< 1 Mafumu 19 >

1 Tsono Ahabu anawuza Yezebeli zonse zimene anachita Eliya ndi momwe anaphera aneneri onse ndi lupanga.
And Achab told Izebel all that Elijah had done, and withal that he had slain all the prophets with the sword.
2 Choncho Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya kuti akamuwuze kuti, “Milungu indilange, ndipo indilange koopsa, ngati mawa nthawi ngati yomwe ino sindidzakupha iwe monga unaphera aneneriwo.”
Then sent Izebel a messenger unto Elijah, saying, So may the gods do to me, and may they thus continue, if about this time tomorrow I do not render thy life as the life of any one of them.
3 Eliya ataona zimenezi, ananyamuka nathawa kupulumutsa moyo wake. Atafika ku Beeriseba ku Yuda, anasiya mtumiki wake kumeneko,
And when he saw this, he arose, and went for his life, and came to Beer-sheba', which belongeth to Judah, and he left his young man there.
4 ndipo Eliyayo anayenda ulendo wa tsiku limodzi mʼchipululu. Anafika pa kamtengo ka tsache, nakhala pansi pa tsinde lake napemphera kuti afe. Iye anati, “Yehova, ine ndatopa nazo. Chotsani moyo wanga. Ineyo sindine wopambana makolo anga.”
But he himself went forward into the wilderness a day's journey, and he came and sat down under a certain broom-bush: and he requested for himself to die; and he said, It is enough, now, O Lord, take away my soul; for I am not better than my fathers.
5 Ndipo Eliya anagona tulo tofa nato pa tsinde pa kamtengoko. Ndipo taonani, mngelo anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye.”
And he laid himself down and slept under a certain broom-bush, and, behold then, an angel was touching him, and said unto him, Arise, eat.
6 Eliya anayangʼana, ndipo taonani kumutu kwake kunali buledi wootcha pa makala ndi botolo la madzi. Iye anadya ndi kumwa, nʼkugonanso.
And he looked about, and, behold, there was at his head a cake baked on coals, and a cruise of water; and he ate and drank, and laid himself down again.
7 Mngelo wa Yehova anabweranso kachiwiri, anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye, popeza ulendowu ndi wautali.”
And the angel of the Lord came again, the second time, and touched him, and said, Arise, eat; because the journey is yet far for thee.
8 Tsono Eliya anadzuka nadya ndi kumwa. Atapeza mphamvu chifukwa cha chakudyacho, anayenda masiku 40, usana ndi usiku mpaka anafika ku Horebu, phiri la Mulungu.
And he arose, and ate and drank; and he went on the strength of that eating forty days and forty nights unto the mount of God, Horeb.
9 Kumeneko analowa mʼphanga, nakhala komweko. Ndipo taonani, Yehova anayankhula naye kuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
And he came there unto a cave, and remained there over night: and, behold, the word of the Lord came to him, and said unto him, What dost thou here, Elijah?
10 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
And he said, I have been very zealous for the Lord, the God of hosts; for the children of Israel have forsaken thy covenant, thy altars have they thrown down, and thy prophets have they slain with the sword: and I am left by myself alone, and they have sought my life, to take it away.
11 Yehova anati, “Tuluka ndipo ukayime pa phiri pamaso pa Yehova, pakuti Yehova ali pafupi kudutsa pamenepo.” Tsono mphepo yayikulu ndi yamphamvu inawomba ningʼamba mapiri ndi kuswa matanthwe pamaso pa Yehova, koma Yehova sanali mʼmphepomo. Itapita mphepoyo panachita chivomerezi, koma Yehova sanali mʼchivomerezicho.
And he said, Go forth, and stand upon the mount before the Lord: and, behold, the Lord passed by, and a wind, great and strong, rending the mountains, and breaking in pieces the rocks [went] before the Lord; but not in the wind was the Lord: and after the wind was an earthquake: but not in the earthquake was the Lord;
12 Chitapita chivomerezicho, panafika moto, koma Yehova sanali mʼmotomo. Ndipo utapita motowo, panamveka kamphepo kayaziyazi.
And after the earthquake was a fire; but not in the fire was the Lord; and after the fire was the sound of a soft whisper.
13 Eliya atamva kamphepoko, anakokera chovala chake naphimba kumutu. Anatuluka ndipo anayima pa khomo la phanga. Ndipo panamveka mawu akuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
And it came to pass, when Elijah heard it, that he concealed his face in his mantle, and went out, and stood in the entrance of the cave: and, behold, there came a voice unto him, and said, What dost thou here, Elijah?
14 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
And he said, I have been very zealous for the Lord, the God of hosts; because the children of Israel have forsaken thy covenant, thy altars have they thrown down, and thy prophets have they slain with the sword: and I am left by myself alone, and they have sought my life, to take it away.
15 Yehova anati kwa Eliyayo, “Bwerera njira imene unadzera, ndipo upite ku Chipululu cha ku Damasiko. Ukakafika kumeneko, ukadzoze Hazaeli kuti akhale mfumu ya ku Aramu.
And the Lord said unto him, Go, return on thy way to the wilderness of Damascus; and go, anoint Chazael to be king over Syria;
16 Ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi kuti akhale mfumu ya Israeli, ndiponso ukadzoze Elisa mwana wa Safati wa ku Abeli-Mehola kuti akhale mneneri wolowa mʼmalo mwako.
And Jehu the son of Nimshi shalt thou anoint to be king over Israel; and Elisha' the son of Shaphat of Abel-mecholah shalt thou anoint to be prophet in thy stead.
17 Yehu adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Hazaeli, ndipo Elisa adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Yehu.
And it shall come to pass, that him that escapeth the sword of Chazael shall Jehu slay; and him that escapeth the sword of Jehu shall Elisha' slay.
18 Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.”
And I will leave in Israel seven thousand, all the knees which have not been bent unto Ba'al, and every mouth which hath not kissed him.
19 Kotero Eliya anachoka kumeneko, nakapeza Elisa mwana wa Safati. Iye ankatipula ndi mapulawo khumi ndi awiri okokedwa ndi ngʼombe ziwiriziwiri zapamagoli, ndipo iye mwini ankayendetsa goli la khumi ndi chiwiri. Eliya anapita kumene anali namuveka chofunda chake.
And he departed thence, and found Elisha' the son of Shaphat, who was ploughing; twelve yoke of oxen were before him, and he was with the twelfth: and Elijah passed up to him, and cast his mantle toward him.
20 Pomwepo Elisa anasiya ngʼombe zake nathamangira Eliya. Iye anati, “Mundilole kuti ndikatsanzike abambo ndi amayi anga, ndipo kenaka ndidzakutsatani.” Eliya anayankha kuti, “Bwerera. Ine ndachita chiyani kwa iwe?”
And he left the oxen, and ran after Elijah, and said, Let me, I pray thee, kiss but my father and my mother, and I will [then] follow thee: and he said unto him, Go, return; for what have I done to thee?
21 Choncho Elisa anamusiya Eliyayo nabwerera kwawo. Anatenga ngʼombe zake ziwiri zapagoli nazipha. Anatenga magoli a mapulawo ake nasonkhera moto kuphikira nyamayo ndipo anayipereka kwa anthu kuti adye. Ndipo ananyamuka natsatira Eliya ndi kukhala mtumiki wake.
And he returned back from him, and took a yoke of oxen, and slew them, and with the instruments of the oxen he boiled the flesh for them, and he gave it unto the people, and they did eat; and then he arose, and went after Elijah, and ministered unto him.

< 1 Mafumu 19 >