< 1 Mafumu 15 >
1 Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
Now in the eighteenth year of the reign of Jeroboam the son of Nabat, Abiam reigned over Juda.
2 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
He reigned three years in Jerusalem: the name of his mother was Maacha the daughter of Abessalom.
3 Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
And he walked in all the sins of his father, which he had done before him: and his heart was not perfect with the Lord his God, as was the heart of David his father.
4 Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
But for David’s sake the Lord his God gave him a lamp in Jerusalem, to set up his son after him, and to establish Jerusalem:
5 pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
Because David had done that which was right in the eyes of the Lord, and had not turned aside from any thing that he commanded him, all the days of his life, except the matter of Urias the Hethite.
6 Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
But there was war between Roboam and Jeroboam all the time of his life.
7 Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
And the rest of the words of Abiam, and all that he did, are they not written in the book of the words of the days of the kings of Juda? And there was war between Abiam and Jeroboam.
8 Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Abiam slept with his fathers, and they buried him in the city of David, and Asa his son reigned in his stead.
9 Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
So in the twentieth year of Jeroboam king of Israel, reigned Asa king of Juda,
10 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
And he reigned one and forty years in Jerusalem. His mother’s name was Maacha, the daughter of Abessalom.
11 Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
And Asa did that which was right in the sight of the Lord, as did David his father:
12 Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
And he took away the effeminate out of the land, and he removed all the filth of the idols, which his fathers had made.
13 Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
Moreover he also removed his mother Maacha, from being the princess in the sacrifices of Priapus, and in the grove which she had consecrated to him: and he destroyed her den, and broke in pieces the filthy idol, and burnt it by the torrent Cedron:
14 Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
But the high places he did not take away. Nevertheless the heart of Asa was perfect with the Lord all his days:
15 Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
And he brought in the things which his father had dedicated, and he had vowed, into the house of the Lord, silver and gold, and vessels.
16 Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
And there was war between Asa, and Baasa king of Israel all their days.
17 Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
And Baasa king of Israel went up against Juda, and built Rama, that no man might go out or come in, of the side of Asa king of Juda.
18 Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
Then Asa took all the silver and gold that remained in the treasures of the house of the Lord, and in the treasures of the king’s house, and delivered it into the hands of his servants: and sent them to Benadad son of Tabremon the son of Hezion, king of Syria, who dwelt in Damascus, saying:
19 “Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
There is a league between me and thee, and between my father and thy father: therefore I have sent thee presents of silver and gold: and I desire thee to come, and break thy league with Baasa king of Israel, that he may depart from me.
20 Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
Benadad hearkening to king Asa, sent the captains of his army against the cities of Israel, and they smote Ahion, and Dan, and Abeldomum Maacha, and all Cenneroth, that is all the land of Nephtali.
21 Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
And when Baasa had heard this, he left off building Rama, and returned into Thersa.
22 Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
But king Asa sent word into all Juda, saying: Let no man be excused: and they took away the stones from Rama, and the timber thereof wherewith Baasa had been building, and with them Asa built Gabaa of Benjamin, and Maspha.
23 Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
But the rest of all the acts of Asa, and all his strength, and all that he did and the cities that he built, are they not written in the book of the words of the days of the kings of Juda? But in the time of his old age he was diseased in his feet.
24 Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And he slept with his fathers, and was buried with them in the city of David his father. And Josaphat his son reigned in his place.
25 Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
But Nadab the son of Jeroboam reigned over Israel the second year of Asa king of Juda: and he reigned over Israel two years.
26 Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
And he did evil in the sight of the Lord, and walked in the ways of his father, and in his sins, wherewith he made Israel to sin.
27 Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
And Baasa the son of Ahias of the house of Issachar, conspired against him, and slew him in Gebbethon, which is a city of the Philistines: for Nadab and all Israel besieged Gebbethon.
28 Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
So Baasa slew him in the third year of Asa king of Juda, and reigned in his place.
29 Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
And when he was king he cut off all the house of Jeroboam: he left not so much as one soul of his seed, till he had utterly destroyed him, according to the word of the Lord, which he had spoken in the hand of Ahias the Silonite:
30 chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
Because of the sin of Jeroboam, which he had sinned, and wherewith he had made Israel to sin, and for the offence, wherewith he provoked the Lord the God of Israel.
31 Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
But the rest of the acts of Nadab, and all that he did, are they not written in the book of the words of the days of the kings of Israel?
32 Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
And there was war between Asa and Baasa the king of Israel all their days.
33 Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
In the third year of Asa king of Juda, Baasa the son of Ahias reigned over all Israel, in Thersa, four and twenty years.
34 Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.
And he did evil before the Lord, and walked in the ways of Jeroboam, and in his sins, wherewith he made Israel to sin.