< 1 Mafumu 16 >
1 Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
I doðe rijeè Gospodnja Juju sinu Ananijevu za Vasu govoreæi:
2 “Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
Što te podigoh iz praha i postavih voðem narodu svojemu Izrailju, a ti ideš putem Jerovoamovijem i navodiš na grijeh narod moj Izrailja da me gnjevi grijesima svojim,
3 Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
Evo, ja æu zatrti natražje Vasino i natražje doma njegova, i uèiniæu s domom tvojim kao s domom Jerovoama sina Navatova.
4 Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
Ko Vasin pogine u gradu, izješæe ga psi, a ko pogine u polju, izješæe ga ptice nebeske.
5 Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
A ostala djela Vasina i što je èinio, i junaštvo njegovo, nije li to zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh?
6 Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
I poèinu Vasa kod otaca svojih, i bi pogreben u Tersi; a na njegovo mjesto zacari se Ila sin njegov.
7 Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
I tako preko proroka Juja sina Ananijeva doðe rijeè Gospodnja protiv Vase i doma njegova za sve zlo što uèini pred Gospodom gnjeveæi ga djelima svojih ruku, te bi kao dom Jerovoamov, i zato što ga pobi.
8 Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
Dvadeset šeste godine carovanja Asina nad Judom zacari se Ila sin Vasin nad Izrailjem, i carova dvije godine u Tersi.
9 Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
A sluga njegov Zimrije, starješina nad polovinom kola, diže bunu na Ilu, kad pijaše u Tersi i opi se u kuæi Arse, koji upravljaše domom njegovijem u Tersi.
10 Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
I doðe Zimrije i ubi ga i pogubi ga dvadeset osme godine carovanja Asina nad Judom, i zacari se na njegovo mjesto.
11 Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
A èim se zacari i sjede na prijesto svoj, pobi sav dom Vasin, ne ostavi mu ni što uza zid mokri, i rodbinu njegovu i prijatelje njegove.
12 Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
Tako Zimrije zatr sav dom Vasin po rijeèi Gospodnjoj koju reèe za Vasu preko Juja proroka,
13 chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
Za sve grijehe Vasine i za grijehe Ile sina njegova, kojima griješiše i kojima na grijeh navodiše Izrailja gnjeveæi Gospoda Boga Izrailjeva taštinama svojim.
14 Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
A ostala djela Ilina i sve što je èinio, nije li to zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh?
15 Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
Godine dvadeset sedme carovanja Asina nad Judom zacari se Zimrije, i carova sedam dana u Tersi; a narod tada stajaše u okolu kod Givetona, koji bješe Filistejski.
16 Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
I narod što bješe u okolu kad èu da je Zimrije digao bunu i cara ubio, isti dan sav Izrailj u okolu postavi carem nad Izrailjem Amrija vojvodu.
17 Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
I Amrije i sav Izrailj s njim otidoše od Givetona i opkoliše Tersu.
18 Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
A Zimrije kad vidje gdje osvojiše grad, otide u dvor carski, i zapali nad sobom dvor carski, te pogibe,
19 chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
Za grijehe svoje kojima je griješio èineæi što je zlo pred Gospodom, hodeæi putem Jerovoamovijem i u grijehu njegovu, kojim je griješio navodeæi na grijeh Izrailja.
20 Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
A ostala djela Zimrijeva i buna koju podiže, nije li to zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh?
21 Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
Tada se razdijeli narod Izrailjev na dvoje: polovina naroda prista za Tivnijom sinom Ginatovijem da ga uèini carem, a druga polovina prista za Amrijem.
22 Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
Ali narod koji prista za Amrijem bi jaèi od naroda koji prista za Tivnijom sinom Ginatovijem. I umrije Tivnija, a carova Amrije.
23 Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
Trideset prve godine carovanja Asina nad Judom poèe carovati Amrije nad Izrailjem, i carova dvanaest godina; u Tersi carova šest godina.
24 Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
I kupi goru Samarijsku od Semera za dva talanta srebra, i sagradi grad na gori, i nazva grad koji sagradi Samarija po imenu Semera gospodara od gore.
25 Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
A Amrije èinjaše što je zlo pred Gospodom, i gore èinjaše od svijeh koji bijahu prije njega.
26 Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
Jer hoðaše svijem putovima Jerovoama sina Navatova i u grijehu njegovu, kojim je naveo na grijeh Izrailja gnjeveæi Gospoda Boga Izrailjeva taštinama svojim.
27 Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
A ostala djela Amrijeva i sve što je èinio, i junaštva koja je èinio, nije li to zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh?
28 Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I poèinu Amrije kod otaca svojih, i bi pogreben u Samariji; a na njegovo se mjesto zacari Ahav sin njegov.
29 Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
I Ahav sin Amrijev poèe carovati nad Izrailjem trideset osme godine carovanja Asina nad Judom, i carova Ahav sin Amrijev nad Izrailjem u Samariji dvadeset i dvije godine.
30 Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
I èinjaše Ahav sin Amrijev što je zlo pred Gospodom, više od svijeh koji bijahu prije njega.
31 Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
I malo mu bijaše što hoðaše u grijesima Jerovoama sina Navatova, nego se još oženi Jezaveljom kæerju Etvala cara Sidonskoga, i otide, te služaše Valu i klanjaše mu se.
32 Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
I naèini oltar Valu u domu Valovu koji sazida u Samariji.
33 Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
I naèini Ahav gaj, i uèini Ahav više od svijeh careva Izrailjevijeh koji biše prije njega, da bi razgnjevio Gospoda Boga Izrailjeva.
34 Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.
Za njegova vremena Hil Vetiljanin sazida Jerihon. Na Avironu prvencu svojem osnova ga, a na Seguvu mjezincu svojem metnu mu vrata po rijeèi Gospodnjoj, koju reèe preko Isusa sina Navina.