< 1 Mafumu 16 >

1 Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
و کلام خداوند بر ییهو ابن حنانی درباره بعشا نازل شده، گفت:۱
2 “Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
«چونکه تو را ازخاک برافراشتم و تو را بر قوم خود، اسرائیل پیشوا ساختم اما تو به راه یربعام سلوک نموده، قوم من، اسرائیل را مرتکب گناه ساخته، تا ایشان خشم مرا از گناهان خود به هیجان آورند.۲
3 Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
اینک من بعشا و خانه او را بالکل تلف خواهم نمود وخانه تو را مثل خانه یربعام بن نباط خواهم گردانید.۳
4 Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
آن را که از بعشا در شهر بمیرد، سگان بخورند و آن را که در صحرا بمیرد، مرغان هوابخورند.»۴
5 Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
و بقیه وقایع بعشا و آنچه کرد و تهور او، آیا در کتاب تواریخ ایام پادشاهان اسرائیل مکتوب نیست؟۵
6 Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
پس بعشا با پدران خود خوابید و درترصه مدفون شد و پسرش ایله در جایش پادشاه شد.۶
7 Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
و نیز کلام خداوند بر ییهوابن حنانی نبی نازل شد، درباره بعشا و خاندانش هم به‌سبب تمام شرارتی که در نظر خداوند بجا آورده، خشم او را به اعمال دستهای خود به هیجان آورد و مثل خاندان یربعام گردید و هم از این سبب که او راکشت.۷
8 Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
و در سال بیست و ششم آسا، پادشاه یهودا، ایله بن بعشا در ترصه بر اسرائیل پادشاه شد و دوسال سلطنت نمود.۸
9 Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
و بنده او، زمری که سردارنصف ارابه های او بود، بر او فتنه انگیخت و او درترصه در خانه ارصا که ناظر خانه او در ترصه بود، می‌نوشید و مستی می‌نمود.۹
10 Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
و زمری داخل شده، او را در سال بیست و هفتم آسا، پادشاه یهودا زد و کشت و در جایش سلطنت نمود.۱۰
11 Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
و چون پادشاه شد و بر کرسی وی بنشست، تمام خاندان بعشا را زد چنانکه یک مرد از اقربا و اصحاب او را برایش باقی نگذاشت.۱۱
12 Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
پس زمری تمامی خاندان بعشا را موافق کلامی که خداوند به واسطه ییهوی نبی درباره بعشا گفته بود، هلاک کرد.۱۲
13 chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
به‌سبب تمامی گناهانی که بعشا و گناهانی که پسرش ایله کرده، و اسرائیل را به آنها مرتکب گناه ساخته بودند، به طوری که ایشان به اباطیل خویش خشم یهوه، خدای اسرائیل رابه هیجان آورد.۱۳
14 Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
و بقیه وقایع ایله و هرچه کرد، آیا درکتاب تواریخ ایام پادشاهان اسرائیل مکتوب نیست.۱۴
15 Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
در سال بیست و هفتم آسا، پادشاه یهودا، زمری در ترصه هفت روز سلطنت نمود و قوم دربرابر جبتون که از آن فلسطینیان بود، اردو زده بودند.۱۵
16 Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
و قومی که در اردو بودند، شنیدند که زمری فتنه برانگیخته و پادشاه را نیز کشته است. پس تمامی اسرائیل، عمری را که سردار لشکربود، در همان روز بر تمامی اسرائیل در اردوپادشاه ساختند.۱۶
17 Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
آنگاه عمری و تمام اسرائیل با وی از جبتون برآمده، ترصه را محاصره نمودند.۱۷
18 Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
و چون زمری دید که شهر گرفته شد، به قصر خانه پادشاه داخل شده، خانه پادشاه را برسر خویش به آتش سوزانید و مرد.۱۸
19 chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
و این به‌سبب گناهانی بود که ورزید و آنچه را که در نظرخداوند ناپسند بود بجا آورد، و به راه یربعام و به گناهی که او ورزیده بود، سلوک نموده، اسرائیل را نیز مرتکب گناه ساخت.۱۹
20 Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
و بقیه وقایع زمری و فتنه‌ای که او برانگیخته بود، آیا در کتاب تواریخ ایام پادشاهان اسرائیل مکتوب نیست؟۲۰
21 Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
آنگاه قوم اسرائیل به دو فرقه تقسیم شدندو نصف قوم تابع تبنی پسر جینت گشتند تا او راپادشاه سازند و نصف دیگر تابع عمری.۲۱
22 Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
اماقومی که تابع عمری بودند بر قومی که تابع تبنی پسر جینت بودند، غالب آمدند پس تبنی مرد وعمری سلطنت نمود.۲۲
23 Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
در سال سی و یکم آسا، پادشاه یهودا، عمری بر اسرائیل پادشاه شد ودوازده سال سلطنت نمود؛ شش سال در ترصه سلطنت کرد.۲۳
24 Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
پس کوه سامره را از سامر به دو وزنه نقره خرید و در آن کوه بنایی ساخت و شهری را که بنا کرد به نام سامر که مالک کوه بود، سامره نامید.۲۴
25 Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
و عمری آنچه در نظر خداوند ناپسند بود، به عمل آورد و از همه آنانی که پیش از او بودند، بدتر کرد.۲۵
26 Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
زیرا که به تمامی راههای یربعام بن نباط و به گناهانی که اسرائیل را به آنها مرتکب گناه ساخته بود به طوری که ایشان به اباطیل خویش خشم یهوه، خدای اسرائیل را به هیجان آورد، سلوک می‌نمود.۲۶
27 Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
و بقیه اعمال عمری که کرد و تهوری که نمود، آیا در کتاب تواریخ ایام پادشاهان اسرائیل مکتوب نیست؟۲۷
28 Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
پس عمری با پدران خویش خوابید و در سامره مدفون شد وپسرش اخاب در جایش سلطنت نمود.۲۸
29 Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
و اخاب بن عمری در سال سی و هشتم آسا، پادشاه یهودا، بر اسرائیل پادشاه شد، واخاب بن عمری بر اسرائیل در سامره بیست و دوسال سلطنت نمود.۲۹
30 Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
و اخاب بن عمری از همه آنانی که قبل از او بودند در نظر خداوند بدتر کرد.۳۰
31 Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
و گویا سلوک نمودن او به گناهان یربعام بن نباط سهل می‌بود که ایزابل، دختر اتبعل، پادشاه صیدونیان را نیز به زنی گرفت و رفته، بعل راعبادت نمود و او را سجده کرد.۳۱
32 Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
و مذبحی به جهت بعل در خانه بعل که در سامره ساخته بود، برپا نمود.۳۲
33 Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
و اخاب اشیره را ساخت و اخاب در اعمال خود افراط نموده، خشم یهوه، خدای اسرائیل را بیشتر از جمیع پادشاهان اسرائیل که قبل از او بودند، به هیجان آورد.۳۳
34 Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.
و در ایام او، حیئیل بیت ئیلی، اریحا را بنا کرد و بنیادش را برنخست زاده خود ابیرام نهاد و دروازه هایش را بر پسر کوچک خود سجوب برپا کرد موافق کلام خداوند که به واسطه یوشع بن نون گفته بود.۳۴

< 1 Mafumu 16 >