< 1 Yohane 4 >
1 Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi.
My beloved, believe not all spirits; but discriminate among spirits, whether they are of God: for many false prophets have gone out into the world.
2 Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu,
By this the Spirit of God is known, every spirit that confesseth that Jesus the Messiah hath come in the flesh, is of God.
3 koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.
And every spirit which confesseth not that Jesus the Messiah hath come in the flesh, is not of God; but he is of the false Messiah, of whom ye have heard that he cometh, and now is he already in the world.
4 Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi.
But ye children, are of God; and ye have overcome them, because greater is he who is in you, than he who is in the world.
5 Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera.
And they are of the world: therefore they speak from the world, and the world heareth them.
6 Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.
But we are of God; and he that knoweth God, heareth us; and he that is not of God, heareth us not. By this, we know the spirit of truth, and the spirit of error.
7 Anzanga okondedwa, tiyeni tikondane wina ndi mnzake, pakuti chikondi chimachokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi ndi mwana wa Mulungu ndipo amadziwa Mulungu.
My beloved, let us love one another: because love is from God; and whoever loveth, is born of God and knoweth God.
8 Aliyense amene alibe chikondi sadziwa Mulungu, chifukwa Mulungu ndiye chikondi.
Because God is love; and whoever loveth not, doth not know God.
9 Mmene Mulungu anaonetsera chikondi chake pakati pathu ndi umu: Iye anatumiza Mwana wake mmodzi yekha ku dziko lapansi kuti mwa Iyeyo tikhale ndi moyo.
By this was the love of God towards us made known, because God sent his only-begotten Son into the world, that we by him might live.
10 Chikondi ndi ichi: osati kuti ife ndife amene tinamukonda Mulungu, koma kuti Iyeyo ndiye amene anatikonda ndipo anatumiza Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu.
In this is love; it was not that we loved God, but that God loved us, and sent his Son a propitiation for our sins.
11 Anzanga okondedwa, popeza Mulungu anatikonda chotere, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake.
My beloved, if God hath so loved us, we also ought to love one another.
12 Palibe amene anaonapo Mulungu, koma tikakondana wina ndi mnzake, ndiye kuti Mulungu amakhala mwa ife ndipo chikondi chake chafika pachimake penipeni mwa ife.
No one hath ever seen God; but if we love one another, God abideth in us, and his love is perfected in us.
13 Ife tikudziwa kuti timakhala mwa Iye ndipo Iyeyo amakhala mwa ife chifukwa anatipatsa Mzimu wake.
And by this we know, that we abide in him and that he abideth in us, because he hath given of his Spirit to us.
14 Ndipo taona ndipo tikuchitira umboni, kuti Atate anatuma Mwana wake kuti akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi.
And we have seen, and do testify, that the Father hath sent his Son, a Redeemer for the world.
15 Ngati aliyense avomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye ndipo iyeyo amakhala mwa Mulungu.
Whoever confesseth Jesus to be the Son of God, God abideth in him, and he abideth in God.
16 Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife. Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye.
And we have believed and known the love, which God hath towards us: for God is love, and whoever abideth in love, abideth in God.
17 Chikondi chafika pachimake penipeni pakati pathu, kotero kuti pa tsiku lachiweruzo tidzakhala olimba mtima chifukwa mʼdziko lapansi moyo wathu uli ngati wa Khristu.
And hereby is his love perfected with us; that we may have open countenances in the day of judgment; because as he was, so also are we in this world.
18 Mulibe mantha mʼchikondi. Koma chikondi ndi changwiro chimachotsa mantha, chifukwa mantha amabwera chifukwa choopa chilango. Munthu amene ali ndi mantha, chikondi chake sichangwiro.
In love there is no fear; but perfect love casteth out fear; because fear existeth in peril, and he that feareth is not perfected in love.
19 Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye anayamba kutikonda.
Let us, therefore, love God; because he hath first loved us.
20 Ngati wina anena kuti, “Ine ndimakonda Mulungu,” koma namadana ndi mʼbale wake ndi wabodza ameneyo. Pakuti aliyense amene sakonda mʼbale wake, amene akumuona, sangathenso kukonda Mulungu amene sanamuone.
And if any one shall say, I love God, and yet hateth his brother, he is a liar: for he that loveth not his brother who is visible, how can he love God who is invisible?
21 Ndipo Iye anatipatsa lamulo lakuti: Aliyense amene amakonda Mulungu ayenera kukondanso mʼbale wake.
And this command we have received from him, that whoever loveth God, must love also his brother.