< 1 Yohane 5 >

1 Aliyense amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Khristu, iyeyo ndi mwana wa Mulungu, ndipo aliyense amene amakonda Atate amakondanso Mwana wake.
Whoever believes that Jesus is the Messiah is born of God. Whoever loves the Father also loves the child who is born of him.
2 Chodziwira kuti timakonda ana a Mulungu nʼchakuti timakonda Mulungu ndi kusunga malamulo ake.
By this we know that we love the children of God, when we love God and do his commandments.
3 Pakuti kukonda Mulungu ndiye kusunga malamulo ake. Ndipo malamulo ake siwolemetsa,
For this is the love of God, that we keep his commandments. His commandments are not grievous.
4 chifukwa aliyense amene ndi mwana wa Mulungu amagonjetsa dziko lapansi. Chikhulupiriro chathu ndicho timagonjetsera dziko lapansi.
For whatever is born of God overcomes the world. This is the victory that has overcome the world: our faith.
5 Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Yekhayo amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.
Who is he who overcomes the world, but he who believes that Jesus is the Son of God?
6 Uyu ndiye anabwera mwa madzi ndi magazi, ndiye Yesu Khristu. Sanabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi magazi. Ndipo ndi Mzimu Woyera amene akuchitira umboni, chifukwa Mzimu Woyera ndi choonadi.
This is he who came by water and blood, Jesus (the) Messiah; not with the water only, but with the water and the blood. It is the Spirit who testifies, because the Spirit is the truth.
7 Pakuti pali atatu amene amachitira umboni.
For there are three who testify:
8 Mzimu Woyera, madzi ndi magazi; ndipo atatu amavomerezana.
the Spirit, the water, and the blood; and the three agree as one.
9 Timalandira umboni wa anthu, koma umboni wa Mulungu ndi wopambana. Umboniwo ndi umene anachitira Mwana wake.
If we accept human testimony, the witness of God is greater; for this is God's testimony that he has testified concerning his Son.
10 Aliyense amene amakhulupirira Mwana wa Mulungu ali nawo umboniwu mu mtima mwake, koma aliyense amene sanakhulupirire Mulungu amayesa kuti Mulunguyo ndi wonama, chifukwa sanakhulupirire umboni umene Mulungu anachitira wa Mwana wake.
He who believes in the Son of God has the testimony in himself. He who does not believe God has made him a liar, because he has not believed in the testimony that God has given concerning his Son.
11 Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. (aiōnios g166)
The testimony is this, that God gave to us everlasting life, and this life is in his Son. (aiōnios g166)
12 Iye amene ali ndi Mwana ali ndi moyo, amene alibe Mwana wa Mulungu alibe moyo.
He who has the Son has the life. He who does not have God's Son does not have the life.
13 Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
These things I have written to you who believe in the name of the Son of God, that you may know that you have everlasting life. (aiōnios g166)
14 Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera.
This is the boldness which we have toward him, that, if we ask anything according to his will, he listens to us.
15 Ndipo ngati tikudziwa kuti amatimvera, chilichonse chimene timapempha, tikudziwanso kuti tili nacho chimene tamupempha Iye.
And if we know that he listens to us, whatever we ask, we know that we have the petitions which we have asked of him.
16 Ngati wina aona mʼbale wake akuchita tchimo losadzetsa imfa, apemphere ndipo Mulungu adzamupatsa moyo mʼbale wakeyo. Ndikunena za ochita tchimo losadzetsa imfa. Pali tchimo lodzetsa imfa. Ine sindikunena kuti apemphere ayi.
If anyone sees his brother sinning a sin not leading to death, he should ask, and he will give him life for those who sin not leading to death. There is a sin leading to death. I do not say that he should make a request concerning this.
17 Chilichonse chosalungama ndi tchimo ndipo pali tchimo losadzetsa imfa.
All unrighteousness is sin, and there is a sin not leading to death.
18 Tikudziwa kuti aliyense amene ndi mwana wa Mulungu sachimwirachimwirabe. Yesu, Mwana wa Mulungu, amamusunga ndipo woyipa uja sangamukhudze.
We know that whoever is born of God does not sin, but he who was born of God protects him, and the evil one does not touch him.
19 Tikudziwa kuti ndife ana a Mulungu ndi kuti dziko lonse lapansi lili pansi pa ulamuliro wa woyipayo.
We know that we are of God, and the whole world lies in the power of the evil one.
20 Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
We know that the Son of God has come, and has given us an understanding, that we know him who is true, and we are in him who is true, in his Son Jesus (the) Messiah. He is the true God and eternal life. (aiōnios g166)
21 Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.
Little children, keep yourselves from idols.

< 1 Yohane 5 >