< 1 Mafumu 14 >
1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
At the time that he became sick Abijah [the] son of Jeroboam.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
And he said Jeroboam to wife his arise please and you will disguise yourself and not people will know that (you *Q(K)*) [are] [the] wife of Jeroboam and you will go Shiloh there! [is] there Ahijah the prophet he he spoke on me to king over the people this.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
And you will take in hand your ten bread[s] and cakes and a jar of honey and you will go to him he he will tell to you what? will it happen to the lad.
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
And she did thus [the] wife of Jeroboam and she arose and she went Shiloh and she went [the] house of Ahijah and Ahijah not he was able to see for they were fixed eyes his from old age his.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
And Yahweh he had said to Ahijah here! [the] wife of Jeroboam [is] about to come to seek a word from with you concerning son her for [is] sick he like this and like this you will speak to her and it may be when comes she and she [will be] acted as a stranger.
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
And it was when heard Ahijah [the] sound of feet her coming in the entrance and he said come O wife of Jeroboam why? this [are] you acting as a stranger and I [have been] sent to you hard.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Go say to Jeroboam thus he says Yahweh [the] God of Israel because that I raised up you from among the people and I made you a ruler over people my Israel.
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
And I tore away the kingdom from [the] house of David and I gave it to you and not you have been like servant my David who he kept commandments my and who he walked after me with all heart his to do only the right in view my.
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
And you have done evil to act more than all [those] who they were before you and you have gone and you have made for yourself gods other and molten images to provoke to anger me and me you have cast behind back your.
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
Therefore here I [am] about to bring calamity to [the] house of Jeroboam and I will cut off to Jeroboam [one who] urinates on a wall shut up and freed in Israel and I will sweep away behind [the] house of Jeroboam just as someone sweeps away dung until is complete it.
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
The [one who] dies of Jeroboam in the city they will devour the dogs and the [one who] dies in the open country they will devour [the] bird[s] of the heavens for Yahweh he has spoken.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
And you arise go to house your when go feet your the city towards and he will die the child.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
And they will mourn for him all Israel and they will bury him for this [one] to only him he will go of Jeroboam into a grave because it was found in him something good to Yahweh [the] God of Israel in [the] house of Jeroboam.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
And he will raise up Yahweh for himself a king over Israel who he will cut off [the] house of Jeroboam this the day and what? also now.
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
And he will strike down Yahweh Israel just as it sways reed in the water and he will pluck up Israel from on the ground good this which he gave to ancestors their and he will scatter them from [the] other side of the River because that they have made Asherah poles their provoking to anger Yahweh.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
So he may give up Israel on account of [the] sins of Jeroboam which he has sinned and which he has caused to sin Israel.
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
And she arose [the] wife of Jeroboam and she went and she came Tirzah towards she [was] coming at [the] threshold of the house and the lad he died.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
And they buried him and they mourned for him all Israel according to [the] word of Yahweh which he spoke by [the] hand of servant his Ahijah the prophet.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
And [the] rest of [the] matters of Jeroboam which he waged war and which he reigned there they [are] written on [the] scroll of [the] matters of the days of [the] kings of Israel.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And the days which he reigned Jeroboam [were] twenty and two year[s] and he lay down with ancestors his and he became king Nadab son his in place of him.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
And Rehoboam [the] son of Solomon he reigned in Judah [was] a son of forty and one year[s] Rehoboam when became king he and seven-teen year[s] - he reigned in Jerusalem the city where he had chosen Yahweh to put name his there from all [the] tribes of Israel and [the] name of mother his [was] Naamah the Ammonite [woman].
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
And it did Judah the evil in [the] eyes of Yahweh and they made jealous him more than all that they had done ancestors their by sins their which they sinned.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
And they built also they for themselves high places and sacred pillars and Asherah poles on every hill high and under every tree luxuriant.
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
And also cult prostitute[s] he was in the land they did according to all the abominations of the nations which he had dispossessed Yahweh from before [the] people of Israel.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
And it was in the year fifth of the king Rehoboam he came up (Shishak *Q(K)*) [the] king of Egypt on Jerusalem.
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
And he took [the] treasures of [the] house of Yahweh and [the] treasures of [the] house of the king and everything he took and he took all [the] shields of gold which he had made Solomon.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
And he made the king Rehoboam in place of them shields of bronze and he entrusted [them] on [the] hand of [the] commanders of the runners who guarded [the] entrance of [the] house of the king.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
And it was as often as went the king [the] house of Yahweh they carried them the runners and they returned them to [the] guardroom of the runners.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
And [the] rest of [the] matters of Rehoboam and all that he did ¿ not [are] they written on [the] scroll of [the] matters of the days of [the] kings of Judah.
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
And war it was between Rehoboam and between Jeroboam all the days.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
And he lay down Rehoboam with ancestors his and he was buried with ancestors his in [the] city of David and [the] name of mother his [was] Naamah the Ammonite [woman] and he became king Abijam son his in place of him.