< 1 Mafumu 15 >
1 Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
A osamnaeste godine carovanja Jerovoama sina Navatova zacari se Avijam nad Judom.
2 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
I carova tri godine u Jerusalimu. A materi mu bješe ime Maha kæi Avesalomova.
3 Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
On hoðaše u svijem grijesima oca svojega, koje je èinio pred njim, i ne bješe srce njegovo cijelo prema Gospodu Bogu njegovu kao srce Davida oca njegova.
4 Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
Ali radi Davida dade mu Gospod Bog njegov vidjelo u Jerusalimu podigav sina njegova nakon njega i utvrdiv Jerusalim;
5 pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
Jer je David èinio što je pravo pred Gospodom niti je otstupao od èega što mu je zapovjedio svega vijeka svojega osim stvari s Urijom Hetejinom.
6 Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
A rat bješe izmeðu Rovoama i Jerovoama do njegova vijeka.
7 Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
A ostala djela Avijamova i sve što je èinio nije li zapisano u dnevniku careva Judinijeh? A bijaše rat izmeðu Avijama i Jerovoama.
8 Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I Avijam poèinu kod otaca svojih, i pogreboše ga u gradu Davidovu, a na njegovo mjesto zacari se Asa sin njegov.
9 Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
Godine dvadesete carovanja Jerovoamova nad Izrailjem zacari se Asa nad Judom.
10 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
Èetrdeset i jednu godinu carova u Jerusalimu. A materi mu bješe ime Maha kæi Avesalomova.
11 Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
I tvoraše Asa što je pravo pred Gospodom kao David otac mu.
12 Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
Jer istrijebi adžuvane iz zemlje i ukide sve gadne bogove koje bjehu naèinili oci njegovi.
13 Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
I mater svoju Mahu svrže s vlasti, jer ona naèini idola u lugu; i Asa izlomi idola i sažeže na potoku Kedronu.
14 Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
Ali visine ne biše oborene; ali srce Asino bješe cijelo prema Gospodu svega vijeka njegova.
15 Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
I unese u dom Gospodnji što bješe posvetio otac njegov i što on posveti, srebro i zlato i sudove.
16 Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
I bješe rat izmeðu Ase i Vase cara Izrailjeva svega vijeka njihova.
17 Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
Jer Vasa car Izrailjev izide na Judu i stade zidati Ramu da ne da nikome otiæi k Asi caru Judinu ni od njega doæi.
18 Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
Ali Asa uzev sve srebro i zlato što bješe ostalo u riznici Gospodnjoj i u riznici doma careva dade ga slugama svojim, i posla ih car Asa Ven-Adadu sinu Tavrimona sina Esionova, caru Sirskom, koji stanovaše u Damasku, i poruèi:
19 “Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
Vjera je izmeðu mene i tebe, izmeðu oca tvojega i oca mojega; evo šaljem ti dar, srebro i zlato; hajde, pokvari vjeru koju imaš s Vasom carem Izrailjevim, eda bi otišao od mene.
20 Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
I posluša Ven-Adad cara Asu, i posla vojvode svoje na gradove Izrailjeve i pokori Ijon i Dan i Avel-Vetmahu i sav Hinerot i svu zemlju Neftalimovu.
21 Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
A kad Vasa to èu, presta zidati Ramu, i vrati se u Tersu.
22 Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
Tada car Asa sazva sav narod Judin, nikoga ne izuzimajuæi; te odnesoše kamenje iz Rame i drva, èim zidaše Vasa, i od njega sazida car Asa Gevu Venijaminovu i Mispu.
23 Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
A ostala sva djela Asina i sva junaštva njegova, i što je god èinio i koje je gradove sagradio, nije li sve zapisano u dnevniku careva Judinijeh? Ali u starosti svojoj bolovaše od nogu.
24 Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I Asa poèinu kod otaca svojih, i bi pogreben kod otaca svojih u gradu Davida oca svojega. A na njegovo mjesto zacari se Josafat sin njegov.
25 Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
A Nadav sin Jerovoamov poèe carovati nad Izrailjem druge godine carovanja Asina nad Judom; i carova nad Izrailjem dvije godine.
26 Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom hodeæi putem oca svojega i u grijehu njegovu, kojim navede na grijeh Izrailja.
27 Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
I diže bunu na nj Vasa sin Ahijin od doma Isaharova, i ubi ga Vasa kod Givetona, koji bijaše Filistejski, kad Nadav i sav Izrailj bjehu opkolili Giveton.
28 Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
I tako ga ubi Vasa treæe godine carovanja Asina nad Judom, i zacari se na njegovo mjesto.
29 Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
A kad se zacari, pobi sav dom Jerovoamov, i ne ostavi nijedne duše od roda Jerovoamova dokle sve ne istrijebi po rijeèi Gospodnjoj, koju reèe preko sluge svojega Ahije Silomljanina,
30 chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
Za grijehe Jerovoamove, kojima je griješio i kojima je na grijeh naveo Izrailja, i za draženje kojim je dražio Gospoda Boga Izrailjeva.
31 Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
A ostala djela Nadavova i sve što je èinio, nije li to zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh?
32 Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
I bješe rat izmeðu Ase i Vase cara Izrailjeva svega vijeka njihova.
33 Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
Treæe godine carovanja Asina nad Judom zacari se Vasa sin Ahijin nad svijem Izrailjem u Tersi, i carova dvadeset i èetiri godine.
34 Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom hodeæi putem Jerovoamovijem i u grijehu njegovu, kojim navede na grijeh Izrailja.