< 1 Mafumu 14 >

1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
At that time Abijah the son of Jeroboam was sick.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
And Jeroboam said to his wife, Arise, I pray thee, and disguise thyself, that thou be not known to be the wife of Jeroboam; and go to Shiloh: behold, there is Ahijah the prophet, who told me that [I should be] king over this people.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
And take with thee ten loaves, and cakes, and a cruse of honey, and go to him: he will tell thee what shall become of the lad.
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
And Jeroboam's wife did so, and arose and went to Shiloh, and came to the house of Ahijah. And Ahijah could not see; for his eyes were set by reason of his age.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
And Jehovah said to Ahijah, Behold, the wife of Jeroboam cometh to ask a thing of thee about her son; for he is sick: thus and thus shalt thou say unto her; for it shall be, when she cometh in, that she shall feign to be another.
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
And it was so, when Ahijah heard the sound of her feet, as she came in at the door, that he said, Come in, thou wife of Jeroboam; why feignest thou to be another? But I am sent to thee with a hard [message].
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Go, tell Jeroboam, Thus saith Jehovah the God of Israel: Forasmuch as I exalted thee from among the people, and made thee prince over my people Israel,
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
and rent the kingdom away from the house of David, and gave it thee; and thou hast not been as my servant David, who kept my commandments, and who followed me with all his heart, to do only that which is right in my sight;
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
but thou hast done evil above all that were before thee, and hast gone and made thee other gods, and molten images, to provoke me to anger, and hast cast me behind thy back:
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
therefore behold, I will bring evil upon the house of Jeroboam, and will cut off from Jeroboam every male, him that is shut up and left in Israel, and will take away the house of Jeroboam, as a man taketh away dung, till it be all gone.
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
Him that dieth of Jeroboam in the city shall the dogs eat, and him that dieth in the field shall the fowl of the heavens eat; for Jehovah hath spoken.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
And thou, arise, go to thine own house; when thy feet enter into the city, the child shall die.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
And all Israel shall mourn for him, and they shall bury him; for he only of Jeroboam shall come to the grave, because in him there is found something good toward Jehovah the God of Israel, in the house of Jeroboam.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
And Jehovah shall raise up for himself a king over Israel, who shall cut off the house of Jeroboam that day; and what? ...even now.
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
And Jehovah will smite Israel, as a reed is shaken in the water, and he will root up Israel out of this good land which he gave to their fathers, and will scatter them beyond the river, because they have made their Asherahs, provoking Jehovah to anger.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
And he will give Israel up because of the sins of Jeroboam, wherewith he has sinned, and made Israel to sin.
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
And Jeroboam's wife arose and departed, and came to Tirzah; when she came to the threshold of the door, the child died.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
And they buried him; and all Israel mourned for him, according to the word of Jehovah, which he spoke through his servant Ahijah the prophet.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
And the rest of the acts of Jeroboam, how he warred, and how he reigned, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And the days that Jeroboam reigned were twenty-two years; and he slept with his fathers. And Nadab his son reigned in his stead.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
And Rehoboam the son of Solomon reigned in Judah. Rehoboam was forty-one years old when he began to reign, and he reigned seventeen years in Jerusalem, the city that Jehovah had chosen out of all the tribes of Israel to put his name there; and his mother's name was Naamah, an Ammonitess.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
And Judah did evil in the sight of Jehovah, and they provoked him to jealousy with their sins which they committed more than all that their fathers had done.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
And they also built for themselves high places, and columns, and Asherahs on every high hill and under every green tree;
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
and there were also sodomites in the land. They did according to all the abominations of the nations that Jehovah had dispossessed before the children of Israel.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
And it came to pass in the fifth year of king Rehoboam, [that] Shishak king of Egypt came up against Jerusalem.
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
And he took away the treasures of the house of Jehovah, and the treasures of the king's house; he even took away all; and he took away all the shields of gold that Solomon had made.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
And king Rehoboam made in their stead brazen shields, and committed them to the hands of the chief of the couriers who kept the entrance of the king's house.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
And it was so, that as often as the king entered into the house of Jehovah, the couriers bore them, and brought them again into the chamber of the couriers.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
And the rest of the acts of Rehoboam, and all that he did, are they not written in the book of the chronicles of the kings of Judah?
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
And there was war between Rehoboam and Jeroboam all [their] days.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
And Rehoboam slept with his fathers, and was buried with his fathers in the city of David. And his mother's name was Naamah, an Ammonitess. And Abijam his son reigned in his stead.

< 1 Mafumu 14 >