< 1 Mafumu 14 >

1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
Toho času roznemohl se Abiáš, syn Jeroboámův.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
I řekl Jeroboám ženě své: Vstaň medle a změň se, aby nepoznali, že jsi žena Jeroboámova, a jdi do Sílo. Hle, tam jest Achiáš prorok, kterýž mi byl předpověděl, že mám býti králem nad lidem tímto.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
A vezma v ruce své deset chlebů a koláčů, a láhvici medu, jdi k němu; onť oznámí tobě, co se stane pacholeti tomuto.
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
I učinila tak žena Jeroboámova; nebo vstavši, šla do Sílo, a přišla do domu Achiášova. Ale Achiáš nemohl již hleděti, nebo pošly mu byly oči pro starost jeho.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
Hospodin pak řekl Achiášovi: Aj, žena Jeroboámova jde, aby se tebe něco zeptala o synu svém, proto že jest nemocen. Toto a toto budeš jí mluviti. Budeť pak, že když přijde, činiti se bude jinou.
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
Protož uslyšev Achiáš šust noh jejích, když vcházela do dveří, řekl: Poď, ženo Jeroboámova, proč se jinou činíš? Já zajisté poslán jsem k tobě s řečí tvrdou.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Jdi, pověz Jeroboámovi: Toto praví Hospodin Bůh Izraelský: Poněvadž jsem tě vyvýšil z prostředku lidu, a postavil jsem tě za vůdce nad lidem svým Izraelským,
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
A odtrhl jsem království od domu Davidova, a dal jsem je tobě, ty však nebyl jsi jako služebník můj David, kterýž ostříhal přikázaní mých, a následoval mne v celém srdci svém, čině toliko to, což jest pravého přede mnou,
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
Ale zlost jsi páchal hojněji nade všecky, kteříž byli před tebou; nebo odšed, učinils sobě bohy cizí a slité, abys mne dráždil, mne pak zavrhl jsi za hřbet svůj:
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
Protož aj, já uvedu zlé věci na dům Jeroboámův, a vyhladím z Jeroboáma, i toho, jenž močí na stěnu, i zajatého i zanechaného v Izraeli, a vyvrhu ostatky domu Jeroboámova, jako hnůj vymítán bývá až dočista.
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
Toho, kdož z domu Jeroboámova umře v městě, psi žráti budou, a toho, kdož umře na poli, ptáci nebeští jísti budou; neboť jest mluvil Hospodin.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
Ty pak vstana, jdi do domu svého, a když vcházeti budeš do města, tehdy umře pachole.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
I budou ho plakati všecken lid Izraelský, a pochovají jej; nebo ten sám z domu Jeroboámova dostane se do hrobu, proto že o něm z domu Jeroboámova jest slovo dobré u Hospodina Boha Izraelského.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
Vyzdvihneť však sobě Hospodin krále nad Izraelem, kterýž vyhladí dům Jeroboámův toho dne. Ale co? Nýbrž již vyzdvihl.
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
A zaklátí Hospodin Izraelem tak, jako se klátí třtina u vodách, a vykoření Izraele z země výborné této, kterouž dal otcům jejich, a rozptýlí je daleko za řeku, proto že sobě zdělali háje, popouzejíce Hospodina.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
A tak vydá Izraele pro hříchy Jeroboámovy, kterýž i sám hřešil, i v hřích uvodil Izraele.
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
Tedy vstavši žena Jeroboámova, odešla a přišla do Tersa, a když vstupovala na prah domu, umřelo pachole.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
I pochovali je, a plakal ho všecken lid Izraelský vedlé řeči Hospodinovy, kterouž mluvil skrze služebníka svého, Achiáše proroka.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Jiné pak věci Jeroboámovy, jaké boje vedl a kterak kraloval, aj, sepsány jsou v knize o králích Izraelských.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Všech dnů, v nichž kraloval Jeroboám, bylo dvamecítma let. I usnul s otci svými, a kraloval Nádab syn jeho místo něho.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
Roboám také syn Šalomounův kraloval nad Judou. V jednom a ve čtyřidcíti letech byl Roboám, když počal kralovati, a sedmnácte let kraloval v Jeruzalémě městě, kteréž vyvolil Hospodin ze všech pokolení Izraelských, aby tam přebývalo jméno jeho. Bylo pak jméno matky jeho Naama Ammonitská.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
Činil také lid Judský to, což zlého jest před Hospodinem, a k zůřivosti ho popudili hříchy svými, kterýmiž hřešili, více nežli otcové jejich všemi věcmi, kteréž činili.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Nebo i oni vystavěli sobě výsosti a sloupy, i háje na každém pahrbku vysokém a pod každým stromem zeleným.
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
Přesto byli ohyzdní sodomáři v zemi té, činíce vedlé všech ohavností pohanských, kteréž byl vyplénil Hospodin před tváří synů Izraelských.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
I stalo se léta pátého království Roboámova, že vytáhl Sesák král Egyptský proti Jeruzalému,
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
A pobral poklady domu Hospodinova a poklady domu královského, všecko to pobral. Vzal také všecky pavézy zlaté, kterýchž byl nadělal Šalomoun.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
Místo kterýchž nadělal král Roboám pavéz měděných, a poručil je úředníkům nad drabanty, kteříž ostříhali brány domu královského.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
A když král chodíval do domu Hospodinova, nosili je drabanti, a zase je přinášeli do pokoje drabantů.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Jiné pak věci Roboámovy, a všecko, což činil, zdaliž není zapsáno v knize o králích Judských.
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
Ano i válka, kteráž byla mezi Roboámem a Jeroboámem po všecky dny.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
I usnul Roboám s otci svými, a pochován jest s nimi v městě Davidově. A jméno matky jeho bylo Naama Ammonitská. I kraloval Abiam syn jeho místo něho.

< 1 Mafumu 14 >