< 1 Mafumu 18 >

1 Patapita masiku ambiri, mʼchaka chachitatu cha chilala, Yehova anayankhula ndi Eliya kuti, “Pita ukadzionetse kwa Ahabu ndipo ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi.”
Amalalu, ode osodayale gibu hame daha eso agoanega, Hina Gode da Ilaidiama amane sia: i, “Di asili, hina bagade A: iha: bema doaga: ma! Amasea, Na da gibu iasimu.”
2 Choncho Eliya anapita kukadzionetsa kwa Ahabu. Tsono nthawi imeneyi njala inakula kwambiri mu Samariya,
Amaiba: le, Ilaidia da muni asi. Samelia soge ganodini, esoiba: le, ha: i da baligili bagadedafa ba: i.
3 ndipo Ahabu anayitana Obadiya amene ankayangʼanira nyumba yake yaufumu. (Obadiya ankaopa Yehova kwambiri.
Amaiba: le, A:iha: be da hina bagade diasu ouligisu dunu Oubadaiama, ema misa: ne sia: i. (Oubadaia da noga: le Hina Godema nodone sia: ne gadosu dawa: i.
4 Pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova, Obadiya anatenga aneneri 100 ndi kuwabisa mʼmapanga awiri, phanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ankawapatsa chakudya ndi madzi).
Yesebele da Hina Gode Ea balofede dunu ili gebewane medole legelaloba, Oubadaia da balofede dunu 100 agoane lale, dogoa mogili gilisisu 50 aduna hamone, magufu gelabo aduna ganodini wamoaligimusa: oule asili, ilima ha: i manu amola hano gaguli masu.)
5 Ahabu anawuza Obadiya kuti, “Pita mʼdziko kulikonse kumene kuli zitsime za madzi ndi ku zigwa zonse. Mwina mwake tingapeze udzu oti nʼkumadyetsa akavalo ndi abulu kuti akhale ndi moyo, kuti tisaphe chiweto chilichonse.”
A: iha: be da Oubadaiama amane sia: i, “Ani ahoa: di! Ania da hano bubuga: su amola hano logo huluane soge ganodini ba: la masunu. Ania da Isala: ili dunu ilia hosi amola miule esalomusa: defele gisi hogola masunu. Amabela: ? Ninia ohe afae da hame medole legei ba: ma: bela: ?”
6 Choncho anagawana dziko loti apiteko, Ahabu anapita mbali ina, Obadiya nʼkupita ina.
Ela da sia: dalu, ela afae afae hogola masunu soge ilegei. Amalalu, ela da logo higagale asi.
7 Obadiya akuyenda mʼnjira anakumana ndi Eliya. Ndipo taonani, Obadiya anamuzindikira Eliyayo, naweramira pansi ndipo anati, “Kodi ndinu, mbuye wanga Eliya?”
Oubadaia da logoga ahoanoba, hedolowane Ilaidia ba: i. E da ea odagi dawa: beba: le, ea midadi gududafa beguduli, amane adole ba: i, “Hina! Amo da dila: ?”
8 Eliya anayankha kuti, “Inde. Pita kawuze mbuye wako kuti, ‘Eliya wabwera.’”
E bu adole i, “Dafawane! Na da Ilaidia wea! Di asili, dia hina bagade ema na da guiguda: esala: ba: ya adoma!”
9 Obadiya anafunsa kuti, “Kodi ndalakwa chiyani kuti inu mupereke mtumiki wanu kwa Ahabu kuti akaphedwe?
Oubadaia da amane adole i, “Na da adi hamobela: ? Dia da abuliba: le na hina bagade A: iha: be, ea na fane legema: ne logo fodosala: ?
10 Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, kulibe mtundu wa anthu kapena ufumu uliwonse kumene mbuye wanga sanatumeko anthu okakufunafunani. Ndipo pamene mtundu wa anthu kapena ufumu unena kuti kuno kulibe, Ahabu ankawalumbiritsa kuti atsimikizedi kuti inuyo kulibe kumeneko.
Dia Hina Gode Esala amo Ea Dioba: le na da dafawane ilegele sia: sa. A: iha: be da osobo bagadega fifi asi gala huluane amo ganodini, di hogoi helei. Soge fi ouligisu dunu afae da di da ea soge ganodini hame esala sia: ne iasu ianoba, A:iha: be da amo hina bagade, e da di hamedafa ba: i, amo dafawane ilegele sia: musa: sia: i.
11 Koma tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’
Amaiba: le, di da abuliba: le nama di da goega: i esala, amane ema sia: na masa: ne sia: bela: ?
12 Ine sindikudziwa kumene Mzimu wa Yehova udzakupititsani ine ndikachoka. Ngati ndipita kukamuwuza Ahabu ndipo iye wosadzakupezani, adzandipha. Komatu ine mtumiki wanu ndakhala ndi kupembedza Yehova kuyambira ubwana wanga.
Na da ahoasea, amola Hina Gode Ea A: silibu da di eno hame dawa: sogega oule ahoasea, na da adi hamoma: bela: ? Amane hamosea, na da A: iha: bema, di da goega: i esala amo adole, e da di goega: i esalebe hame ba: sea, na medole legemu. Di bu dawa: ma! Na goi fonobahadiga ganini, Hina Godema noga: le nodone sia: ne gadosu dawa: i.
13 Mbuye wanga, kodi simunamve zimene ndinachita pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova? Ine ndinabisa aneneri 100 a Yehova mʼmapanga awiri, mʼphanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ndinkawapatsa chakudya ndi madzi akumwa.
Yesebele da Hina Gode Ea balofede dunu ili gebewane medole legelaloba, na da balofede dunu 100 agoane lale, dogoa mogili gilisisu idi 50 aduna hamone, magufu gelabo aduna ganodini wamoaligimusa: oule asili, ilima ha: i manu amola hano gaguli masu. Amo di da hame nabibala: ?
14 Ndiye inu tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’ Iyeyo adzandipha ndithu!”
Amaiba: le, di da abuli na hina bagadema, di da goega: i esala: ba: ya adoma: ne, nama sia: sala: ? E da na medole legemu!”
15 Eliya anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse wamoyo, amene ndimamutumikira, ine lero ndidzaonekera ndithu pamaso pa Ahabu.”
Ilaidia da bu adole i, “Na da Hina Gode Bagadedafa Esala amo Ea hawa: hamonana. Amola na da Ea Dioba: le dafawane ilegele sia: sa. Na da wali esoga, hina bagadema odagi olemu.”
16 Choncho Obadiya anapita kukakumana ndi Ahabu, namuwuza, ndipo Ahabu anapita kukakumana ndi Eliya.
Amaiba: le, Oubadaia da hina bagade A: iha: bema asili, ema Ilaidia da esala: ba: ya adoi. Amalu, A:iha: be da Ilaidia gousa: musa: asi.
17 Pamene Ahabu anaona Eliya, anati kwa iye, “Kodi ndiwedi, munthu wovutitsa Israeli uja?”
A: iha: be da Ilaidia ba: beba: le, amane sia: i, “Agoea esalebe! Di da Isala: ili soge ganodini bidi hamosu dunu oda ilia hamosu bagadewane baligisa.”
18 Eliya anayankha kuti, “Ine sindinavutitse Israeli, koma ndinuyo ndi banja lanu. Mwasiya malamulo a Yehova ndipo mwatsatira Abaala.
Ilaidia da bu adole i, “Na da bidi hamosu dunudafa hame. Be di amola dia ada alia da bidi hamosu dunu. Di da Hina Gode Ea hamoma: ne sia: i amo mae nabawane hamone, ogogole ‘gode’ Ba: ile agoaila hahamoi amoma nodone sia: ne gadolala.
19 Tsopano sonkhanitsani anthu a mʼdziko lonse la Israeli kuti akumane nane pa Phiri la Karimeli. Ndipo mubwere nawo aneneri a Baala 450 ndi aneneri a fano la Asera 400, amene amadya pa tebulo la Yezebeli.”
Waha Isala: ili dunu huluane na gousa: musa: , Gamele Goumi amoga misa: ne sia: ma. Ilia da Ba: ile balofede dunu 450 agoane amola ogogole uda ‘gode’ Asila ea balofede dunu 400 agoane amo da hina bagade uda Yesebele ea fuligala: be, amo huluane oule misa.”
20 Choncho Ahabu anatumiza mawu mʼdziko lonse la Israeli, ndipo anasonkhanitsa aneneri a Baala ku Phiri la Karimeli.
Amaiba: le, A:iha: be da Isala: ili dunu huluane amola Ba: ile balofede dunu huluane, Gamele Goumia gilisima: ne sia: i.
21 Eliya anapita patsogolo pa anthuwo ndipo anati, “Kodi mudzakhala anthu a mitima iwiri mpaka liti? Ngati Yehova ndi Mulungu, mutsateni; koma ngati Baala ndi Mulungu, mutsateni.” Koma anthu aja sanayankhe.
Ilaidia da dunu huluanema asili, amane sia: i, “Dilia da habo wali seda ‘gode’ aduna elama fa: no bobogemusa: dadawa: loma: bela: ? Dilia da Hina Gode da Godedafa dawa: sea, Ema nodone sia: ne gadoma! Be dilia da Ba: ile da Godedafa dawa: sea, ema nodone sia: ne gadoma!” Be Isala: ili dunu da sia: afae hamedafa sia: i.
22 Pamenepo Eliya ananena kwa iwo kuti, “Ine ndilipo ndekha mneneri wa Yehova, koma Baala ali ndi aneneri 450.
Amalalu, Ilaidia da amane sia: i, “Na fawane da Hina Gode Ea balofede dunudafa esala. Be Ba: ile ea balofede dunu da 450 agoane esala.
23 Tibweretsereni ngʼombe zazimuna ziwiri. Iwo asankhepo okha ngʼombe imodzi, ndipo ayidule nthulinthuli ndi kuziyika pa nkhuni nthulizo, koma osakolezapo moto. Ndipo ine ndidzadula nthulinthuli ngʼombe inayo ndi kuyika pa nkhuni koma sindikolezapo moto.
Bulamagau gawali aduna gaguli misa! Ba: ile balofede dunu ilia da afae lale, medole, dasega: le, lalu habei da: iya ligisima. Be lalu mae ulagima. Na da bulamagau eno amoga ilia hamoi amo defele hamomu.
24 Kenaka inu muyitane dzina la mulungu wanu, ndipo ine ndidzayitana dzina la Yehova. Mulungu amene ati ayankhe potumiza moto, iyeyo ndiye Mulungu.” Pamenepo anthu onse anati, “Izi mwanena zamveka bwino.”
Amalu, Ba: ile balofede dunu da ilia ‘gode’ma sia: ne gadoma: ma. Amola na da Hina Godema sia: ne gadomu. Amalu, nowa ea hahamoi lalu nene gala: be ba: sea, amo ilia ‘gode’ da Godedafa esalebe dawa: mu.” Dunu huluane da amo hamomu hou hahawane nababeba: le, wele sia: i.
25 Eliya anawuza aneneri a Baala kuti, “Yambani ndinu. Sankhani ngʼombe yayimuna imodzi, muyikonze, popeza mulipo ambiri. Muyitane dzina la mulungu wanu, koma musakoleze moto.”
Ilaidia da Ba: ile balofede dunuma amane sia: i, “Dilia da dunu bagohameba: le, dili hidadea, bulamagau gawali lale, hahamoma. Dilia ‘gode’ma sia: ne gadoma, be lalu habei mae ulagisima.”
26 Choncho iwo anatenga ngʼombe yayimunayo imene anawapatsa, nayikonza. Kenaka anayitana dzina la Baala kuyambira mmawa mpaka masana. Iwo anafuwula kuti, “Inu Baala, tiyankheni ife.” Koma panalibe yankho; palibe amene anayankha. Ndipo anavinavina mozungulira guwa lansembe limene anapanga.
Ilia da bulamagau gawali amo da ilima gaguli misi, amo lale hahamoi. Amalu, Ba: ilema sia: ne gadolalobawane, esomogoa doaga: i. Ilia da amane wele sia: i, “Ba: ile! Ba: ile! Ninia sia: ne gadobe nabima: i!” Amola, ilia da oloda ilia gagili, amo sisiga: le, gagafodudalu. Be amomane, Ba: ile da ilima dabe hame adole i.
27 Nthawi yamasana Eliya anayamba kuwanyogodola ndipo anati, “Fuwulani kwambiri. Ndithudi, iye ndi mulungu! Mwinatu akulingalira kwambiri, kapena watanganidwa, kapena ali paulendo. Mwina wagona ndipo nʼkofunika kuti adzutsidwe.”
Esomogoadafa, Ilaidia da iliba: le lalasogole oufesega: nu. E amane sia: i, “Bu ha: giwane sia: ne gadoma! E da ‘gode’! E da olobolala ganumu o baeya sowana ganumu. O e da logoba: le asi ganumu. O e da golai diala ganumu. Amo didilisima!”
28 Choncho iwo anafuwula kwambiri ndi kudzichekacheka ndi malupanga ndi mikondo, potsata miyambo yawo, mpaka kutuluka magazi.
Amaiba: le, balofede dunu da bu ha: giwane sia: ne gadole amola ilia hou defele, ili gobele gobihei amola nusi amoga fofa: ginanobawane, maga: me da a: idafia: i.
29 Nthawi yamasana inadutsa, ndipo anapitiriza kunenera mwakhama mpaka nthawi yopereka nsembe ya madzulo. Koma panalibe yankho. Palibe amene anayankha, kapena kulabadira zimenezo.
Ilia da dadoula sisiga: sa lafia: lalobawane, baloga doaga: i. Be dabe adole iasu sia: da afae hame nabi.
30 Pamenepo Eliya anati kwa anthu onse, “Senderani pafupi ndi ine.” Ndipo anthu onsewo anasendera pafupi ndi iye, ndipo iye anakonza guwa lansembe la Yehova limene linali litawonongeka.
Amalalu, Ilaidia da dunu huluanema amane sia: i, “Nama gadenena misa.” Ilia da Ilaidiama gilisila misi. E da Hina Gode Ea oloda mugului, amo bu hahamoi.
31 Eliya anatenga miyala 12, mwala uliwonse kuyimira fuko lililonse la Yakobo, amene Yehova anamuwuza kuti, “Dzina lako lidzakhala Israeli.”
E da gele fagoyale gala lai. Amo gele afae afae da Ya: igobe (Hina Gode da ema Isala: ili dio asuli) amo ea mano afae afae dawa: ma: ne, lai.
32 Ndi miyala imeneyo anamanga guwa mʼdzina la Yehova, ndipo anakumba ngalande yayikulu yolowa malita 15 a madzi kuzungulira guwalo.
Amo gelega, e da Hina Godema nodone sia: ne gadosu oloda bu hahamoi. Oloda sisiga: le, e da hano logo amoga hano soga: sali amo nabai defei da 15 lida.
33 Anayika nkhuni zija mʼmalo mwake nadula nthulinthuli ngʼombe yayimuna ija ndi kuyika nthulizo pa nkhunipo. Pamenepo Eliya anati, “Dzazani mitsuko inayi ndi madzi ndipo muwathire pa nyama ya nsembeyo ndi nkhunizo.”
Amalu, e da oloda da: iya, lalu habei ligisili, bulamagau dasega: le, fofonobone dadamuni ligisi. E amane sia: i, “Dilia da osoboga hamoi ofodo bagade biyaduyale amoga hano dili, amo bulamagau gobele salimu amo da: iya amola lalu habei da: iya sogaga: la: ma.” Ilia da amo defele hamoi.
34 Eliya anati, “Thiraninso kachiwiri.” Anthu aja anathiranso madziwo kachiwiri. Iye analamula kuti, “Thiraninso kachitatu.” Ndipo iwo anathiranso kachitatu.
E amane sia: i, “Bu hamoma!” Ilia da amane hamoi. E amane sia: i, “Bu hamoma!” Amola ilia da amane hamoi.
35 Madziwo anayenderera pansi kuzungulira guwa lansembe, nadzaza ngalande yonse.
Hano da gudu sa: ili, oloda sisiga: le, hano logo nabalesi.
36 Pa nthawi yopereka nsembe, mneneri Eliya anasendera pafupi ndi guwa lansembe, napemphera kuti, “Inu Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, lero zidziwike kuti ndinu Mulungu mu Israeli ndipo kuti ine ndine mtumiki wanu, kuti ine ndachita zonsezi chifukwa mwalamula ndinu.
37 Ndiyankheni, Inu Yehova, ndiyankheni, kuti anthu awa adziwe Inu Yehova, kuti ndinu Mulungu, ndipo kuti mutembenuziranso mitima yawo kwa Inu.”
Baloga, ilia gobele salasu hamoma: ne ilegebe, balofede Ilaidia da oloda amoga asili, amane sia: ne gadoi, “Hina Gode! A: ibalaha: me amola Aisage amola Ya: igobe ilia Gode! Di da Isala: ili Godedafa, amola na da Dia hawa: hamosu dunu, amola na wali hamoi da Dia hamoma: ne sia: beba: le hamoi, Isala: ili dunu da amo huluane dafawaneyale dawa: ma: ne, Dia na adole ba: su sia: ne gadosu amoma dabe adole ima. Hina Gode! Nama bu adole ima. Isala: ili dunu da Di, Hina Gode, da Godedafa amola Di da ili Dima bu hiougilala, amo ilia da dawa: ma: ne, na sia: ne gadosu amo dabe adole ima.”
38 Pamenepo moto wa Yehova unagwa, nunyeketsa nsembe yopserezayo, nkhuni, miyala ndi dothi lomwe. Unawumitsanso madzi amene anali mʼngalande.
Hina Gode da lalu gudu sanasi. Lalu da gobele salasu bulamagau amola lalu habei amola gele amola osobo huluane nene dagoi. Amola hano amo hano logo ganodini dialu amo huluane hafoga: i dagoi ba: i.
39 Anthu onse ataona zimenezi, anaweramitsa nkhope zawo pansi, nafuwula kuti, “Yehova ndiye Mulungu! Yehova ndiye Mulungu!”
Dunu huluane da amo hou ba: beba: le, ilisu osoba gala: la sa: i. Ilia amane wele sia: i, “Hina Gode da Godedafa! Hina Gode Hisu da Godedafa!”
40 Pamenepo Eliya analamula anthuwo kuti, “Gwirani aneneri a Baala. Musalole kuti wina aliyense athawe!” Anagwira onsewo ndipo Eliya anabwera nawo ku Chigwa cha Kisoni, nawapha kumeneko.
Ilaidia da amane hamoma: ne sia: i, “Ba: ile balofede dunu gagulaliligima! Dunu afae da maedafa hobeama: ma!” Isala: ili dunu da Ba: ile balofede dunu huluane gagulaliligi. Amola Ilaidia da ili oule, Gaisione Hanoga sa: ili, ili huluane fane lelegei.
41 Ndipo Eliya anati kwa Ahabu, “Pitani, kadyeni ndi kumwa, pakuti kukumveka mkokomo wa mvula.”
Amalalu, Ilaidia da hina bagade A: iha: bema amane sia: i, “Waha ha: i namasa! Na da gibu bagade olamabe naba!”
42 Choncho Ahabu anapita kukadya ndi kumwa, koma Eliya anakwera pamwamba pa Phiri la Karimeli, ndipo anawerama mpaka pansi, nayika mutu wake pakati pa mawondo ake.
A: iha: be da ha: i na ahoanoba, Ilaidia da Gamele Goumi da: iya heda: le, beguduli, osoboga muguni adoba dialuma bugi.
43 Eliya anawuza mtumiki wake kuti, “Pita kayangʼane ku nyanja.” Ndipo iye anapita nakayangʼana. Mtumikiyo anati, “Kulibe kanthu.” Kasanu nʼkawiri Eliya anati, “Pitanso.”
E da ea hawa: hamosu dunuma amane sia: i, “Di da asili, hano wayabo bagade amoga ba: le gama!” Ea hawa: hamosu dunu da amo ba: la asili, bu misini, amane sia: i, “Na da liligi hamedafa ba: i.” Ilaidia da ema fesuale agoane ba: la afufuma: ne sia: i.
44 Ulendo wachisanu ndi chiwiri mtumikiyo anafotokoza kuti, “Taonani, kamtambo kakangʼono kokhala ngati dzanja la munthu kakutuluka ku nyanja.” Pamenepo Eliya anati, “Pita, kamuwuze Ahabu kuti, ‘Konzani galeta lanu ndipo mutsike mvula isanakutsekerezeni.’”
E da afufulala fesu amoga ba: la asi, bu misini, amane sia: i, “Na da mobi fonobahadi, dunu ea lobo agoai, amo baligili hame, be agoai fawane hano wayabo gudunini gado heda: lebe ba: i.” Ilaidia da ea hawa: hamosu dunuma amane sia: i, “hina bagade A: iha: bema asili, ea masunu logo gibuga ga: sa: besa: le, ea ‘sa: liode’ lale, amo da: iya fila heda: le, hi diasua hedolo masa: ne sia: ma.”
45 Nthawi imeneyi nʼkuti kuthambo kutayamba kusonkhana mitambo yakuda, mphepo inawomba, mvula yamphamvu inagwa ndipo Ahabu anakwera galeta napita ku Yezireeli.
Fonobahadi aligili, mu da mobiga gasili gala: i ba: i, amola fo da muni misi amola gibu bagade da muni sa: i. A: iha: be da ea ‘sa: liode’ da: iya fila heda: le, Yeseliele moilai bai bagadega buhagi.
46 Dzanja la Yehova linali pa Eliya ndipo atamangira lamba chovala chake, anathamanga ndi kumupitirira Ahabu mpaka kukhala woyamba kukafika ku Yezireeli.
Hina Bagade Gode Ea gasa da misini, Ilaidiama doaga: i. Ilaidia da ea abula hina: bulu ga: sua ha: gidafa idiniginanu, A:iha: be fa: nonesilalu, ea bisili hehenaiya ahoana, Yeseliele amoma doaga: i.

< 1 Mafumu 18 >