< 1 Mafumu 14 >
1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
At that time Abijah son of Jeroboam was sick,
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
and Jeroboam says to his wife, “Now rise and change yourself, and they do not know that you [are the] wife of Jeroboam, and you have gone to Shiloh; behold, Ahijah the prophet [is] there; he spoke to me of [being] king over this people;
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
and you have taken in your hand ten loaves, and crumbs, and a bottle of honey, and have gone to him; he declares to you what becomes of the youth.”
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
And the wife of Jeroboam does so, and rises, and goes to Shiloh, and enters the house of Ahijah, and Ahijah is not able to see, for his eyes have stood because of his age.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
And YHWH said to Ahijah, “Behold, the wife of Jeroboam is coming to seek a word from you concerning her son, for he is sick; thus and thus you speak to her, and it comes to pass at her coming in, that she is making herself strange.”
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
And it comes to pass, at Ahijah’s hearing the sound of her feet [as] she came to the opening, that he says, “Come in, wife of Jeroboam, why is this [that] you are making yourself strange? And I am sent to you [with] a sharp thing.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Go, say to Jeroboam, Thus said YHWH, God of Israel: Because that I have made you high out of the midst of the people, and appoint you leader over my people Israel,
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
and tear the kingdom from the house of David, and give it to you—and you have not been as My servant David who kept My commands, and who walked after Me with all his heart, to only do that which [is] right in My eyes,
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
and you do evil above all who have been before you, and go, and make other gods and molten images for yourself to provoke Me to anger, and you have cast Me behind your back—
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
therefore, behold, I am bringing calamity to the house of Jeroboam, and have cut off to Jeroboam those sitting on the wall—shut up and left—in Israel, and have put away the posterity of the house of Jeroboam, as one puts away the dung until its consumption;
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
the dogs eat him who dies of Jeroboam in a city, and birds of the heavens eat him who dies in a field, for YHWH has spoken.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
And you, rise, go to your house; in the going in of your feet to the city, the boy has died;
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
and all Israel has mourned for him, and buried him, for this one—by himself—of Jeroboam comes to a grave, because there has been found in him a good thing toward YHWH, God of Israel, in the house of Jeroboam.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
And YHWH has raised up for Himself a king over Israel who cuts off the house of Jeroboam this day—and what? Even now!
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
And YHWH has struck Israel as the reed is moved by the waters, and has plucked Israel from off this good ground that He gave to their fathers, and scattered them beyond the River, because that they made their Asherim, provoking YHWH to anger;
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
and He gives up Israel because of the sins of Jeroboam that he sinned, and that he caused Israel to sin.”
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
And the wife of Jeroboam rises, and goes, and comes to Tirzah; she has come to the threshold of the house, and the youth dies;
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
and they bury him, and all Israel mourns for him, according to the word of YHWH that he spoke by the hand of His servant Ahijah the prophet.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
And the rest of the matters of Jeroboam, how he fought, and how he reigned, behold, they are written on the scroll of the Chronicles of the Kings of Israel.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And the days that Jeroboam reigned [are] twenty-two years, and he lies with his fathers, and his son Nadab reigns in his stead.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
And Rehoboam son of Solomon has reigned in Judah; Rehoboam [is] a son of forty-one years in his reigning, and he has reigned seventeen years in Jerusalem, the city that YHWH chose to set His Name there, out of all the tribes of Israel, and the name of his mother [is] Naamah the Ammonitess.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
And Judah does evil in the eyes of YHWH, and they make Him zealous above all that their fathers did by their sins that they have sinned.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
And they build—they also—for themselves high places, and standing-pillars, and Asherim, on every high height, and under every green tree;
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
and a whoremonger has also been in the land; they have done according to all the abominations of the nations that YHWH dispossessed from the presence of the sons of Israel.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
And it comes to pass, in the fifth year of King Rehoboam, Shishak king of Egypt has gone up against Jerusalem,
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
and he takes the treasures of the house of YHWH, and the treasures of the house of the king, indeed, he has taken the whole; and he takes all the shields of gold that Solomon made.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
And King Rehoboam makes shields of bronze in their stead, and has made [them] a charge on the hand of the heads of the runners, those keeping the opening of the house of the king,
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
and it comes to pass, from the going in of the king to the house of YHWH, the runners carry them, and have brought them back to the chamber of the runners.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
And the rest of the matters of Rehoboam and all that he did, are they not written on the scroll of the Chronicles of the Kings of Judah?
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
And there has been war between Rehoboam and Jeroboam [for] all the days;
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
and Rehoboam lies with his fathers, and is buried with his fathers in the City of David, and the name of his mother [is] Naamah the Ammonitess, and his son Abijam reigns in his stead.