< 1 Mafumu 11 >

1 Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
Kral Süleyman firavunun kızının yanısıra Moavlı, Ammonlu, Edomlu, Saydalı ve Hititli birçok yabancı kadın sevdi.
2 Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
Bu kadınlar RAB'bin İsrail halkına, “Ne siz onların arasına girin, ne de onlar sizin aranıza girsinler; çünkü onlar kesinlikle sizi kendi ilahlarının ardınca yürümek üzere saptıracaklardır” dediği uluslardandı. Buna karşın, Süleyman onlara sevgiyle bağlandı.
3 Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
Süleyman'ın kral kızlarından yedi yüz karısı ve üç yüz cariyesi vardı. Karıları onu yolundan saptırdılar.
4 Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
Süleyman yaşlandıkça, karıları onu başka ilahların ardınca yürümek üzere saptırdılar. Böylece Süleyman bütün yüreğini Tanrısı RAB'be adayan babası Davut gibi yaşamadı.
5 Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
Saydalılar'ın tanrıçası Aştoret'e ve Ammonlular'ın iğrenç ilahı Molek'e taptı.
6 Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
Böylece RAB'bin gözünde kötü olanı yaptı, RAB'bin yolunda yürüyen babası Davut gibi tam anlamıyla RAB'bi izlemedi.
7 Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
Yeruşalim'in doğusundaki tepede Moavlılar'ın iğrenç ilahı Kemoş'a ve Ammonlular'ın iğrenç ilahı Molek'e tapmak için bir yer yaptırdı.
8 Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
İlahlarına buhur yakıp kurban kesen bütün yabancı karıları için de aynı şeyleri yaptı.
9 Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
İsrail'in Tanrısı RAB, kendisine iki kez görünüp, “Başka ilahlara tapma!” demesine karşın, Süleyman RAB'bin yolundan saptı ve O'nun buyruğuna uymadı. Bu yüzden RAB Süleyman'a öfkelenerek,
10 Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
11 Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
“Seninle yaptığım antlaşmaya ve kurallarıma bilerek uymadığın için krallığı elinden alacağım ve görevlilerinden birine vereceğim” dedi,
12 Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
“Ancak baban Davut'un hatırı için, bunu senin yaşadığın sürede değil, oğlun kral olduktan sonra yapacağım.
13 Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
Ama oğlunun elinden bütün krallığı almayacağım. Kulum Davut'un ve kendi seçtiğim Yeruşalim'in hatırı için oğluna bir oymak bırakacağım.”
14 Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
RAB kral soyundan gelen bir düşmanı, Edomlu Hadat'ı Süleyman'a karşı ayaklandırdı.
15 Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
Daha önce, Davut Edomlular'la savaşırken, ölüleri gömmeye giden ordu komutanı Yoav Edom'daki bütün erkekleri öldürmüştü.
16 Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
Yoav ile İsrailliler Edom'daki erkeklerin hepsini yok edinceye dek, altı ay orada kalmışlardı.
17 Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
Ancak genç Hadat, babasının görevlilerinden bazı Edomlular'la birlikte Mısır'a kaçmıştı.
18 Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
Sonra Midyan'dan ayrılıp Paran'a gitmişler, oradan bazı Paranlılar'ı da yanlarına alıp Mısır'a, firavunun yanına gelmişlerdi. Firavun Hadat'a barınak, yiyecek ve toprak sağlamıştı.
19 Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
Hadat firavunun dostluğunu kazandı. Bunun üzerine firavun, kendi karısı Kraliçe Tahpenes'in kızkardeşini Hadat'la evlendirdi.
20 Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
Tahpenes'in kızkardeşi Hadat'a Genuvat adlı bir oğul doğurdu. Tahpenes çocuğu sarayda firavunun çocuklarıyla birlikte büyüttü.
21 Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
Hadat Davut'la ordu komutanı Yoav'ın ölüm haberini Mısır'da duydu. Firavuna, “İzin ver, kendi ülkeme döneyim” dedi.
22 Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
Firavun, “Bir eksiğin mi var, neden ülkene dönmek istiyorsun?” diye sordu. Hadat, “Hayır, ama lütfen gitmeme izin ver” diye yanıtladı.
23 Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
Tanrı, efendisi Sova Kralı Hadadezer'den kaçan bir düşmanı, Elyada oğlu Rezon'u Süleyman'a karşı ayaklandırdı.
24 Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
Davut Sovalılar'a saldırdığında, Rezon çevresine haydutları toplayıp onlara önderlik etmişti. Birlikte Şam'a gitmişler, orada kalıp yönetimi ele geçirmişlerdi.
25 Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
Hadat'ın yaptığı kötülüğün yanısıra, Rezon Süleyman yaşadığı sürece İsrail'in düşmanı oldu; Aram'da krallık yaparak İsrail'den nefret etti.
26 Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
Efrayim oymağından Nevat oğlu Seredalı Yarovam Kral Süleyman'a karşı ayaklandı. Yarovam Süleyman'ın görevlilerindendi. Annesi Serua adlı dul bir kadındı.
27 Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
Yarovam'ın krala karşı ayaklanmasının öyküsü şöyleydi: Süleyman Millo'yu yaptırıp babası Davut'un Kenti'ndeki surların gediğini kapatmıştı.
28 Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
Yarovam çok yetenekli biriydi. Süleyman bu genç adamın ne denli çalışkan olduğunu görünce, Yusuf soyunun bütün ağır işlerinin sorumluluğunu ona verdi.
29 Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
Bir gün Yarovam Yeruşalim'in dışına çıktı. Yolda Şilolu Peygamber Ahiya ile karşılaştı. Ahiya yeni giysisini giymişti. İkisi kent dışında yalnızdılar.
30 ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
Ahiya üzerindeki giysiyi yırtıp on iki parçaya ayırdı
31 Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
ve Yarovam'a, “On parçayı kendine al” dedi, “Çünkü İsrail'in Tanrısı RAB diyor ki, ‘Ben, Süleyman'ın elinden krallığı alıp on oymağı sana vereceğim.
32 Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
Ama kulum Davut'un ve İsrail oymaklarının yaşadığı kentler arasından seçtiğim Yeruşalim Kenti'nin hatırı için bir oymağı onda bırakacağım.
33 Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
Çünkü Süleyman bana sırt çevirip Saydalılar'ın tanrıçası Aştoret'e, Moavlılar'ın ilahı Kemoş'a ve Ammonlular'ın ilahı Molek'e taptı. Kurallarıma, ilkelerime uyup gözümde doğru olanı yapan babası Davut gibi yollarımı izlemedi.
34 “‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
Ama buyruklarıma, kurallarıma bağlı kalan, seçtiğim kulum Davut'un hatırı için Süleyman'ın elinden bütün krallığı almayacağım. Yaşamı boyunca onu önder yapacağım.
35 Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
Ancak krallığı oğlunun elinden alıp on oymağı sana vereceğim.
36 Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
Adımı yerleştirmek için kendime seçtiğim Yeruşalim Kenti'nde kulum Davut için önümde sönmeyen bir ışık olmak üzere Süleyman'ın oğluna bir oymak vereceğim.
37 Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
Sana gelince, seni İsrail Kralı yapacağım. İsrail'i dilediğin gibi yöneteceksin.
38 Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
Kulum Davut gibi isteklerimi yerine getirir, kurallarıma ve buyruklarıma uyar, gözümde doğru olanı yapar, yollarımı izlersen, seninle birlikte olacağım. Davut'a yaptığım gibi senin için de güçlü bir hanedan kurup İsrail'i sana vereceğim.
39 Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
Süleyman'ın günahından ötürü Davut soyunun gururunu kıracağım, ancak sonsuza dek değil.’”
40 Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
Süleyman Yarovam'ı öldürmeye çalıştı. Ama Yarovam Mısır'a kaçıp Mısır Kralı Şişak'a sığındı. Süleyman'ın ölümüne kadar orada kaldı.
41 Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
Süleyman'ın krallığı dönemindeki öteki olaylar, bütün yaptıkları ve bilgeliği Süleyman'ın tarihinde yazılıdır.
42 Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
Süleyman kırk yıl süreyle bütün İsrail'i Yeruşalim'den yönetti.
43 Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.
Süleyman ölüp atalarına kavuşunca babası Davut'un Kenti'nde gömüldü. Yerine oğlu Rehavam kral oldu.

< 1 Mafumu 11 >