< 1 Mafumu 13 >
1 Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
А гле, човек Божји дође из земље Јудине с речју Господњом у Ветиљ, кад Јеровоам стајаше код олтара да кади.
2 Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
И повика пут олтара речју Господњом говорећи: Олтаре! Олтаре! Овако вели Господ: Ево, родиће се син дому Давидовом по имену Јосија, који ће на теби клати свештенике висина, који каде на теби, и људске ће кости спалити на теби.
3 Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
И учини знак истог дана говорећи: Ово је знак да је Господ то рекао: Ето, олтар ће се распасти и просуће се пепео што је на њему.
4 Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
А кад цар Јеровоам чу речи човека Божијег које викаше олтару ветиљском, пружи руку своју с олтара говорећи: Држите га! Али усахну му рука коју пружи на њ, и не могаше је повратити к себи.
5 Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
А олтар се распаде, и просу се пепео с олтара по знаку који учини човек Божји речју Господњом.
6 Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
Тада цар рече човеку Божијем: Припадни ка Господу Богу свом, и помоли се за ме да ми се поврати рука. И човек се Божји помоли Господу, и поврати се цару рука, и поста као што је била.
7 Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
И рече цар човеку Божијем: Ходи са мном кући мојој, и поткрепи се, и даћу ти дар.
8 Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
Али човек Божји рече цару: Да ми даш по куће своје, не бих ишао с тобом нити бих јео хлеба ни воде пио у овом месту.
9 Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
Јер ми је тако заповедио својом речју Господ говорећи: Не једи хлеба ни пиј воде, нити се враћај истим путем којим отидеш.
10 Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
И отиде другим путем, а не врати се оним којим беше дошао у Ветиљ.
11 Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
А у Ветиљу живљаше један стари пророк, коме дође син његов и приповеди све што учини пророк Божји онај дан у Ветиљу, и речи које рече цару; и приповедише синови тог пророка оцу свом.
12 Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
А отац им рече: Којим је путем отишао? И показаше синови пут којим отиде човек Божји који беше дошао из земље Јудине.
13 Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
А он рече синовима својим: Осамарите ми магарца. И осамарише му магарца, те уседе на њ.
14 ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
И пође за човеком Божјим, и нађе га а он седи под храстом, па му рече: Јеси ли ти човек Божји што дође из земље Јудине? Он му одговори: Ја сам.
15 Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
А он му рече: Ходи са мном мојој кући да једеш хлеба.
16 Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
Али он одговори: Не могу се вратити с тобом ни ићи с тобом; нити ћу јести хлеба ни пити воде с тобом у овом месту.
17 Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
Јер ми је речено речју Господњом: Не једи хлеба ни пиј воде онде, нити се враћај путем којим отидеш.
18 Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
А он му рече: и ја сам пророк као ти, и анђео Господњи рече ми речју Господњом говорећи: Врати га са собом у своју кућу нека једе хлеба и пије воде. Али му слага.
19 Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
И врати се с њим, те једе хлеба у његовој кући и пи воде.
20 Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
А кад сеђаху за столом, дође реч Господња пророку који га беше вратио;
21 Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
И повика на човека Божјег који беше дошао из земље Јудине, и рече: Овако вели Господ: Што ниси послушао реч Господњу, и ниси држао заповест коју ти је заповедио Господ Бог твој,
22 Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
Него си се вратио и јео хлеба и пио воде на месту за које ти је рекао: Не једи хлеба ни пиј воде; зато неће твоје тело доћи у гроб твојих отаца.
23 Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
И пошто се пророк ког беше вратио наједе хлеба и пошто се напи, осамари му магарца.
24 Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
А кад отиде, удеси га лав на путу и закла га. И тело његово лежаше на путу и магарац стајаше код њега; такође и лав стајаше код тела.
25 Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
И гле, људи пролазећи видеше тело где лежи на путу и лава где стоји код тела, и дошавши јавише у граду у коме живљаше стари пророк.
26 Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
А кад то чу пророк који га беше вратио с пута, рече: Ово је човек Божји, који не послуша речи Господње, зато га даде Господ лаву да га растргне и усмрти по речи Господњој коју му рече.
27 Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
И рече синовима својим говорећи: Осамарите ми магарца. И осамарише.
28 Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
И отишавши, нађе тело где лежи на путу, и магарца и лава где стоје код тела: Лав не беше изјео тело ни магарца растргао.
29 Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
Тада пророк подиже тело човека Божијег, и метнув га на магарца, однесе га натраг, и дође у град стари пророк да га ожали и погребе.
30 Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
И метну тело у свој гроб, и плакаху над њим говорећи: Јаох брате!
31 Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
А пошто га погребе, рече синовима својим говорећи: Кад умрем, погребите ме у гробу где је погребен човек Божји, покрај костију његових метните кости моје.
32 Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
Јер ће се зацело збити шта је огласио по речи Господњој за олтар ветиљски и за све куће висина које су по градовима самаријским.
33 Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
Пошто ово би, опет се Јеровоам не врати са свог злог пута; него опет начини из простог народа свештенике висинама; ко год хоћаше, томе он посвећиваше руке и тај постајаше свештеник висинама.
34 Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.
И то би на грех дому Јеровоамовом да би се истребио и да би га нестало са земље.