< 1 Mafumu 11 >

1 Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
Inkosi uSolomoni yayithanda-ke abafazi abanengi bezizweni, kanye lendodakazi kaFaro, amaMowabikazi, amaAmonikazi, amaEdomikazi, amaSidonikazi, amaHethikazi,
2 Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
ababevela ezizweni iNkosi eyayithe ngazo kubantwana bakoIsrayeli: Kaliyikungena kibo, labo kabayikungena kini; isibili bazaphendula inhliziyo yenu ilandele onkulunkulu babo. Bona uSolomoni wabanamathela ngothando.
3 Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
Wayelabafazi abangamakhulu ayisikhombisa, amakhosazana, labafazi abancane abangamakhulu amathathu; abafazi bakhe basebephambula inhliziyo yakhe.
4 Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
Ngoba kwathi esikhathini sokuluphala kukaSolomoni, abafazi bakhe baphambulela inhliziyo yakhe ekulandeleni abanye onkulunkulu, lenhliziyo yakhe yayingaphelelanga kuJehova uNkulunkulu wakhe, njengenhliziyo kaDavida uyise.
5 Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
Ngoba uSolomoni wahamba emva kukaAshitarothi unkulunkulu wamaSidoni lemva kukaMilkomu isinengiso samaAmoni.
6 Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
USolomoni wasesenza okubi emehlweni eNkosi, kayilandelanga ngokupheleleyo iNkosi njengoDavida uyise.
7 Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
Ngalesosikhathi uSolomoni wakhela uKemoshi isinengiso sakoMowabi indawo ephakemeyo entabeni ephambi kweJerusalema, loMoleki isinengiso sabantwana bakoAmoni.
8 Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
Langokunjalo wabenzela bonke abafazi bakhe bezizweni abatshisa impepha bahlabela onkulunkulu babo.
9 Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
INkosi yasimthukuthelela uSolomoni, ngoba inhliziyo yakhe yayiphambukile eNkosini, uNkulunkulu kaIsrayeli, eyayibonakele kuye kabili,
10 Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
yamlaya mayelana lalinto, ukuthi angalandeli abanye onkulunkulu; kodwa kagcinanga lokho iNkosi eyamlaya khona.
11 Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
Ngakho iNkosi yathi kuSolomoni: Ngenxa yokuthi lokhu kwenziwe nguwe, ungagcinanga isivumelwano sami lezimiso zami, engakulaya khona, ngizawudabula lokuwudabula umbuso kuwe, ngiwunike inceku yakho.
12 Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
Kanti kangiyikukwenza ensukwini zakho ngenxa kaDavida uyihlo; ngizawudabula usuke esandleni sendodana yakho.
13 Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
Loba kunjalo kangiyikudabula wonke umbuso; ngizanika indodana yakho isizwe esisodwa ngenxa kaDavida inceku yami langenxa yeJerusalema engiyikhethileyo.
14 Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
INkosi yasimvusela uSolomoni isitha, uHadadi umEdoma; wayengowenzalo yenkosi eEdoma.
15 Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
Ngoba kwathi uDavida eseEdoma, uJowabi induna yebutho wayenyukele ukungcwaba ababuleweyo, watshaya wonke owesilisa eEdoma.
16 Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
Ngoba uJowabi wahlala lapho inyanga eziyisithupha, loIsrayeli wonke, waze waquma wonke owesilisa eEdoma.
17 Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
Kodwa uHadadi wabaleka, yena lamaEdoma athile avela encekwini zikayise kanye laye, ukungena eGibhithe; njalo uHadadi wayengumfanyana.
18 Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
Basebesuka eMidiyani, bafika eParani, bathatha amadoda labo eParani, bafika eGibhithe, kuFaro inkosi yeGibhithe, owamnika indlu, wammisela ukudla, wamnika umhlabathi.
19 Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
UHadadi wasethola umusa omkhulu emehlweni kaFaro, waze wamendisela udadewabo womkakhe, udadewabo kaTapenesi indlovukazi.
20 Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
Udadewabo kaTapenesi wasemzalela uGenubathi indodana yakhe, uTapenesi amlumulela phakathi kwendlu kaFaro; njalo uGenubathi wayesendlini kaFaro phakathi kwabantwana bakaFaro.
21 Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
Kwathi uHadadi esezwile eseGibhithe ukuthi uDavida ulele laboyise lokuthi uJowabi induna yebutho usefile, uHadadi wathi kuFaro: Ngivumela ngisuke ukuthi ngiye elizweni lakithi.
22 Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
UFaro wasesithi kuye: Kodwa usweleni ulami ukuthi, khangela, udinge ukuya elizweni lakini? Wasesithi: Akulalutho, loba kunjalo ngivumela lokungivumela ngihambe.
23 Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
UNkulunkulu wasemvusela isitha, uRezoni indodana kaEliyada owayebalekile enkosini yakhe uHadadezeri inkosi yeZoba.
24 Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
Wasezibuthela amadoda, waba ngumkhokheli weviyo, lapho uDavida ebabulala; basebesiya eDamaseko, bahlala kuyo, babusa eDamaseko.
25 Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
Wasesiba yisitha kuIsrayeli insuku zonke zikaSolomoni, phezu kobubi uHadadi abenzayo; njalo wanengwa nguIsrayeli, wabusa phezu kukaSiriya.
26 Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
LoJerobhowamu, indodana kaNebati, umEfrayimi weZereda, inceku kaSolomoni, obizo likanina lalinguZeruwa, owesifazana ongumfelokazi, laye waphakamisa isandla emelene lenkosi.
27 Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
Yilolu-ke udaba lokuthi aphakamise isandla emelene lenkosi. USolomoni wakha iMilo, wavala isikhala somuzi kaDavida uyise.
28 Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
UJerobhowamu wayeliqhawe elilamandla. Kwathi uSolomoni ebona lelijaha ukuthi likhuthele emsebenzini, walibeka phezu kwawo wonke umthwalo wendlu kaJosefa.
29 Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
Kwasekusithi ngalesosikhathi lapho uJerobhowamu ephuma eJerusalema, uAhiya umShilo umprofethi wamfica endleleni. Njalo wayezigqokise isigqoko esitsha; bobabili babebodwa egangeni.
30 ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
UAhiya wasesibamba isigqoko esitsha esasikuye, wasidabula iziqa ezilitshumi lambili,
31 Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
wathi kuJerobhowamu: Zithathele iziqa ezilitshumi, ngoba itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli: Khangela, ngizadabula umbuso usuke esandleni sikaSolomoni, ngikunike izizwe ezilitshumi.
32 Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
Kodwa yena uzakuba lesizwe esisodwa ngenxa yenceku yami uDavida langenxa yeJerusalema, umuzi engiwukhethileyo ezizweni zonke zakoIsrayeli.
33 Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
Ngenxa yokuthi bangitshiyile, bakhonza uAshitarothi unkulunkulu wamaSidoni, uKemoshi unkulunkulu wamaMowabi, loMilkomu unkulunkulu wabantwana bakoAmoni, kabahambanga ngendlela zami, ukwenza okulungileyo emehlweni ami, lokulondoloza izimiso zami lezahlulelo zami, njengoDavida uyise.
34 “‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
Loba kunjalo kangiyikuwususa umbuso wonke esandleni sakhe; kodwa ngizamenza abe ngumbusi zonke izinsuku zempilo yakhe ngenxa kaDavida inceku yami, engamkhethayo, owagcina imilayo yami lezimiso zami.
35 Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
Kodwa ngizawususa umbuso esandleni sendodana yakhe, ngiwunike wena, izizwe ezilitshumi.
36 Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
Lendodana yakhe ngizayinika isizwe sibe sinye ukuze uDavida inceku yami abe lesibane zonke izinsuku phambi kwami eJerusalema, umuzi engizikhethele wona ukuze ngibeke ibizo lami khona.
37 Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
Wena-ke ngizakuthatha, uzabusa phezu kwakho konke umphefumulo wakho okuloyisayo, ube yinkosi phezu kukaIsrayeli.
38 Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
Kuzakuthi-ke, uba ulalela konke engikulaya khona, uhambe ngezindlela zami, wenze okulungileyo emehlweni ami, ukugcina izimiso zami lemilayo yami, njengokwenza kukaDavida inceku yami, ngizakuba lawe, ngikwakhele indlu eqinileyo, njengengayakhela uDavida, ngizakunika uIsrayeli,
39 Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
njalo ngihluphe inzalo kaDavida ngenxa yalokhu, kodwa kungabi kokuphela.
40 Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
Ngakho uSolomoni wadinga ukumbulala uJerobhowamu, kodwa uJerobhowamu wasuka wabalekela eGibhithe, kuShishaki inkosi yeGibhithe, wayeseGibhithe waze wafa uSolomoni.
41 Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
Ezinye-ke zezindaba zikaSolomoni, lakho konke akwenzayo, lenhlakanipho yakhe, kakubhalwanga yini egwalweni lwendaba zikaSolomoni?
42 Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
Isikhathi-ke uSolomoni abusa ngaso eJerusalema phezu kukaIsrayeli wonke saba yiminyaka engamatshumi amane.
43 Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.
USolomoni waselala laboyise, wangcwatshelwa emzini kaDavida uyise. URehobhowamu indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.

< 1 Mafumu 11 >