< 1 Yohane 5 >
1 Aliyense amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Khristu, iyeyo ndi mwana wa Mulungu, ndipo aliyense amene amakonda Atate amakondanso Mwana wake.
Ech man that bileueth that Jhesus is Crist, is borun of God; and ech man that loueth hym that gendride, loueth hym that is borun of hym.
2 Chodziwira kuti timakonda ana a Mulungu nʼchakuti timakonda Mulungu ndi kusunga malamulo ake.
In this thing we knowen, that we louen the children of God, whanne we louen God, and don his maundementis.
3 Pakuti kukonda Mulungu ndiye kusunga malamulo ake. Ndipo malamulo ake siwolemetsa,
For this is the charite of God, that we kepe hise maundementis; and his maundementis ben not heuy.
4 chifukwa aliyense amene ndi mwana wa Mulungu amagonjetsa dziko lapansi. Chikhulupiriro chathu ndicho timagonjetsera dziko lapansi.
For al thing that is borun of God, ouercometh the world; and this is the victorie that ouercometh the world, oure feith.
5 Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Yekhayo amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.
And who is he that ouercometh the world, but he that bileueth that Jhesus is the sone of God?
6 Uyu ndiye anabwera mwa madzi ndi magazi, ndiye Yesu Khristu. Sanabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi magazi. Ndipo ndi Mzimu Woyera amene akuchitira umboni, chifukwa Mzimu Woyera ndi choonadi.
This is Jhesus Crist, that cam bi watir and blood; not in water oonli, but in watir and blood. And the spirit is he that witnessith, that Crist is treuthe.
7 Pakuti pali atatu amene amachitira umboni.
For thre ben, that yyuen witnessing in heuene, the Fadir, the Sone, and the Hooli Goost; and these thre ben oon.
8 Mzimu Woyera, madzi ndi magazi; ndipo atatu amavomerezana.
`And thre ben, that yyuen witnessing in erthe, the spirit, water, and blood; and these thre ben oon.
9 Timalandira umboni wa anthu, koma umboni wa Mulungu ndi wopambana. Umboniwo ndi umene anachitira Mwana wake.
If we resseyuen the witnessing of men, the witnessing of God is more; for this is the witnessing of God, that is more, for he witnesside of his sone.
10 Aliyense amene amakhulupirira Mwana wa Mulungu ali nawo umboniwu mu mtima mwake, koma aliyense amene sanakhulupirire Mulungu amayesa kuti Mulunguyo ndi wonama, chifukwa sanakhulupirire umboni umene Mulungu anachitira wa Mwana wake.
He that bileueth in the sone of God, hath the witnessing of God in hym. He that bileueth not to the sone, makith hym a liere; for he bileueth not in the witnessing, that God witnesside of his sone.
11 Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. (aiōnios )
And this is the witnessyng, for God yaf to you euerlastinge lijf, and this lijf is in his sone. (aiōnios )
12 Iye amene ali ndi Mwana ali ndi moyo, amene alibe Mwana wa Mulungu alibe moyo.
He that hath the sone of God, hath also lijf; he that hath not the sone of God, hath not lijf.
13 Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. (aiōnios )
I write to you these thingis, that ye wite, that ye han euerlastynge lijf, which bileuen in the name of Goddis sone. (aiōnios )
14 Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera.
And this is the trist which we han to God, that what euer thing we axen aftir his wille, he schal here vs.
15 Ndipo ngati tikudziwa kuti amatimvera, chilichonse chimene timapempha, tikudziwanso kuti tili nacho chimene tamupempha Iye.
And we witen, that he herith vs, what euer thing we axen; we witen, that we han the axyngis, which we axen of hym.
16 Ngati wina aona mʼbale wake akuchita tchimo losadzetsa imfa, apemphere ndipo Mulungu adzamupatsa moyo mʼbale wakeyo. Ndikunena za ochita tchimo losadzetsa imfa. Pali tchimo lodzetsa imfa. Ine sindikunena kuti apemphere ayi.
He that woot that his brother synneth a synne not to deth, axe he, and lijf schal be youun to hym that synneth not to deth. Ther is a synne to deth; `not for it Y seie, that ony man preie.
17 Chilichonse chosalungama ndi tchimo ndipo pali tchimo losadzetsa imfa.
Ech wickidnesse is synne, and ther is synne to deth.
18 Tikudziwa kuti aliyense amene ndi mwana wa Mulungu sachimwirachimwirabe. Yesu, Mwana wa Mulungu, amamusunga ndipo woyipa uja sangamukhudze.
We witen, that ech man that is borun of God, synneth not; but the generacioun of God kepith hym, and the wickid touchith hym not.
19 Tikudziwa kuti ndife ana a Mulungu ndi kuti dziko lonse lapansi lili pansi pa ulamuliro wa woyipayo.
We witen, that we ben of God, and al the world is set in yuel.
20 Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha. (aiōnios )
And we witen, that the sone of God cam in fleisch, and yaf to vs wit, that we know veri God, and be in the veri sone of hym. This is veri God, and euerlastynge lijf. (aiōnios )
21 Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.
My litle sones, kepe ye you fro maumetis.