< 1 Mafumu 18 >

1 Patapita masiku ambiri, mʼchaka chachitatu cha chilala, Yehova anayankhula ndi Eliya kuti, “Pita ukadzionetse kwa Ahabu ndipo ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi.”
Après bien des jours, la parole de Yahvé fut adressée à Élie, la troisième année, en ces termes: « Va, montre-toi à Achab, et je ferai tomber la pluie sur la terre. »
2 Choncho Eliya anapita kukadzionetsa kwa Ahabu. Tsono nthawi imeneyi njala inakula kwambiri mu Samariya,
Élie alla se montrer à Achab. La famine était grave à Samarie.
3 ndipo Ahabu anayitana Obadiya amene ankayangʼanira nyumba yake yaufumu. (Obadiya ankaopa Yehova kwambiri.
Achab appela Abdias, qui avait la charge de la maison. (Or Abdias craignait beaucoup Yahvé;
4 Pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova, Obadiya anatenga aneneri 100 ndi kuwabisa mʼmapanga awiri, phanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ankawapatsa chakudya ndi madzi).
car lorsque Jézabel avait exterminé les prophètes de Yahvé, Abdias avait pris cent prophètes, en avait caché cinquante dans une caverne, et les avait nourris de pain et d'eau).
5 Ahabu anawuza Obadiya kuti, “Pita mʼdziko kulikonse kumene kuli zitsime za madzi ndi ku zigwa zonse. Mwina mwake tingapeze udzu oti nʼkumadyetsa akavalo ndi abulu kuti akhale ndi moyo, kuti tisaphe chiweto chilichonse.”
Achab dit à Abdias: « Parcourez le pays, allez à toutes les sources d'eau et à tous les ruisseaux. Peut-être trouverons-nous de l'herbe et sauverons-nous les chevaux et les mules en vie, afin de ne pas perdre tous les animaux. »
6 Choncho anagawana dziko loti apiteko, Ahabu anapita mbali ina, Obadiya nʼkupita ina.
Et ils se partagèrent le pays pour le parcourir. Achab prit un chemin à part, et Abdias prit un autre chemin à part.
7 Obadiya akuyenda mʼnjira anakumana ndi Eliya. Ndipo taonani, Obadiya anamuzindikira Eliyayo, naweramira pansi ndipo anati, “Kodi ndinu, mbuye wanga Eliya?”
Comme Abdias était en chemin, voici qu'Élie le rencontra. Il le reconnut, tomba sur sa face et dit: « Est-ce toi, mon seigneur Élie? »
8 Eliya anayankha kuti, “Inde. Pita kawuze mbuye wako kuti, ‘Eliya wabwera.’”
Il lui répondit: « C'est moi. Va dire à ton maître: « Voici Élie, il est là! ».
9 Obadiya anafunsa kuti, “Kodi ndalakwa chiyani kuti inu mupereke mtumiki wanu kwa Ahabu kuti akaphedwe?
Il dit: « Comment ai-je péché, pour que tu livres ton serviteur entre les mains d'Achab, afin qu'il me tue?
10 Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, kulibe mtundu wa anthu kapena ufumu uliwonse kumene mbuye wanga sanatumeko anthu okakufunafunani. Ndipo pamene mtundu wa anthu kapena ufumu unena kuti kuno kulibe, Ahabu ankawalumbiritsa kuti atsimikizedi kuti inuyo kulibe kumeneko.
L'Éternel, ton Dieu, est vivant! Il n'y a ni nation ni royaume où mon seigneur n'ait envoyé pour te chercher. Quand on a dit: « Il n'est pas ici », il a juré par le royaume et la nation qu'on ne te trouverait pas.
11 Koma tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’
Maintenant, vous dites: « Va dire à ton maître: « Voici Élie qui est ici ».
12 Ine sindikudziwa kumene Mzimu wa Yehova udzakupititsani ine ndikachoka. Ngati ndipita kukamuwuza Ahabu ndipo iye wosadzakupezani, adzandipha. Komatu ine mtumiki wanu ndakhala ndi kupembedza Yehova kuyambira ubwana wanga.
Il arrivera, dès que je te quitterai, que l'Esprit de Yahvé te portera je ne sais où; aussi, quand je viendrai prévenir Achab, et qu'il ne te trouvera pas, il me tuera. Mais moi, ton serviteur, j'ai craint Yahvé dès ma jeunesse.
13 Mbuye wanga, kodi simunamve zimene ndinachita pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova? Ine ndinabisa aneneri 100 a Yehova mʼmapanga awiri, mʼphanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ndinkawapatsa chakudya ndi madzi akumwa.
N'a-t-on pas raconté à mon seigneur ce que j'ai fait quand Jézabel a tué les prophètes de l'Éternel, comment j'ai caché cent hommes des prophètes de l'Éternel avec cinquante dans une caverne, et comment je les ai nourris de pain et d'eau?
14 Ndiye inu tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’ Iyeyo adzandipha ndithu!”
Et maintenant, tu dis: « Va dire à ton maître: « Voici Élie », et il me tuera. Il me tuera. »
15 Eliya anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse wamoyo, amene ndimamutumikira, ine lero ndidzaonekera ndithu pamaso pa Ahabu.”
Élie dit: « L'Éternel des armées est vivant, devant qui je me tiens, et je me montrerai à lui aujourd'hui. »
16 Choncho Obadiya anapita kukakumana ndi Ahabu, namuwuza, ndipo Ahabu anapita kukakumana ndi Eliya.
Abdias alla à la rencontre d'Achab et le lui dit, et Achab alla à la rencontre d'Élie.
17 Pamene Ahabu anaona Eliya, anati kwa iye, “Kodi ndiwedi, munthu wovutitsa Israeli uja?”
Lorsqu'Achab vit Élie, il lui dit: « Est-ce toi, le trouble-fête d'Israël? »
18 Eliya anayankha kuti, “Ine sindinavutitse Israeli, koma ndinuyo ndi banja lanu. Mwasiya malamulo a Yehova ndipo mwatsatira Abaala.
Il répondit: « Ce n'est pas Israël que j'ai troublé, mais toi et la maison de ton père, parce que vous avez abandonné les commandements de l'Éternel et que vous avez suivi les Baals.
19 Tsopano sonkhanitsani anthu a mʼdziko lonse la Israeli kuti akumane nane pa Phiri la Karimeli. Ndipo mubwere nawo aneneri a Baala 450 ndi aneneri a fano la Asera 400, amene amadya pa tebulo la Yezebeli.”
Maintenant, envoie et rassemble vers moi tout Israël sur la montagne du Carmel, ainsi que quatre cent cinquante des prophètes de Baal et quatre cents des prophètes d'Ashéra, qui mangent à la table de Jézabel. »
20 Choncho Ahabu anatumiza mawu mʼdziko lonse la Israeli, ndipo anasonkhanitsa aneneri a Baala ku Phiri la Karimeli.
Achab envoya donc chercher tous les enfants d'Israël et rassembla les prophètes sur le mont Carmel.
21 Eliya anapita patsogolo pa anthuwo ndipo anati, “Kodi mudzakhala anthu a mitima iwiri mpaka liti? Ngati Yehova ndi Mulungu, mutsateni; koma ngati Baala ndi Mulungu, mutsateni.” Koma anthu aja sanayankhe.
Élie s'approcha de tout le peuple et dit: « Jusques à quand hésiterez-vous entre les deux camps? Si Yahvé est Dieu, suivez-le; mais si c'est Baal, suivez-le. » Les gens n'ont pas dit un mot.
22 Pamenepo Eliya ananena kwa iwo kuti, “Ine ndilipo ndekha mneneri wa Yehova, koma Baala ali ndi aneneri 450.
Et Élie dit au peuple: « Moi, et moi seul, je suis resté comme prophète de l'Éternel; mais les prophètes de Baal sont quatre cent cinquante hommes.
23 Tibweretsereni ngʼombe zazimuna ziwiri. Iwo asankhepo okha ngʼombe imodzi, ndipo ayidule nthulinthuli ndi kuziyika pa nkhuni nthulizo, koma osakolezapo moto. Ndipo ine ndidzadula nthulinthuli ngʼombe inayo ndi kuyika pa nkhuni koma sindikolezapo moto.
Qu'ils nous donnent donc deux taureaux; qu'ils en choisissent un pour eux, qu'ils le coupent en morceaux, qu'ils le posent sur le bois et qu'ils n'y mettent pas le feu; et moi, je préparerai l'autre taureau, je le poserai sur le bois et je n'y mettrai pas le feu.
24 Kenaka inu muyitane dzina la mulungu wanu, ndipo ine ndidzayitana dzina la Yehova. Mulungu amene ati ayankhe potumiza moto, iyeyo ndiye Mulungu.” Pamenepo anthu onse anati, “Izi mwanena zamveka bwino.”
Tu invoqueras le nom de ton dieu, et moi j'invoquerai le nom de Yahvé. Le Dieu qui répond par le feu, qu'il soit Dieu. » Tout le peuple répondit: « Ce que tu dis est bien. »
25 Eliya anawuza aneneri a Baala kuti, “Yambani ndinu. Sankhani ngʼombe yayimuna imodzi, muyikonze, popeza mulipo ambiri. Muyitane dzina la mulungu wanu, koma musakoleze moto.”
Élie dit aux prophètes de Baal: « Choisissez pour vous un taureau, et habillez-le le premier, car vous êtes nombreux; invoquez le nom de votre dieu, mais n'y mettez pas le feu. »
26 Choncho iwo anatenga ngʼombe yayimunayo imene anawapatsa, nayikonza. Kenaka anayitana dzina la Baala kuyambira mmawa mpaka masana. Iwo anafuwula kuti, “Inu Baala, tiyankheni ife.” Koma panalibe yankho; palibe amene anayankha. Ndipo anavinavina mozungulira guwa lansembe limene anapanga.
Ils prirent le taureau qu'on leur avait donné, l'habillèrent et invoquèrent le nom de Baal depuis le matin jusqu'à midi, en disant: « Baal, écoute-nous! ». Mais il n'y avait pas de voix, et personne ne répondait. Ils sautèrent autour de l'autel qui avait été construit.
27 Nthawi yamasana Eliya anayamba kuwanyogodola ndipo anati, “Fuwulani kwambiri. Ndithudi, iye ndi mulungu! Mwinatu akulingalira kwambiri, kapena watanganidwa, kapena ali paulendo. Mwina wagona ndipo nʼkofunika kuti adzutsidwe.”
À midi, Élie se moqua d'eux et dit: « Criez à haute voix, car c'est un dieu. Ou bien il est plongé dans ses pensées, ou bien il est parti quelque part, ou bien il est en voyage, ou bien il dort et il faut le réveiller. »
28 Choncho iwo anafuwula kwambiri ndi kudzichekacheka ndi malupanga ndi mikondo, potsata miyambo yawo, mpaka kutuluka magazi.
Ils criaient à haute voix et se coupaient sur leur chemin avec des couteaux et des lances jusqu'à ce que le sang jaillisse sur eux.
29 Nthawi yamasana inadutsa, ndipo anapitiriza kunenera mwakhama mpaka nthawi yopereka nsembe ya madzulo. Koma panalibe yankho. Palibe amene anayankha, kapena kulabadira zimenezo.
Quand midi fut passé, ils prophétisèrent jusqu'au moment de l'offrande du soir; mais il n'y eut ni voix, ni réponse, et personne ne fit attention.
30 Pamenepo Eliya anati kwa anthu onse, “Senderani pafupi ndi ine.” Ndipo anthu onsewo anasendera pafupi ndi iye, ndipo iye anakonza guwa lansembe la Yehova limene linali litawonongeka.
Elie dit à tout le peuple: « Approchez-vous de moi! »; et tout le peuple s'approcha de lui. Il répara l'autel de Yahvé qui avait été renversé.
31 Eliya anatenga miyala 12, mwala uliwonse kuyimira fuko lililonse la Yakobo, amene Yehova anamuwuza kuti, “Dzina lako lidzakhala Israeli.”
Elie prit douze pierres, selon le nombre des tribus des fils de Jacob, à qui la parole de Yahvé avait été adressée en disant: « Israël sera ton nom. »
32 Ndi miyala imeneyo anamanga guwa mʼdzina la Yehova, ndipo anakumba ngalande yayikulu yolowa malita 15 a madzi kuzungulira guwalo.
Avec les pierres, il construisit un autel au nom de Yahvé. Il fit autour de l'autel une tranchée assez grande pour contenir deux seahs de semences.
33 Anayika nkhuni zija mʼmalo mwake nadula nthulinthuli ngʼombe yayimuna ija ndi kuyika nthulizo pa nkhunipo. Pamenepo Eliya anati, “Dzazani mitsuko inayi ndi madzi ndipo muwathire pa nyama ya nsembeyo ndi nkhunizo.”
Il rangea le bois, coupa le taureau en morceaux et le posa sur le bois. Il dit: « Remplissez d'eau quatre jarres, et versez-la sur l'holocauste et sur le bois. »
34 Eliya anati, “Thiraninso kachiwiri.” Anthu aja anathiranso madziwo kachiwiri. Iye analamula kuti, “Thiraninso kachitatu.” Ndipo iwo anathiranso kachitatu.
Il dit: « Faites-le une seconde fois. » Et ils le firent une seconde fois. Il dit: « Faites-le une troisième fois. » Et ils le firent une troisième fois.
35 Madziwo anayenderera pansi kuzungulira guwa lansembe, nadzaza ngalande yonse.
L'eau coulait autour de l'autel; il remplit aussi d'eau la tranchée.
36 Pa nthawi yopereka nsembe, mneneri Eliya anasendera pafupi ndi guwa lansembe, napemphera kuti, “Inu Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, lero zidziwike kuti ndinu Mulungu mu Israeli ndipo kuti ine ndine mtumiki wanu, kuti ine ndachita zonsezi chifukwa mwalamula ndinu.
Au moment de l'offrande du soir, le prophète Élie s'approcha et dit: « Yahvé, Dieu d'Abraham, d'Isaac et d'Israël, que l'on sache aujourd'hui que tu es Dieu en Israël et que je suis ton serviteur, et que j'ai fait toutes ces choses selon ta parole.
37 Ndiyankheni, Inu Yehova, ndiyankheni, kuti anthu awa adziwe Inu Yehova, kuti ndinu Mulungu, ndipo kuti mutembenuziranso mitima yawo kwa Inu.”
Écoute-moi, Yahvé, écoute-moi, afin que ce peuple sache que toi, Yahvé, tu es Dieu, et que tu as ramené son cœur à la raison. »
38 Pamenepo moto wa Yehova unagwa, nunyeketsa nsembe yopserezayo, nkhuni, miyala ndi dothi lomwe. Unawumitsanso madzi amene anali mʼngalande.
Le feu de l'Éternel tomba et consuma l'holocauste, le bois, les pierres et la poussière, et il lécha l'eau qui était dans le fossé.
39 Anthu onse ataona zimenezi, anaweramitsa nkhope zawo pansi, nafuwula kuti, “Yehova ndiye Mulungu! Yehova ndiye Mulungu!”
Quand tout le peuple vit cela, il tomba sur sa face. Ils disaient: « Yahvé, c'est Dieu! Yahvé, c'est Dieu! »
40 Pamenepo Eliya analamula anthuwo kuti, “Gwirani aneneri a Baala. Musalole kuti wina aliyense athawe!” Anagwira onsewo ndipo Eliya anabwera nawo ku Chigwa cha Kisoni, nawapha kumeneko.
Élie leur dit: « Saisissez les prophètes de Baal! Ne laissez pas un seul d'entre eux s'échapper! » Ils s'en emparèrent, et Élie les fit descendre au torrent de Kishon, où il les tua.
41 Ndipo Eliya anati kwa Ahabu, “Pitani, kadyeni ndi kumwa, pakuti kukumveka mkokomo wa mvula.”
Élie dit à Achab: « Lève-toi, mange et bois, car on entend le bruit d'une pluie abondante. »
42 Choncho Ahabu anapita kukadya ndi kumwa, koma Eliya anakwera pamwamba pa Phiri la Karimeli, ndipo anawerama mpaka pansi, nayika mutu wake pakati pa mawondo ake.
Et Achab monta pour manger et pour boire. Élie monta au sommet du Carmel; il se prosterna par terre et mit son visage entre ses genoux.
43 Eliya anawuza mtumiki wake kuti, “Pita kayangʼane ku nyanja.” Ndipo iye anapita nakayangʼana. Mtumikiyo anati, “Kulibe kanthu.” Kasanu nʼkawiri Eliya anati, “Pitanso.”
Il dit à son serviteur: « Monte maintenant et regarde vers la mer. » Il est monté et a regardé, puis a dit: « Il n'y a rien. » Il a dit sept fois: « Vas-y encore ».
44 Ulendo wachisanu ndi chiwiri mtumikiyo anafotokoza kuti, “Taonani, kamtambo kakangʼono kokhala ngati dzanja la munthu kakutuluka ku nyanja.” Pamenepo Eliya anati, “Pita, kamuwuze Ahabu kuti, ‘Konzani galeta lanu ndipo mutsike mvula isanakutsekerezeni.’”
La septième fois, il dit: « Voici qu'un petit nuage, semblable à la main d'un homme, s'élève de la mer. » Il dit: « Monte, dis à Achab: « Prépare-toi et descends, pour que la pluie ne t'arrête pas. »"
45 Nthawi imeneyi nʼkuti kuthambo kutayamba kusonkhana mitambo yakuda, mphepo inawomba, mvula yamphamvu inagwa ndipo Ahabu anakwera galeta napita ku Yezireeli.
En peu de temps, le ciel s'obscurcit de nuages et de vent, et il y eut une grande pluie. Achab monta à cheval et se rendit à Jizreel.
46 Dzanja la Yehova linali pa Eliya ndipo atamangira lamba chovala chake, anathamanga ndi kumupitirira Ahabu mpaka kukhala woyamba kukafika ku Yezireeli.
La main de Yahvé était sur Elie; il mit son manteau dans sa ceinture et courut devant Achab jusqu'à l'entrée de Jizreel.

< 1 Mafumu 18 >