< 1 Mafumu 14 >
1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
В онова време се разболя Авия, Еровоамовият син.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
И Еровоам каза на жена си: Стани, моля, предреши се така, щото да не познаят, че си Еровоамовата жена, и иди в Сило; ето там е пророк Ахия, който ми каза, че ще царувам над тия люде.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
Вземи със себе си десет хляба, сухари и едно гърне мед та иди при него; той ще ти яви какво ще стане на детето.
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
И тъй, Еровоамовата жена стори така; тя стана та отиде в Сило, и дойде в Ахиевата къща. А Ахия не можеше да вижда, защото очите му бяха се помрачили от старостта му.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
А Господ беше рекъл на Ахия: Ето, Еровоамовата жена иде да се допита до тебе за сина си, защото е болен. Така и така да й кажеш; защото, когато влезе, ще се престори на друга.
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
И тъй, като чу Ахия стъпването на нозете й като влизаше във вратата, рече: Влез, Еровоамова жено; защо се преструваш на друга? Но аз съм пратен при тебе с тежки известия.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Иди, кажи на Еровоама: Така казва Господ Израилевият Бог: Понеже Аз те издигнах отсред людете, и те поставих вожд на людете Си Израиля,
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
и, като откъснаха царството от Давидовия дом, дадоха го на тебе, но пак ти не биде както слугата Ми Давида, който опази заповедите Ми и като Ме следва с цялото си сърце, за да върши само онова, което е пред Мене,
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
но ти надмина в зло всички, които са били преди тебе, защото отиде и си направи други богове и леяни идоли, та Ме разгневи и отхвърли зад гърба си,
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
затова, ето, ще докарам зло на Еровоамовия дом, и ще изтребя от Еровоамовия род всеки от мъжки пол, както малолетния, така пълнолетния в Израиля, и ще измета Еровоамовия дом, както някой измита тора, догде не остане нищо.
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
Който от Еровоамовия род умре в града, него кучетата ще изядат; а който умре в полето, въздушните птици ще го изядат; защото Господ каза това.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
Ти, прочее, остани, иди у дома си; и като влязат нозете ти в града, детето ще умре.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
Целият Израил ще го оплаче, и ще го погребат; защото само то от Еровоамовия род ще се положи в гроб, понеже в него измежду Еровоамовия дом се намери нещо добро пред Господа Израилевия Бог.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
А Господ ще си въздигне цар над Израиля, който ще изтреби Еровоамовия дом в оня ден; но що? даже и сега!
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
И Господ ще порази Израиля като тръст, която се клати у водата; и ще изкорени Израиля из тая добра земя, която е дал на бащите им, и ще ги разпръсне оттатък реката Евфрат, понеже направиха ашерите си та разгневиха Господа.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
И ще предадете Израиля поради греховете, с които Еровоам съгреши, и с които направи Израиля да съгреши.
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
Тогава Еровоамовата жена стана та си отиде, и дойде в Терса; и като стъпи на прага на къщната врата, детето умря.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
И целият Израил го оплака, и погребаха го, според словото, което Господ говори чрез слугата Си пророка Ахия.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
А останалите дела на Еровоама, как воюва и как царува, ето, те са написани в Книгата на летописите на Израилевите царе.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Времето, през което Еровоам царуваше, беше двадесет и две години; и той заспа с бащите си, и вместо него се възцари син му Надав.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
А Ровоам, Соломоновият син царуваше над Юда. Ровоам бе на четиридесет и една година, когато стана цар, и царува седемнадесет години в Ерусалим, града, който Господ бе избрал измежду всичките Израилеви племена за да настани името Си там. Името на майка му, амонката, бе Наама.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
А Юда върши зло пред Господа; и раздразниха Го до ревнуване с извършените си грехове, които бяха повече от всичко, що бяха извършили бащите им.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Защото и те си издигнаха високи места и кумири и ашери на всеки висок хълм и под всяко зелено дърво.
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
Още в земята имаше мъжеложци, които постъпваха според всичките мерзости на народите, които Господ беше изгонил отпред израилтяните.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
И в петата година от Ровоамовото царуване, египетският цар Сисак дойде против Ерусалим,
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
та отнесе съкровищата на Господния дом и съкровищата на царската къща; отнесе всичко; отнесе още всички златни щитове, които Соломон бе направил.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
А вместо тях цар Ровоам направи медни щитове и ги предаде в ръцете на началниците на телохранителите, които пазеха вратата и царската къща.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
И когато влизаше царят в Господния дом, телохранителите ги държаха: после пак ги занасяха в залата на телохранителите.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
А останалите дела на Ровоама, и всичко що извърши, не са ли написани в Книгата на летописите на Юдовите царе?
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
А между Ровоама и Еровоама имаше постоянна война.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
И Ровоам заспа с бащите си, и погребан биде с бащите си в Давидовия град. Името на майка му, амонката, бе Наама. А вместо него се възцари син му Авия.