< 1 Mafumu 19 >

1 Tsono Ahabu anawuza Yezebeli zonse zimene anachita Eliya ndi momwe anaphera aneneri onse ndi lupanga.
Or Achab annonça à Jézabel tout ce qu’avait fait Elie, et de quelle manière il avait tué par le glaive tous les prophètes.
2 Choncho Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya kuti akamuwuze kuti, “Milungu indilange, ndipo indilange koopsa, ngati mawa nthawi ngati yomwe ino sindidzakupha iwe monga unaphera aneneriwo.”
Et Jézabel envoya un messager à Elie, disant: Que les dieux me fassent ceci, et qu’ils ajoutent cela, si demain à cette heure, je ne mets ton âme comme l’âme de chacun d’eux!
3 Eliya ataona zimenezi, ananyamuka nathawa kupulumutsa moyo wake. Atafika ku Beeriseba ku Yuda, anasiya mtumiki wake kumeneko,
Elie craignit donc, et, se levant, il s’en alla partout où le portait son désir; or il vint à Bersabée en Juda, et là il renvoya son serviteur,
4 ndipo Eliyayo anayenda ulendo wa tsiku limodzi mʼchipululu. Anafika pa kamtengo ka tsache, nakhala pansi pa tsinde lake napemphera kuti afe. Iye anati, “Yehova, ine ndatopa nazo. Chotsani moyo wanga. Ineyo sindine wopambana makolo anga.”
Et il fit dans le désert le chemin d’une journée. Or lorsqu’il fut venu, et qu’il se fut assis sous un genièvre, il demanda pour son âme de mourir, et il dit: C’est assez pour moi. Seigneur, prenez mon âme; car je ne suis pas meilleur que mes pères.
5 Ndipo Eliya anagona tulo tofa nato pa tsinde pa kamtengoko. Ndipo taonani, mngelo anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye.”
Et il se jeta parterre, et s’endormit à l’ombre du genièvre; et voilà qu’un ange du Seigneur le toucha, et lui dit: Lève-toi, et mange.
6 Eliya anayangʼana, ndipo taonani kumutu kwake kunali buledi wootcha pa makala ndi botolo la madzi. Iye anadya ndi kumwa, nʼkugonanso.
Il regarda, et voilà auprès de sa tête un pain cuit sous la cendre et un vase d’eau; il mangea donc et but, et de nouveau il s’endormit.
7 Mngelo wa Yehova anabweranso kachiwiri, anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye, popeza ulendowu ndi wautali.”
Et l’ange du Seigneur revint une seconde fois, le toucha, et lui dit: Lève-toi, et mange; car il te reste un grand chemin.
8 Tsono Eliya anadzuka nadya ndi kumwa. Atapeza mphamvu chifukwa cha chakudyacho, anayenda masiku 40, usana ndi usiku mpaka anafika ku Horebu, phiri la Mulungu.
Et, lorsqu’il se fut levé, il mangea et but; et il marcha, fortifié par cette nourriture, quarante jours et quarante nuits, jusqu’à Horeb, la montagne de Dieu.
9 Kumeneko analowa mʼphanga, nakhala komweko. Ndipo taonani, Yehova anayankhula naye kuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
Or, lorsqu’il fut arrivé là, il demeura dans la caverne; et voilà que la parole du Seigneur lui fut adressée, et lui dit: Que fais-tu ici, Elie?
10 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
Or lui répondit: Je brûle d’un grand zèle pour vous, Seigneur Dieu des armées, parce que les enfants d’Israël ont abandonné votre alliance; ils ont détruit vos autels, ils ont tué vos prophètes par le glaive, et je suis resté moi seul, et ils cherchent mon âme pour la détruire.
11 Yehova anati, “Tuluka ndipo ukayime pa phiri pamaso pa Yehova, pakuti Yehova ali pafupi kudutsa pamenepo.” Tsono mphepo yayikulu ndi yamphamvu inawomba ningʼamba mapiri ndi kuswa matanthwe pamaso pa Yehova, koma Yehova sanali mʼmphepomo. Itapita mphepoyo panachita chivomerezi, koma Yehova sanali mʼchivomerezicho.
Alors le Seigneur lui dit: Sors, et tiens-toi sur la montagne devant le Seigneur: et voilà que le Seigneur passa, et un vent violent et impétueux renversant des montagnes et brisant des rochers devant le Seigneur, et le Seigneur n’était point dans le vent; et après le vent, un tremblement de terre, et le Seigneur n’était pas dans le tremblement;
12 Chitapita chivomerezicho, panafika moto, koma Yehova sanali mʼmotomo. Ndipo utapita motowo, panamveka kamphepo kayaziyazi.
Et après le tremblement, un feu, et le Seigneur n’était point dans le feu; et après le feu, vint le souffle d’une brise légère.
13 Eliya atamva kamphepoko, anakokera chovala chake naphimba kumutu. Anatuluka ndipo anayima pa khomo la phanga. Ndipo panamveka mawu akuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
Ce qu’ayant entendu. Elie couvrit son visage de son manteau, et étant sorti, il se tint à l’entrée de la caverne; et voilà qu’une voix vint à lui, disant: Que fais-tu là, Elie? Et lui répondit:
14 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
Je brûle d’un grand zèle pour vous. Seigneur Dieu des armées, parce que les enfants d’Israël ont abandonné votre alliance; ils ont détruit vos autels, ils ont tué vos prophètes par le glaive, et je suis resté moi seul, et ils cherchent mon âme pour la détruire.
15 Yehova anati kwa Eliyayo, “Bwerera njira imene unadzera, ndipo upite ku Chipululu cha ku Damasiko. Ukakafika kumeneko, ukadzoze Hazaeli kuti akhale mfumu ya ku Aramu.
Et le Seigneur lui dit: Va, et retourne en ta voie par le désert, à Damas; et, lorsque tu y seras arrivé, tu oindras Hazaël roi sur la Syrie.
16 Ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi kuti akhale mfumu ya Israeli, ndiponso ukadzoze Elisa mwana wa Safati wa ku Abeli-Mehola kuti akhale mneneri wolowa mʼmalo mwako.
Tu oindras encore Jéhu, fils de Namsi, roi sur Israël; mais Elisée, fils de Saphat, qui est d’Abelméhula, tu l’oindras prophète en ta place.
17 Yehu adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Hazaeli, ndipo Elisa adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Yehu.
Et il adviendra que quiconque aura échappé au glaive d’Hazaël, Jéhu le tuera; et quiconque aura échappé au glaive de Jéhu, Elisée le tuera.
18 Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.”
Et je me réserverai dans Israël sept mille hommes dont les genoux n’ont pas fléchi devant Baal, et toute bouche qui ne l’a pas adoré en baisant ses mains.
19 Kotero Eliya anachoka kumeneko, nakapeza Elisa mwana wa Safati. Iye ankatipula ndi mapulawo khumi ndi awiri okokedwa ndi ngʼombe ziwiriziwiri zapamagoli, ndipo iye mwini ankayendetsa goli la khumi ndi chiwiri. Eliya anapita kumene anali namuveka chofunda chake.
Etant donc parti de là, Elie trouva Elisée, fils de Saphat, qui labourait avec douze paires de bœufs; et lui-même était un de ceux qui labouraient avec les douze paires de bœufs. Et lorsqu’il fut venu vers Elisée, il jeta son manteau sur lui.
20 Pomwepo Elisa anasiya ngʼombe zake nathamangira Eliya. Iye anati, “Mundilole kuti ndikatsanzike abambo ndi amayi anga, ndipo kenaka ndidzakutsatani.” Eliya anayankha kuti, “Bwerera. Ine ndachita chiyani kwa iwe?”
Elisée aussitôt, ses bœufs abandonnés, courut après Elie, et dit: Que j’embrasse, je vous prie, mon père et ma mère, et alors je vous suivrai. Et il lui répondit: Va, et reviens; car j’ai fait pour toi ce que j’avais à faire.
21 Choncho Elisa anamusiya Eliyayo nabwerera kwawo. Anatenga ngʼombe zake ziwiri zapagoli nazipha. Anatenga magoli a mapulawo ake nasonkhera moto kuphikira nyamayo ndipo anayipereka kwa anthu kuti adye. Ndipo ananyamuka natsatira Eliya ndi kukhala mtumiki wake.
Elisée, ayant quitté Elie, prit une paire de bœufs et les tua; et avec la charrue des bœufs il fit cuire la chair, et la donna au peuple, et ils mangèrent; alors, se levant, il s’en alla, suivit Elie; et il le servait.

< 1 Mafumu 19 >