< 1 Mafumu 11 >
1 Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
Et le roi Salomon aimait les femmes. Il avait sept cents femmes princesses et trois cents concubines. Il avait épousé des femmes étrangères: la fille du Pharaon, puis des Moabites, des Ammonites, des Syriennes, des Iduméennes, des Hettéennes et des Amorrhéennes,
2 Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
Des femmes de ces peuples dont le Seigneur avait dit aux fils d'Israël: «Vous n'aurez point avec eux de commerce, ni eux avec vous, de peur qu'ils ne détournent vos cœurs vers leurs idoles.» Salomon s'était attaché à elles, il les aimait.
3 Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
Et, au temps de sa vieillesse, son cœur ne fut point parfait à l'égard du Seigneur son Dieu, comme le cœur de David, son père. Car les femmes étrangères détournèrent son cœur vers leurs dieux.
4 Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
Et, au temps de sa vieillesse, son cœur ne fut point parfait à l'égard du Seigneur son Dieu, comme le cœur de David, son père. Car les femmes étrangères détournèrent son cœur vers leurs dieux.
5 Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
Alors, Salomon bâtit un haut lieu à Chamos, idole de Moab; à leur roi, idole des fils d'Ammon,
6 Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
Et à Astarté, abomination des Sidoniens.
7 Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
A toutes ses femmes étrangères, il accorda de sacrifier à leurs idoles et de les encenser.
8 Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
Et Salomon fit le mal devant le Seigneur; il ne suivit point le Seigneur, comme l'avait suivi David, son père.
9 Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
Et le Seigneur se courrouça contre Salomon, parce qu'il avait détourné son cœur du Seigneur Dieu d'Israël qui lui était apparu deux fois,
10 Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
Et lui avait expressément commandé de ne jamais suivre d'autres dieux, d'être attentif à faire tout ce qu'avait prescrit le Seigneur Dieu; en effet, son cœur n'était point parfait à l'égard du Seigneur, comme le cœur de David, son père.
11 Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
Et le Seigneur dit à Salomon: En punition de ce que tu as agi de la sorte et n'as point gardé mes commandements et mes ordonnances que je t'avais donnés, je déchirerai dans tes mains ton royaume, et j'en donnerai une part à ton serviteur.
12 Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
Seulement, à cause de David, ton père, je ne ferai point ces choses de ton vivant; je retirerai des mains de ton fils cette part du royaume.
13 Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
Car je ne le lui prendrai pas tout entier; je laisserai un sceptre à ton fils, à cause de David, mon serviteur, et à cause de Jérusalem, ville que j'ai choisie.
14 Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
Et le Seigneur avait suscité des satans contre Salomon: Ader l'Iduméen et Esron, fils d'Eliadaé de Raama, jadis serviteur d'Adadézer, roi de Suba; ils avaient rassemblé des hommes contre lui, et Ader, chef de cette troupe, avait pris Damas; il fut l'ennemi d'Israël tant que vécut Salomon, et il était de la famille des rois de l'Idumée.
15 Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
Or, ceci était advenu: Dans le temps que David exterminait Edom, et que Joab, général de son armée, était à ensevelir les morts, car ils frappaient tous les mâles dans l'Idumée,
16 Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
(Joab y passa six mois avec tout Israël, jusqu'à ce qu'ils eussent détruit tous les mâles de l'Idumée.)
17 Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
Ader s'enfuit emmenant avec lui tous les Iduméens, serviteurs de son père; il se réfugia en Égypte, alors petit enfant;
18 Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
Et des hommes de la ville de Madian s'étaient soulevés; quand Ader et les siens entrèrent dans Pharan, prirent avec eux les hommes, et allèrent chez le Pharaon, roi d'Égypte. Ader fut introduit auprès du Pharaon; le roi lui donna une demeure, et lui assigna des vivres.
19 Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
Et Ader trouva grâce devant le Pharaon, et le roi lui fit épouser la sœur de sa femme Thécémina, la sœur aînée de Thécémina.
20 Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
Cette sœur de Thécémina enfanta pour Ader un fils nommé Ganebath, que Thécémina éleva avec les fils du Pharaon; Ganebath était donc parmi les fils du Pharaon.
21 Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
Lorsque Ader apprit en Égypte que David dormait auprès de ses pères, et que Joab, général de son armée, était mort; il dit au Pharaon: Congédie-moi, et je retournerai dans mon pays.
22 Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
Et le Pharaon répondit à Ader: Que te manque-t-il parmi nous? Pourquoi demandes-tu à retourner en ton pays? Ader reprit: Je désire que tu me congédies. Et il revint en sa contrée.
23 Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
Voilà d'où venait la méchanceté d'Ader, il contristait Israël et il régnait sur Edom.
24 Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
Voilà d'où venait la méchanceté d'Ader, il contristait Israël et il régnait sur Edom.
25 Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
Voilà d'où venait la méchanceté d'Ader, il contristait Israël et il régnait sur Edom.
26 Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
Or, Jéroboam, fils de Nabat l'Ephrathéen de Sarira, fils d'une femme veuve, était serviteur de Salomon.
27 Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
Voici à quelle occasion il leva les mains contre le roi son maître. Le roi Salomon était à bâtir la citadelle, et il entourait de murs l'enceinte de la ville de David.
28 Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
Jéroboam était vaillant, et Salomon discerna que le jeune serviteur était un homme d'action, et il le nomma intendant des tributs de la maison de Joseph.
29 Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
En ce temps-là, Jéroboam sortit de Jérusalem, et il fut rencontré sur la route par Achias, le prophète silonite. Achias se détourna du chemin, et Achias était enveloppé d'un manteau neuf; ils étaient seuls tous les deux dans les champs,
30 ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
Et Achias ôta son manteau neuf et le déchira en douze parts,
31 Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
Et il dit à Jéroboam: Prends pour toi dix de ces lambeaux; car voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël: Je déchirerai entre les mains de Salomon son royaume, et je te donnerai dix tribus.
32 Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
Et il lui restera deux tribus, à cause de mon serviteur David, et à cause de Jérusalem, ville que j'ai choisie parmi toutes les tribus d'Israël.
33 Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
C'est en punition de ce qu'il m'a abandonné; de ce qu'il a sacrifié à Astarté, abomination des Sidoniens, à Chamos, aux idoles de Moab et à leur roi, abomination des fils d'Ammon, et de ce qu'il n'a point marché en toutes mes voies pour faire devant moi ce qui est droit, comme l'a fait David, son père.
34 “‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
Toutefois, je ne retirerai point de sa main le royaume entier; je le lui laisserai même tout le reste de sa vie, à cause de David, son père, mon élu.
35 Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
Mais je prendrai le royaume des mains de son fils, et je te donnerai dix tribus.
36 Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
Et je laisserai à son fils deux tribus, afin qu'il y ait toujours devant moi, pour mon serviteur David, un trône en Jérusalem, dans la ville que je me suis choisie pour que mon nom y résidât.
37 Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
Pour toi, je te prendrai, et tu règneras comme le désire ton âme; tu seras roi d'Israël.
38 Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
Et, si tu observes tout ce que je t'ordonnerai, si tu marches en mes voies, si tu fais devant moi ce qui est droit, en gardant mes commandements et mes ordonnances, comme a fait David, mon serviteur, je serai avec toi, et je te bâtirai une maison sûre, de même que j'en ai bâti une pour David.
39 Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
Et Salomon chercha à faire périr Jéroboam; mais il partit, et s'enfuit auprès de Sésac, roi d'Égypte, et il y demeura jusqu'à la mort de Salomon.
40 Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
Et Salomon chercha à faire périr Jéroboam; mais il partit, et s'enfuit auprès de Sésac, roi d'Égypte, et il y demeura jusqu'à la mort de Salomon.
41 Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
Le reste de l'histoire de Salomon, tout ce qu'il a fait, toute sa sagesse, ne sont-ils pas écrits au livre de la vie de Salomon?
42 Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
Salomon régna quarante ans sur tout Israël.
43 Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.
Et il s'endormit avec ses pères, et on l'ensevelit en la ville de David, et Roboam, son fils, régnait à sa place.