< 1 Mafumu 14 >

1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
Ved den Tid blev Jeroboams Søn Abija syg.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
Da sagde Jeroboam til sin Hustru: "Tag og forklæd dig, så man ikke kan kende, at du er Jeroboams Hustru, og begiv dig til Silo, thi der bor Profeten Ahija, som kundgjorde mig, at jeg skulde blive Konge over dette Folk;
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
tag ti Brød, noget Bagværk og en Krukke Honning med og henvend dig til ham, så vil han sige dig, hvorledes det skal gå Drengen!"
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
Jeroboams Hustru gjorde nu således; hun begav sig til Silo og gik ind i Ahijas Hus. Ahija kunde ikke se, da hans Øjne var sløve af Alderdom;
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
men HERREN havde sagt til Ahija: "Se, Jeroboams Hustru kommer til dig for at høre sig for hos dig angående sin Søn, da han er syg; det og det skal du svare hende; men når hun kommer, er hun forklædt."
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
Da nu Ahija hørte Lyden af hendes Trin, som hun gik ind ad Døren, sagde han: "Kom kun ind, Jeroboams Hustru! Hvorfor er du forklædt? Mig er det pålagt at bringe dig en tung Tidende.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Gå hen og sig til Jeroboam: Så siger HERREN, Israels Gud: Jeg ophøjede dig af Folkets Midte og gjorde dig til Fyrste over mit Folk Israel
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
og rev Riget fra Davids Hus og gav dig det; dog har du ikke været som min Tjener David, der holdt mine Bud og fulgte mig af hele sit Hjerte og kun gjorde, hvad der er ret i mine Øjne,
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
men du har handlet værre end alle dine Forgængere; du gik hen og krænkede mig og gjorde dig andre Guder og støbte Billeder, men mig kastede du bag din Ryg;
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
se, derfor vil jeg bringe Ulykke over Jeroboams Hus og udrydde hvert mandligt Væsen, hver og en af Jeroboams Slægt i Israel, og jeg vil feje Jeroboams Hus bort, som man fejer Skarn bort, til der ikke er Spor tilbage!
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
Den af Jeroboams Slægt, som dør i Byen, skal Hundene æde, og den, som dør på Marken, skal Himmelens Fugle æde, thi det er HERREN, der har talet!
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
Men gå nu hjem! Når din Fod betræder Byen, skal Barnet dø;
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
og hele Israel skal holde Dødeklage over ham og jorde ham, thi han er den eneste af Jeroboams Slægt, der skal komme i en Grav; thi hos ham fandtes dog noget, der vandt HERREN Israels Guds Behag inden for Jeroboams Slægt.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
Men HERREN vil oprejse sig en Konge over Israel, der skal udrydde Jeroboams Hus på den Dag.
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
Men også siden vil HERREN slå Israel, så at de svajer hid og did som Sivet i Vandet, og rykke Israel op fra dette herlige Land, som han gav deres Fædre, og sprede dem hinsides Floden, fordi de har lavet sig Asjerastøtter og krænket HERREN;
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
og han vil give Israel til Pris for de Synders Skyld, Jeroboam har begået og forledt Israel til."
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
Da gav Jeroboams Hustru sig på Vej og kom til Tirza; og da hun betrådte Husets Tærskel, døde Drengen;
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
og man jordede ham, og hele Israel holdt Dødeklage over ham efter det Ord, HERREN havde talet ved sin Tjener, Profeten Ahija.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Hvad der ellers er at fortælle om Jeroboam, hvorledes han førte Krig, og hvorledes han herskede står jo optegnet i Israels kongers Krønike.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Jeroboams Regeringstid udgjorde to og tyve År. Så lagde han sig til Hvile hos sine Fædre, og hans Søn Nadab blev Konge i hans Sted.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
Rehabeam, Salomos Søn, blev Kongei Juda. Rehabeam var een og fyrretyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede sytten År i Jerusalem, den By, HERREN havde udvalgt af alle Israels Stammer for der at stedfæste sit Navn. Hans Moder var en ammonitisk Kvinde ved Navn Na'ama.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
Og Juda gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, og med de Synder, de begik, vakte de hans Nidkærhed, mere end deres Fædre havde gjort.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Også de byggede sig Offerhøje, Stenstøtter og Asjerastøtter på alle høje Steder og under alle grønne Træer;
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
ja, der var endog Mandsskøger i Landet. De øvede alle de Vederstyggeligheder, som var begået af de Folk, HERREN havde drevet bort foran Israeliterne.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
Men i Kong Rebabeams femte Regeringsår drog Ægypterkongen Sjisjak op imod Jerusalem
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
og tog Skattene i HERRENs Hus og i Kongens Palads; alt tog han, også de Guldskjolde, Salomo havde ladet lave.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
Kong Rehabeam lod da i Stedet lave Kobberskjolde og gav dem i Forvaring hos Høvedsmændene for Livvagten, der holdt Vagt ved Indgangen til Kongens Palads;
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
og hver Gang Kongen begav sig til HERRENs Hus, bentede Livvagten dem, og bagefter bragte de dem tilbage til Vagtstuen.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Hvad der ellers er at fortælle om Rehabeam, alt, hvad han gjorde, står jo optegnet i Judas Kongers Krønike.
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
Rehabeam og Jeroboam lå i Krig med hinanden hele Tiden.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
Så lagde Rehabeam sig til Hvile hos sine Fædre og blev jordet hos sine Fædre i Davidsbyen. Hans Moder var en ammonitisk Kvinde ved Navn Na'ama. Og hans Søn Abija blev Konge i hans Sted.

< 1 Mafumu 14 >