< 1 Mafumu 16 >

1 Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
那時,有上主的話傳於哈納尼的兒子耶胡,斥責巴厄沙說:「
2 “Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
我由塵埃中提拔了你,立你做我民以色列的領袖,你卻走了雅洛貝罕的路,使我民以色列犯罪,激怒我;
3 Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
我現在,我要掃除巴厄沙和他的家族,使他的家如同乃巴特的兒子雅洛貝罕的一家一樣:
4 Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
凡屬巴厄沙家的人,死在城中的,必為狗吞食,死在田野間的,必為空中的飛鳥啄食。」
5 Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
巴厄沙其餘的事蹟,他所行的事和他的功績,都記載在以色列列王實錄上。
6 Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
巴厄沙與列祖同眠,葬在提爾匝;他的兒子厄拉繼位為王。
7 Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
上主藉哈納尼的兒子,先知耶胡傳話斥責巴厄沙和他的家族,是因為他行了許多上主眼中視為惡的事,以自己的作為激怒了上主,如同雅洛貝罕的家一樣;又因為他殺了雅洛貝罕全家。厄拉為以色列王
8 Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
猷大王阿撒二十六年,巴厄沙的兒子厄拉在提爾匝登極作以色列王,在位凡二年。
9 Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
他的臣僕,即率領他半數戰車的隊長,齊默黎結黨背叛了他。當他在提爾匝,他的家在阿爾匝家喝醉時,
10 Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
齊默黎衝入,擊殺了他,篡奪了他的王位,時在猶大王阿撒二十七年。
11 Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
齊默黎一登極,立刻屠殺了巴厄沙全家,沒有給他留下一個男子,連他的親屬朋友都殺了。
12 Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
齊默黎這樣毀滅了巴厄沙全家,應驗了上主藉先知耶胡斥責巴厄沙所說的話。
13 chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
這是因為巴厄沙和他的兒子厄拉所犯的一切罪,即引以色列陷於罪惡,因他們製造了虛無偶像,激怒了上主,以色列的天主。
14 Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
厄拉其餘的事蹟,他的一切作為,都記載在以色列列王實錄上。齊默黎為以色列王
15 Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
猶大王阿撒二十七年,齊默黎王提爾匝作王僅七天。當時人民正在圍攻培肋舍特人的基貝通,
16 Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
消息傳到營中說:齊默黎已經叛變,擊殺了君王,全以色列人當天即在營中,選立了軍長敖默黎作以色列王。
17 Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
敖默黎和與他在一起的全以色列人,從基貝通上去圍攻提爾匝。
18 Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
齊默黎一見城已失陷,即走進王宮的城堡,縱火焚燒王宮,自焚而死。
19 chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
這是因為他所犯的罪惡,行了上主視為惡的事,走了雅洛貝罕的路,並以自己所犯的罪,使以色列陷於罪惡。
20 Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
齊默黎其餘的事蹟,暗殺叛變的事,都記載在以色列列王實錄。
21 Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
那時,以色列人民分裂為二:一半跟隨基納特的兒子提貝尼,要立他為王;一半跟隨敖默黎。
22 Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
跟隨敖默黎的人勝過了跟隨基納特的兒子提貝尼的人;提貝尼死後,敖默黎便作了王。敖默黎為以色列王
23 Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
猶大王阿撒三十一年,敖默黎登極作以色列王,在位凡十二年,其中六年在提爾匝。
24 Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
敖默黎用兩「塔冷通」銀子,由舍默爾手中買下了芍默龍山。他修建了這座山,依照山的原主舍默爾的名字,給他所建築的城起名叫「撒瑪黎雅。」
25 Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
敖默黎行了上主視為惡的事,甚至比他以前的人更為邪惡。
26 Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
事事仿效乃巴特的兒子雅洛貝罕所走的路,犯了更使以色列陷於罪惡的罪,又敬拜邪神偶像,激怒上主,以色列的天主。
27 Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
敖默黎其餘的事蹟,他的作為和功蹟,都記載在以色列列王實錄上。
28 Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
敖默黎與列祖同眠,葬在撒瑪黎雅;他的兒子阿哈布繼位為王。阿哈布為以色列王
29 Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
猶大王阿撒三十八年,敖默黎的兒子阿哈布登極作以色列王。敖默黎的兒子阿哈布在撒瑪黎雅作以色列王,凡二十二年。
30 Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
敖默黎的兒子阿哈布行了上主視為惡的事,甚於他以前的人。
31 Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
他走了乃巴特的兒子雅洛貝罕犯罪的路,尚以為是小事,又娶了漆冬王厄特巴耳的女兒依則貝耳為妻,親自去服事敬拜巴耳,
32 Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
在撒瑪黎雅為巴耳建築了一座廟宇,廟內為巴耳設立了一座祭壇。
33 Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
阿哈布又立了阿舍辣;阿哈布行事激怒上主,以色列的天主,尤甚於他以前的以色列王。
34 Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.
他在位的時候,貝特耳人希耳重建了耶里哥;奠基的時候,死了長子阿彼蘭;安門的時候,死了幼子色古布:這正應驗了上主藉農的兒子若蘇厄所說的話。

< 1 Mafumu 16 >