< 1 Mafumu 11 >

1 Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
Men kong Salomo elsket mange fremmede kvinner foruten Faraos datter, moabittiske, ammonittiske, edomittiske, sidoniske, hetittiske,
2 Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
kvinner av de hedningefolk om hvilke Herren hadde sagt til Israels barn: I skal ikke gi eder i lag med dem, og de ikke med eder; ellers kommer de visselig til å vende eders hjerte til sine guder. Til dem holdt Salomo sig og elsket dem.
3 Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
Han hadde syv hundre hustruer av fyrstelig rang og tre hundre medhustruer; disse hans hustruer bøide hans sinn.
4 Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
Og da Salomo blev gammel, vendte hustruene hans hjerte til andre guder, og hans hjerte var ikke helt med Herren hans Gud, således som hans far Davids hjerte hadde vært.
5 Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
Og Salomo fulgte Astarte, sidoniernes guddom, og Milkom, ammonittenes vederstyggelighet.
6 Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
Og Salomo gjorde hvad ondt var i Herrens øine, og fulgte ikke trolig efter Herren, således som hans far David hadde gjort.
7 Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
På den tid bygget Salomo en offerhaug for Kamos, Moabs vederstyggelighet, på det fjell som ligger midt imot Jerusalem, og for Molok, Ammons barns vederstyggelighet.
8 Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
Og det samme gjorde han for alle sine fremmede hustruer, som brente røkelse og ofret til sine guder.
9 Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
Da blev Herren vred på Salomo fordi han hadde vendt sitt hjerte bort fra Herren, Israels Gud, som hadde åpenbaret sig for ham to ganger
10 Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
og uttrykkelig forbudt ham å følge andre guder; men han hadde ikke holdt sig efter Herrens bud.
11 Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
Da sa Herren til Salomo: Siden dette er kommet dig i sinne, og du ikke har holdt min pakt og mine lover, som jeg har gitt dig, så vil jeg rive riket fra dig og gi det til din tjener.
12 Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
Men for din far Davids skyld vil jeg ikke gjøre det i din tid - fra din sønn vil jeg rive riket.
13 Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
Dog vil jeg ikke rive hele riket fra ham; en stamme vil jeg gi din sønn for min tjener Davids skyld og for Jerusalems skyld, som jeg har utvalgt.
14 Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
Og Herren opreiste Salomo en motstander i edomitten Hadad; han var av kongeætten i Edom.
15 Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
For dengang David var i Edom, og hærføreren Joab drog op for å begrave de falne og slo ihjel alle menn i Edom.
16 Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
i seks måneder blev Joab og hele Israel der, til han hadde utryddet alle menn i Edom -
17 Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
da flyktet Hadad med nogen edomittiske menn som hørte til hans fars tjenere, og tok veien til Egypten. Hadad var dengang en liten gutt.
18 Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
De brøt op fra Midian og kom til Paran; fra Paran tok de nogen menn med sig og kom så til Egypten til Farao, kongen i Egypten, og han gav ham et hus og tilsa ham livsophold og lot ham få jord.
19 Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
Og Hadad fant stor nåde for Faraos øine, så han gav ham til hustru en søster av sin egen hustru, dronning Tahpenes.
20 Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
Og Tahpenes' søster fødte ham sønnen Genubat; Tahpenes avvente ham i Faraos hus, og siden var Genubat i Faraos hus blandt Faraos egne barn.
21 Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
Da nu Hadad i Egypten fikk høre at David hadde lagt sig til hvile hos sine fedre, og at hærføreren Joab var død, sa han til Farao: La mig fare, så jeg kan dra hjem til mitt land!
22 Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
Farao sa til ham: Hvad fattes dig her hos mig siden du ønsker å dra hjem til ditt land? Han svarte: Ingen ting; men du må endelig la mig få fare.
23 Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
Gud opreiste Salomo en annen motstander, Reson, Eliadas sønn, som var flyktet fra sin herre Hadadeser, kongen i Soba.
24 Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
Han samlet folk om sig og blev fører for en røverflokk, dengang David slo dem ihjel; og de drog til Damaskus og slo sig ned der og gjorde sig til herrer i Damaskus.
25 Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
Han var en motstander av Israel så lenge Salomo levde, og både han og Hadad voldte Israel skade. Han hatet Israel og var konge over Syria.
26 Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
Så var det en av Salomos tjenere, Jeroboam, Nebats sønn, en efra'imitt fra Sereda: hans mor hette Serua og var enke. Han reiste sig også mot kongen.
27 Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
Og således gikk det til at han reiste sig mot kongen: Salomo bygget på Millo - han vilde lukke det åpne sted i sin far Davids stad.
28 Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
Nu var Jeroboam en dyktig kar, og da Salomo så at den unge mann var en duelig arbeider, satte han ham til å ha tilsyn med alt det arbeid Josefs hus hadde å utføre.
29 Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
På den tid hendte det engang da Jeroboam var gått ut fra Jerusalem, at profeten Akia fra Silo traff ham på veien; han hadde en ny kappe på, og de to var alene på marken.
30 ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
Da tok Akia den nye kappe han hadde på, og rev den i tolv stykker.
31 Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
Og han sa til Jeroboam: Ta dig ti stykker! For så sier Herren, Israels Gud: Jeg river riket ut av Salomos hånd og gir dig de ti stammer;
32 Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
men den ene stamme skal han få ha for min tjener Davids skyld og for Jerusalems skyld, den stad som jeg har utvalgt blandt alle Israels stammer.
33 Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
Så vil jeg gjøre fordi de har forlatt mig og tilbedt Astarte, sidoniernes guddom, og Kamos, Moabs gud, og Milkom, Ammons barns gud, og ikke vandret på mine veier og ikke gjort hvad rett er i mine øine, og ikke holdt mine lover og bud, således som hans far David gjorde.
34 “‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
Dog vil jeg ikke ta noget av riket fra ham selv, men la ham være fyrste så lenge han lever, for min tjener Davids skyld, som jeg utvalgte, og som holdt sig efter mine bud og lover.
35 Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
Men jeg vil ta riket fra hans sønn og gi dig det - de ti stammer;
36 Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
men hans sønn vil jeg gi en stamme, forat min tjener David alltid må ha en lampe brennende for mitt åsyn i Jerusalem, den stad jeg har utvalgt mig for å la mitt navn bo der.
37 Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
Men dig vil jeg ta og la dig råde over alt hvad du attrår, og være konge over Israel.
38 Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
Og hvis du hører på alt det jeg byder dig, og vandrer på mine veier og gjør hvad rett er i mine øine, så du holder mine lover og bud, således som min tjener David gjorde, så vil jeg være med dig og bygge dig et hus som står fast, likesom jeg gjorde for David, og jeg vil gi dig Israel.
39 Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
Og Davids ætt vil jeg ydmyke på grunn av det som er gjort, dog ikke for alle tider.
40 Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
Salomo søkte nu å drepe Jeroboam; men Jeroboam tok avsted og flyktet til Egypten, til Sisak, kongen i Egypten, og han blev i Egypten til Salomos død.
41 Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
Hvad som ellers er å fortelle om Salomo, om alt det han gjorde, og om hans visdom, det er opskrevet i Salomos krønike.
42 Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
Den tid Salomo var konge i Jerusalem over hele Israel, var firti år.
43 Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.
Så la Salomo sig til hvile hos sine fedre og blev begravet i sin far Davids stad, og hans sønn Rehabeam blev konge i hans sted.

< 1 Mafumu 11 >