< 1 Mafumu 19 >

1 Tsono Ahabu anawuza Yezebeli zonse zimene anachita Eliya ndi momwe anaphera aneneri onse ndi lupanga.
and to tell Ahab to/for Jezebel [obj] all which to make: do Elijah and [obj] all which to kill [obj] all [the] prophet in/on/with sword
2 Choncho Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya kuti akamuwuze kuti, “Milungu indilange, ndipo indilange koopsa, ngati mawa nthawi ngati yomwe ino sindidzakupha iwe monga unaphera aneneriwo.”
and to send: depart Jezebel messenger to(wards) Elijah to/for to say thus to make: do [emph?] God and thus to add [emph?] for like/as time tomorrow to set: make [obj] soul: life your like/as soul: life one from them
3 Eliya ataona zimenezi, ananyamuka nathawa kupulumutsa moyo wake. Atafika ku Beeriseba ku Yuda, anasiya mtumiki wake kumeneko,
and to see: see and to arise: rise and to go: walk to(wards) soul: life his and to come (in): come Beersheba Beersheba which to/for Judah and to rest [obj] youth his there
4 ndipo Eliyayo anayenda ulendo wa tsiku limodzi mʼchipululu. Anafika pa kamtengo ka tsache, nakhala pansi pa tsinde lake napemphera kuti afe. Iye anati, “Yehova, ine ndatopa nazo. Chotsani moyo wanga. Ineyo sindine wopambana makolo anga.”
and he/she/it to go: went in/on/with wilderness way: journey day and to come (in): come and to dwell underneath: under broom (one *Q(k)*) and to ask [obj] soul: myself his to/for to die and to say many now LORD to take: take soul: life my for not pleasant I from father my
5 Ndipo Eliya anagona tulo tofa nato pa tsinde pa kamtengoko. Ndipo taonani, mngelo anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye.”
and to lie down: lay down and to sleep underneath: under broom one and behold this messenger: angel to touch in/on/with him and to say to/for him to arise: rise to eat
6 Eliya anayangʼana, ndipo taonani kumutu kwake kunali buledi wootcha pa makala ndi botolo la madzi. Iye anadya ndi kumwa, nʼkugonanso.
and to look and behold head his bun coal and jar water and to eat and to drink and to return: again and to lie down: lay down
7 Mngelo wa Yehova anabweranso kachiwiri, anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye, popeza ulendowu ndi wautali.”
and to return: again messenger: angel LORD second and to touch in/on/with him and to say to arise: rise to eat for many from you [the] way: journey
8 Tsono Eliya anadzuka nadya ndi kumwa. Atapeza mphamvu chifukwa cha chakudyacho, anayenda masiku 40, usana ndi usiku mpaka anafika ku Horebu, phiri la Mulungu.
and to arise: rise and to eat and to drink and to go: went in/on/with strength [the] food [the] he/she/it forty day and forty night till mountain: mount [the] God Horeb
9 Kumeneko analowa mʼphanga, nakhala komweko. Ndipo taonani, Yehova anayankhula naye kuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
and to come (in): come there to(wards) [the] cave and to lodge there and behold word LORD to(wards) him and to say to/for him what? to/for you here Elijah
10 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
and to say be jealous be jealous to/for LORD God Hosts for to leave: forsake covenant your son: descendant/people Israel [obj] altar your to overthrow and [obj] prophet your to kill in/on/with sword and to remain I to/for alone me and to seek [obj] soul: life my to/for to take: take her
11 Yehova anati, “Tuluka ndipo ukayime pa phiri pamaso pa Yehova, pakuti Yehova ali pafupi kudutsa pamenepo.” Tsono mphepo yayikulu ndi yamphamvu inawomba ningʼamba mapiri ndi kuswa matanthwe pamaso pa Yehova, koma Yehova sanali mʼmphepomo. Itapita mphepoyo panachita chivomerezi, koma Yehova sanali mʼchivomerezicho.
and to say to come out: come and to stand: stand in/on/with mountain: mount to/for face: before LORD and behold LORD to pass and spirit: breath great: large and strong to tear mountain: mount and to break crag to/for face: before LORD not in/on/with spirit: breath LORD and after [the] spirit: breath quaking not in/on/with quaking LORD
12 Chitapita chivomerezicho, panafika moto, koma Yehova sanali mʼmotomo. Ndipo utapita motowo, panamveka kamphepo kayaziyazi.
and after [the] quaking fire not in/on/with fire LORD and after [the] fire voice: sound silence thin
13 Eliya atamva kamphepoko, anakokera chovala chake naphimba kumutu. Anatuluka ndipo anayima pa khomo la phanga. Ndipo panamveka mawu akuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
and to be like/as to hear: hear Elijah and to wrap face his in/on/with clothing his and to come out: come and to stand: stand entrance [the] cave and behold to(wards) him voice and to say what? to/for you here Elijah
14 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
and to say be jealous be jealous to/for LORD God Hosts for to leave: forsake covenant your son: descendant/people Israel [obj] altar your to overthrow and [obj] prophet your to kill in/on/with sword and to remain I to/for alone me and to seek [obj] soul: life my to/for to take: take her
15 Yehova anati kwa Eliyayo, “Bwerera njira imene unadzera, ndipo upite ku Chipululu cha ku Damasiko. Ukakafika kumeneko, ukadzoze Hazaeli kuti akhale mfumu ya ku Aramu.
and to say LORD to(wards) him to go: went to return: return to/for way: road your wilderness [to] Damascus and to come (in): come and to anoint [obj] Hazael to/for king upon Syria
16 Ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi kuti akhale mfumu ya Israeli, ndiponso ukadzoze Elisa mwana wa Safati wa ku Abeli-Mehola kuti akhale mneneri wolowa mʼmalo mwako.
and [obj] Jehu son: child Nimshi to anoint to/for king upon Israel and [obj] Elisha son: child Shaphat from Abel-meholah Abel-meholah to anoint to/for prophet underneath: instead you
17 Yehu adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Hazaeli, ndipo Elisa adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Yehu.
and to be [the] to escape from sword Hazael to die Jehu and [the] to escape from sword Jehu to die Elisha
18 Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.”
and to remain in/on/with Israel seven thousand all [the] knee which not to bow to/for Baal and all [the] lip which not to kiss to/for him
19 Kotero Eliya anachoka kumeneko, nakapeza Elisa mwana wa Safati. Iye ankatipula ndi mapulawo khumi ndi awiri okokedwa ndi ngʼombe ziwiriziwiri zapamagoli, ndipo iye mwini ankayendetsa goli la khumi ndi chiwiri. Eliya anapita kumene anali namuveka chofunda chake.
and to go: went from there and to find [obj] Elisha son: child Shaphat and he/she/it to plow/plot two ten pair to/for face: before his and he/she/it in/on/with two [the] ten and to pass Elijah to(wards) him and to throw clothing his to(wards) him
20 Pomwepo Elisa anasiya ngʼombe zake nathamangira Eliya. Iye anati, “Mundilole kuti ndikatsanzike abambo ndi amayi anga, ndipo kenaka ndidzakutsatani.” Eliya anayankha kuti, “Bwerera. Ine ndachita chiyani kwa iwe?”
and to leave: forsake [obj] [the] cattle and to run: run after Elijah and to say to kiss please to/for father my and to/for mother my and to go: follow after you and to say to/for him to go: went to return: again for what? to make: do to/for you
21 Choncho Elisa anamusiya Eliyayo nabwerera kwawo. Anatenga ngʼombe zake ziwiri zapagoli nazipha. Anatenga magoli a mapulawo ake nasonkhera moto kuphikira nyamayo ndipo anayipereka kwa anthu kuti adye. Ndipo ananyamuka natsatira Eliya ndi kukhala mtumiki wake.
and to return: return from after him and to take: take [obj] pair [the] cattle and to sacrifice him and in/on/with article/utensil [the] cattle to boil them [the] flesh and to give: give to/for people and to eat and to arise: rise and to go: follow after Elijah and to minister him

< 1 Mafumu 19 >