< 1 Mafumu 19 >

1 Tsono Ahabu anawuza Yezebeli zonse zimene anachita Eliya ndi momwe anaphera aneneri onse ndi lupanga.
When Ahab got home, he told [his wife] Jezebel what Elijah had done. He told her that Elijah had killed all the prophets of Baal.
2 Choncho Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya kuti akamuwuze kuti, “Milungu indilange, ndipo indilange koopsa, ngati mawa nthawi ngati yomwe ino sindidzakupha iwe monga unaphera aneneriwo.”
So Jezebel sent this message to Elijah: “By this time tomorrow I will have [killed] you, just like you [killed all those prophets of Baal]. If I do not do that, I hope the gods will kill me.”
3 Eliya ataona zimenezi, ananyamuka nathawa kupulumutsa moyo wake. Atafika ku Beeriseba ku Yuda, anasiya mtumiki wake kumeneko,
When Elijah received [her message], he was afraid. So [taking his servant with him], he fled in order that he would not be killed. He went [far south] to Beersheba, in Judah. He left his servant there.
4 ndipo Eliyayo anayenda ulendo wa tsiku limodzi mʼchipululu. Anafika pa kamtengo ka tsache, nakhala pansi pa tsinde lake napemphera kuti afe. Iye anati, “Yehova, ine ndatopa nazo. Chotsani moyo wanga. Ineyo sindine wopambana makolo anga.”
Then he went by himself further [south] into the desert. He walked all day. He sat down under a broom tree and prayed that [Yahweh] would allow him to die. He said, “Yahweh, I’ve had enough. So allow me to die, because for me to live is no better than [being with] my ancestors [who have died].”
5 Ndipo Eliya anagona tulo tofa nato pa tsinde pa kamtengoko. Ndipo taonani, mngelo anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye.”
Then he lay down under the broom tree and slept. But while he was sleeping, an angel touched him and [woke him up and] said to him, “Get up and eat some food!”
6 Eliya anayangʼana, ndipo taonani kumutu kwake kunali buledi wootcha pa makala ndi botolo la madzi. Iye anadya ndi kumwa, nʼkugonanso.
Elijah looked around and saw some bread which had been baked on hot stones, and he also saw a jar of water. So he ate some bread and drank some water and lay down [to sleep] again.
7 Mngelo wa Yehova anabweranso kachiwiri, anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye, popeza ulendowu ndi wautali.”
Then the angel [who had been sent by] Yahweh came again and touched him, and said, “Get up and eat some [more] food, because you need [more strength] to go on a long journey.”
8 Tsono Eliya anadzuka nadya ndi kumwa. Atapeza mphamvu chifukwa cha chakudyacho, anayenda masiku 40, usana ndi usiku mpaka anafika ku Horebu, phiri la Mulungu.
So he got up and ate and drank some more, and because of doing that, he got enough strength to enable him to travel for forty days and nights to Sinai Mountain, the mountain [that was dedicated to] God.
9 Kumeneko analowa mʼphanga, nakhala komweko. Ndipo taonani, Yehova anayankhula naye kuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
He went into a cave there and slept there that night. [The next morning, ] Yahweh said to him “Elijah, why are you here?”
10 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
Elijah replied, “I have zealously served you, Yahweh, God Almighty. But the Israeli people have broken the agreement that they made with you. They have torn down your altars, and they have killed all of your prophets. I am the only one whom they have not killed, and now they are trying to kill me, too. [So I am running away from them].”
11 Yehova anati, “Tuluka ndipo ukayime pa phiri pamaso pa Yehova, pakuti Yehova ali pafupi kudutsa pamenepo.” Tsono mphepo yayikulu ndi yamphamvu inawomba ningʼamba mapiri ndi kuswa matanthwe pamaso pa Yehova, koma Yehova sanali mʼmphepomo. Itapita mphepoyo panachita chivomerezi, koma Yehova sanali mʼchivomerezicho.
Yahweh said to him, “Go out and stand in front of me on this mountain while I pass by.” [Suddenly] a strong windstorm struck the mountain. As a result, rocks were loosened from the mountainside. But Yahweh was not in the wind. Then there was an earthquake, but Yahweh was not in the earthquake.
12 Chitapita chivomerezicho, panafika moto, koma Yehova sanali mʼmotomo. Ndipo utapita motowo, panamveka kamphepo kayaziyazi.
Then there was a fire, but Yahweh was not in the fire. Then there was a sound like someone whispering quietly.
13 Eliya atamva kamphepoko, anakokera chovala chake naphimba kumutu. Anatuluka ndipo anayima pa khomo la phanga. Ndipo panamveka mawu akuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
When Elijah heard that, he wrapped his cloak around his face. He went out of the cave and stood at its entrance. And he heard Yahweh speaking to him, saying again, “Elijah, why are you here?”
14 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
He replied again, “I have zealously served you, Yahweh, God Almighty. But the Israeli people have broken the agreement that they made with you. They have torn down your altars, and they have killed all of your prophets. I am the only one whom they have not killed, and now they are trying to kill me, too. [So I am running away from them].”
15 Yehova anati kwa Eliyayo, “Bwerera njira imene unadzera, ndipo upite ku Chipululu cha ku Damasiko. Ukakafika kumeneko, ukadzoze Hazaeli kuti akhale mfumu ya ku Aramu.
Then Yahweh told him, “Go back to the desert near Damascus. When you arrive there, anoint [with olive oil] a man named Hazael, [to appoint him] to be the king of Syria.
16 Ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi kuti akhale mfumu ya Israeli, ndiponso ukadzoze Elisa mwana wa Safati wa ku Abeli-Mehola kuti akhale mneneri wolowa mʼmalo mwako.
Then anoint Jehu, the son of Nimshi, to be the king of Israel, and also anoint Elisha the son of Shaphat, from Abel-Meholah [town], to become my prophet after you are dead.
17 Yehu adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Hazaeli, ndipo Elisa adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Yehu.
Hazael’s army [will kill many people, and] those who escape from [being killed by] his army will be killed by Jehu’s [army], and those who escape from [being killed by] Jehu’s army will be killed by Elisha.
18 Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.”
But [you need to know that] there are still 7,000 people in Israel who have never bowed to [worship] Baal or kissed his [idol].”
19 Kotero Eliya anachoka kumeneko, nakapeza Elisa mwana wa Safati. Iye ankatipula ndi mapulawo khumi ndi awiri okokedwa ndi ngʼombe ziwiriziwiri zapamagoli, ndipo iye mwini ankayendetsa goli la khumi ndi chiwiri. Eliya anapita kumene anali namuveka chofunda chake.
So Elijah went [to Syria] and found Elisha as he was plowing a field with a team of oxen. There were eleven other men who were in front of him, plowing with teams of oxen in the same field. Elijah went to Elisha, and took off his own coat and put it on Elisha, [to show Elisha that he wanted him to take his place as a prophet. Then he started to walk away].
20 Pomwepo Elisa anasiya ngʼombe zake nathamangira Eliya. Iye anati, “Mundilole kuti ndikatsanzike abambo ndi amayi anga, ndipo kenaka ndidzakutsatani.” Eliya anayankha kuti, “Bwerera. Ine ndachita chiyani kwa iwe?”
Elisha left the oxen standing there and ran after Elijah, and said to him, “I will go with you, but first let me kiss my parents goodbye.” Elijah replied, “Okay, go home. But do not forget why I have [given my cloak] to you!”
21 Choncho Elisa anamusiya Eliyayo nabwerera kwawo. Anatenga ngʼombe zake ziwiri zapagoli nazipha. Anatenga magoli a mapulawo ake nasonkhera moto kuphikira nyamayo ndipo anayipereka kwa anthu kuti adye. Ndipo ananyamuka natsatira Eliya ndi kukhala mtumiki wake.
So Elisha went back [to his oxen]. He killed them [and cut them in pieces] and used the wood from the plow to build a fire to roast the meat. He distributed the meat to the other people [in his town], and they all ate some. Then he went with Elijah and became his helper.

< 1 Mafumu 19 >