glavu Joaba i njegova potomstva dovijeka, a Davidu, njegovu potomstvu, vladalačkoj kući i prijestolju neka od Jahve bude trajan mir.”
34 Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
I ode Benaja, sin Jojadin, obori se na Joaba i usmrti ga. Pokopali su Joaba u njegovu domu u pustinji.
35 Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
Mjesto njega postavi kralj na čelo vojske Benaju, sina Jojadina, a na mjesto Ebjatara postavi svećenika Sadoka.
36 Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
Salomon pozva Šimeja i reče mu: “Sagradi sebi kuću u Jeruzalemu: tu stanuj, i nikamo odatle ne izlazi.
37 Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
Onoga dana kad iziđeš i prijeđeš potok Kidron, znaj dobro da ćeš umrijeti. Krv tvoja na glavu tvoju.”
38 Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
Šimej odgovori kralju: “Dobro. Kako moj gospodar kralj kaže, tako će učiniti sluga tvoj.” I Šimej dugo življaše u Jeruzalemu.
39 Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
Ali poslije tri godine dogodi se te Šimeju pobjegoše dvojica slugu k Akišu, sinu Maakinu, kralju gatskom. I dojaviše Šimeju: “Eno ti slugu u Gatu.”
40 Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
Tada usta Šimej, osedla magarca i ode u Gat, k Akišu, da traži svoje sluge. I vratio se Šimej i doveo svoje sluge iz Gata.
41 Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
I javiše Salomonu: “Šimej otišao iz Jeruzalema u Gat i vratio se.”
42 mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
Kralj pozva Šimeja i reče mu: “Nisam li ti se zakleo Jahvom i strogo te opomenuo: 'Onoga dana kad budeš izišao i pošao bilo kamo, znaj dobro da ćeš umrijeti!' A ti si mi tada odgovorio: 'Dobra je riječ koju sam čuo.'
43 Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
Zašto nisi održao zakletvu Jahvinu i zapovijed koju sam ti dao?”
44 Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
Još reče kralj Šimeju: “Ti znaš sve zlo koje si učinio mome ocu Davidu. Tvoje je srce toga svjesno. Jahve neka učini da se tvoja zloća obori na tvoju glavu.
45 Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
A blagoslovljen je kralj Salomon, i prijestolje će Davidovo biti čvrsto pred Jahvom dovijeka.”
46 Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.
I zapovjedi kralj Benaji, sinu Jojadinu, te on iziđe i udari Šimeja i tako Šimej umrije. Tako se učvrstilo kraljevstvo u ruci Salomonovoj.

< 1 Mafumu 2 >