< 1 Yohane 3 >
1 Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye.
Behold, what manner of love the Father hath bestowed upon us, that we should be called the sons of God: therefore the world knoweth us not, because it knew him not.
2 Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili.
Beloved, now are we the sons of God, and it doth not yet appear what we shall be: but we know that, when he shall appear, we shall be like him; for we shall see him as he is.
3 Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.
And every man that hath this hope in him purifieth himself, even as he is pure.
4 Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo.
Whoever committeth sin transgresseth also the law; for sin is the transgression of the law.
5 Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo.
And ye know that he was manifested to take away our sins; and in him is no sin.
6 Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.
Whoever abideth in him sinneth not: whoever sinneth hath not seen him, neither known him.
7 Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama.
Little children, let no man deceive you: he that doeth righteousness is righteous, even as he is righteous.
8 Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi.
He that committeth sin is of the devil; for the devil sinneth from the beginning. For this purpose the Son of God was manifested, that he might destroy the works of the devil.
9 Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu.
Whoever is born of God doth not commit sin; for his seed remaineth in him: and he cannot sin, because he is born of God.
10 Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.
In this the children of God are manifest, and the children of the devil: whoever doeth not righteousness is not of God, neither he that loveth not his brother.
11 Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake.
For this is the message that ye have heard from the beginning, that we should love one another.
12 Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama.
Not as Cain, [who] was of that wicked one, and slew his brother. And why did he slay him? Because his own works were evil, and his brother's righteous.
13 Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu.
Marvel not, my brethren, if the world hate you.
14 Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa.
We know that we have passed from death to life, because we love the brethren. He that loveth not [his] brother, abideth in death.
15 Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios )
Whoever hateth his brother, is a murderer: and ye know that no murderer hath eternal life abiding in him. (aiōnios )
16 Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu.
By this we perceive the love [of God], because he laid down his life for us: and we ought to lay down [our] lives for the brethren.
17 Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu?
But he who hath this world's good, and seeth his brother have need, and shutteth up his bowels [of compassion] from him, how dwelleth the love of God in him?
18 Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi.
My little children, let us not love in word, neither in tongue, but in deed and in truth.
19 Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu,
And by this we know that we are of the truth, and shall assure our hearts before him.
20 nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.
For if our heart condemneth us, God is greater than our heart, and knoweth all things.
21 Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu.
Beloved, if our heart doth not condemn us, [then] have we confidence towards God.
22 Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa.
And whatever we ask, we receive from him, because we keep his commandments, and do those things that are pleasing in his sight.
23 Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira.
And this is his commandment; That we should believe on the name of his Son Jesus Christ, and love one another, as he gave us commandment.
24 Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.
And he that keepeth his commandments, dwelleth in him, and he in him. And by this we know that he abideth in us, by the Spirit which he hath given us.