< 1 Mafumu 14 >
1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
O sıralarda İsrail Kralı Yarovam'ın oğlu Aviya hastalandı.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
Yarovam, karısına, “Kalk, Yarovam'ın karısı olduğunu anlamamaları için kılığını değiştirip Şilo'ya git” dedi, “Bu halkın kralı olacağımı bana bildiren Peygamber Ahiya orada oturuyor.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
Ona on ekmek, birkaç çörek, bir tulum bal götür. Çocuğa ne olacağını o sana bildirecektir.”
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
Yarovam'ın karısı denileni yaptı; kalkıp Şilo'ya, Ahiya'nın evine gitti. Ahiya'nın gözleri yaşlılıktan görmez olmuştu.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
RAB, Ahiya'ya şöyle dedi: “Şimdi Yarovam'ın karısı gelecek. Hastalanan oğlunun durumunu senden soracak. Onu söylediğin gibi yanıtlayacaksın. O geldiğinde kendini sana başka biriymiş gibi gösterecek.”
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
Ahiya, kapıdan içeri giren kadının ayak seslerini duyunca, “Gel, Yarovam'ın karısı!” dedi, “Neden başka kılığa giriyorsun? Sana kötü haberlerim var.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Git Yarovam'a de ki, ‘İsrail'in Tanrısı RAB, Ben seni halkın arasından seçip kendi halkıma, İsrailliler'e önder yaptım, diyor,
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
Krallığı Davut'un soyundan alıp sana verdim. Ama sen buyruklarıma uyan, gözümde yalnız doğru olanı yapan ve bütün yüreğiyle yollarımı izleyen kulum Davut'a benzemedin.
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
Senden önce yaşayanların hepsinden çok kötülük yaptın. Beni reddettin; kendine başka ilahlar buldun, dökme putlar yaparak beni öfkelendirdin.
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
“‘Bundan dolayı Yarovam'ın ailesini sıkıntılara sokup İsrail'de onun soyundan gelen genç yaşlı bütün erkekleri öldüreceğim. Yarovam'ın ailesini gübre yakarcasına kökünden kurutacağım.
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
Yarovam'ın ailesinden kentte ölenleri köpekler, kırda ölenleri yırtıcı kuşlar yiyecek.’ RAB böyle konuştu.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
“Sana gelince, kalk, evine dön. Kente ayak basar basmaz çocuk ölecek.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
Bütün İsrail halkı ağıt yakıp onu gömecek. Yarovam'ın ailesinden yalnız o gömülecek. Çünkü Yarovam ailesi içinde İsrail'in Tanrısı RAB'bi hoşnut eden nitelikler yalnız onda bulundu.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
“RAB İsrail'e bir kral atayacak. Bu kral aynı gün Yarovam'ın ailesine son verecek. Ne zaman mı? Hemen şimdi.
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
RAB İsrail halkını cezalandıracak. İsrail halkı suda sallanan bir kamışa dönecek. RAB onları atalarına vermiş olduğu bu iyi topraklardan söküp Fırat Irmağı'nın ötelerine dağıtacak. Çünkü Aşera putlarını dikerek RAB'bi öfkelendirdiler.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
Yarovam'ın işlediği ve İsrail halkını sürüklediği günahlar yüzünden RAB İsrail'i terk edecek.”
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
Yarovam'ın karısı oradan ayrılıp Tirsa'ya döndü. Evinin eşiğine varınca çocuk öldü.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
Bütün İsrail halkı, RAB'bin kulu Peygamber Ahiya aracılığıyla söylediği söz uyarınca, çocuğu gömüp onun için ağıt yaktı.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Yarovam'ın krallığı dönemindeki öteki olaylar, nasıl savaştığı, ülkesini nasıl yönettiği İsrail krallarının tarihinde yazılıdır.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Yarovam yirmi iki yıl krallık yaptı. Ölüp atalarına kavuşunca, yerine oğlu Nadav kral oldu.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
Süleyman oğlu Rehavam Yahuda Kralı olduğunda kırk bir yaşındaydı. RAB'bin adını yerleştirmek için bütün İsrail oymaklarının yaşadığı kentler arasından seçtiği Yeruşalim Kenti'nde on yedi yıl krallık yaptı. Annesi Ammonlu Naama'ydı.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
Yahudalılar RAB'bin gözünde kötü olanı yaparak, işledikleri günahlarla Tanrı'yı atalarından daha çok öfkelendirdiler.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Ayrıca kendilerine her yüksek tepenin üstüne ve bol yapraklı her ağacın altına tapınma yerleri, dikili taşlar ve Aşera putları yaptılar.
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
Ülkedeki putperest törenlerinde fuhuş yapan kadın ve erkekler bile vardı. Yahudalılar RAB'bin İsrail halkının önünden kovduğu ulusların yaptığı bütün iğrençlikleri yaptılar.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
Rehavam'ın krallığının beşinci yılında Mısır Kralı Şişak Yeruşalim'e saldırdı.
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
Süleyman'ın yaptırmış olduğu altın kalkanlar dahil RAB'bin Tapınağı'nın ve sarayın bütün hazinelerini boşaltıp götürdü.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
Kral Rehavam bunların yerine tunç kalkanlar yaptırarak sarayın kapı muhafızlarının komutanlarına emanet etti.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
Kral RAB'bin Tapınağı'na her gittiğinde, muhafızlar bu kalkanları taşır, sonra muhafız odasına götürürlerdi.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Rehavam'ın krallığı dönemindeki öteki olaylar ve bütün yaptıkları Yahuda krallarının tarihinde yazılıdır.
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
Rehavam'la Yarovam arasında sürekli savaş vardı.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
Rehavam ölüp atalarına kavuşunca, Davut Kenti'nde atalarının yanına gömüldü. Annesi Ammonlu Naama'ydı. Rehavam'ın yerine oğlu Aviyam kral oldu.