< 1 Mafumu 14 >
1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
At that time, Jeroboam’s son Abijah became very sick.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
Jeroboam said to his wife, “Disguise yourself, in order that no one will recognize that you are my wife. Then go to Shiloh [city], where the prophet Ahijah [lives]. He is the one who predicted/prophesied that I would become the king of Israel.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
Take with you ten [loaves of] bread and some small flat cakes, and a jar of honey, [and give them] to him. [Tell him about] our son, [and] he will tell you what will happen to him.”
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
So his wife went to Shiloh, to Ahijah’s house. Ahijah was unable to see, because he was very old and had become blind.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
But [before she got there, ] Yahweh told Ahijah that Jeroboam’s wife was coming to inquire about their son, who was very sick. And Yahweh told Ahijah what he should tell her. When she came to him, she pretended to be another woman.
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
But when Ahijah heard her footsteps as she entered the doorway, he said to her, “Come in, wife of Jeroboam! (Why do you pretend that you are someone else?/It will not help you to pretend that you are someone else.) [RHQ] [Yahweh] has given me bad news to tell you.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Go and tell Jeroboam that this is what Yahweh, the God whom we Israelis [worship], says to you: ‘I chose you from among the common people and enabled you to become the king of my Israeli people.
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
I took [most of] the kingdom of Israel away from David’s descendants and gave it to you. But you have not been like David, who served me [very well]. He obeyed all my commandments very sincerely, doing only things that I considered to be right.
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
But you have done more evil things/deeds than all those [who ruled] before you. You have rejected me, and you have caused me to become very angry by making metal images of other gods so that you [and others] could worship them.
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
‘So, I am going to cause terrible things to happen to your family. I will cause all your male descendants to die, young ones and old ones. I will completely get rid of your family [MTY]. I will get rid of your family [MTY] just like a man completely burns dung [to cook his food].
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
[The corpses of] any members of your family who die in cities will be eaten by dogs. And [the corpses of] any members of your family who die in the open fields will be eaten by vultures. [This will surely happen because] I, Yahweh, have said [that it will happen].’
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
So go back home. And as soon as you enter the city, your son will die.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
All the Israeli people will mourn for him and bury him. He is the only one of Jeroboam’s family who will be buried [properly], because he is the only one of Jeroboam’s family with whom Yahweh is pleased.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
Furthermore, Yahweh will appoint for himself a king to rule over Israel who will get rid of Jeroboam’s descendants. And that [will start to happen] today!
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
Yahweh will punish the people of Israel; he will shake them like [the wind] shakes the reeds [that grow in] a stream. He will expel the Israeli people from this good land that he gave to our ancestors. He will scatter them into countries east of [the Euphrates] River, because they have caused him to become very angry by [worshiping statues of] the goddess Asherah.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
Yahweh will abandon the Israeli people because of the sins that Jeroboam committed, sins which led the Israeli people to commit them.”
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
Jeroboam’s wife returned home to Tirzah [city, the new capital of Israel]. And just as she entered her house, her son died.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
All the Israeli people mourned for him and buried him, which is what Yahweh had told his servant, the prophet Ahijah, would happen.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Everything else that Jeroboam did, and the record of wars that his [army] fought, and how he ruled, is written in the scroll called ‘The History of the Kings of Israel’.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Jeroboam ruled for 22 years; then he died [EUP] and his son Nadab became king.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
Solomon’s son Rehoboam ruled Judah. He was 41 years old when he started to rule, and he ruled for 17 years. He ruled in Jerusalem, which is the city that Yahweh chose out of all the tribes of Israel to be the place where he should be worshiped [MTY]. Rehoboam’s mother’s name was Naamah; she was from the Ammon people-group.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
The people of Judah did things that Yahweh considered to be evil. They caused him to become angry because they committed more sins than their ancestors had committed: They worshiped many other gods instead of worshiping only Yahweh.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
They built places to worship those gods; on high hills, and under big trees they set up [stone] pillars to worship the goddess Asherah.
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
Also, there were male prostitutes at these places of worship. The Israeli people did the same disgraceful things that had been done by the people whom Yahweh had expelled while the Israelis were advancing through the land.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
When Rehoboam had been ruling for almost five years, King Shishak of Egypt came [with his army] to attack Jerusalem.
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
They took away all the valuable things in the temple and in the king’s palace, including the gold shields that Solomon’s [workers] had made.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
King Rehoboam’s [workers] made bronze shields to replace them and entrusted them to officers who guarded the entrance to the king’s palace.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
Every time that the king went into the temple, those guards carried those shields; and [when he left the temple] they returned the shields to the storeroom.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Everything else that Rehoboam did is written [RHQ] in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah’.
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
There were wars continually between [the armies of] Rehoboam and Jeroboam.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
Then Rehoboam died [EUP], and he was buried in [the part of Jerusalem called] ‘The City of David’, where his ancestors were buried. Then his son Abijah became the king.