< 1 Yohane 2 >

1 Inu Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zimenezi kuti musachimwe. Koma wina akachimwa, tili nayo Nkhoswe yotinenera kwa Atate, Yesu Khristu, Wolungamayo.
ای فرزندان من، این را به شما می‌نویسم تاگناه نکنید؛ و اگر کسی گناهی کند، شفیعی داریم نزد پدر یعنی عیسی مسیح عادل.۱
2 Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso machimo onse a dziko lapansi.
واوست کفاره بجهت گناهان ما و نه گناهان ما فقطبلکه بجهت تمام جهان نیز.۲
3 Ife timatsimikiza kuti tikumudziwa ngati tikusunga malamulo ake.
و از این می‌دانیم که او را می‌شناسیم، اگر احکام او را نگاه داریم.۳
4 Munthu akamanena kuti, “Ine ndimadziwa Mulungu,” koma samvera malamulo a Mulunguyo, ndi wabodza ameneyo ndipo mwa iye mulibe choonadi.
کسی‌که گوید او را می‌شناسم و احکام او رانگاه ندارد، دروغگوست و در وی راستی نیست.۴
5 Koma munthu aliyense akamvera mawu ake, ndiye kuti chikondi cha Mulungu chafikadi penipeni mwa iyeyo. Pamenepo timatsimikizadi kuti tili mwa Iye.
لکن کسی‌که کلام او را نگاه دارد، فی الواقع محبت خدا در وی کامل شده است و از این می‌دانیم که در وی هستیم.۵
6 Aliyense amene amati amakhala mwa Mulungu, ayenera kukhala moyo umene Yesu ankakhala.
هرکه گوید که در وی می‌مانم، به همین طریقی که او سلوک می‌نمود، اونیز باید سلوک کند.۶
7 Okondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lakale lomwe lija, limene munali nalo kuyambira pachiyambi. Lamulo la kalelo ndi mawu amene munawamva kale.
‌ای حبیبان، حکمی تازه به شما نمی نویسم، بلکه حکمی کهنه که آن را از ابتدا داشتید؛ و حکم کهنه آن کلام است که از ابتدا شنیدید.۷
8 Komabe ndi lamulo latsopano limene ndikukulemberani. Choonadi chake chikuoneka mwa Yesu ndiponso mwa inu, chifukwa mdima ukutha ndipo kuwunika kwenikweni kwayamba kale kuwala.
و نیزحکمی تازه به شما می‌نویسم که آن در وی و درشما حق است، زیرا که تاریکی درگذر است و نورحقیقی الان می‌درخشد.۸
9 Aliyense amene amati ali mʼkuwunika, koma nʼkumadana ndi mʼbale wake ali mu mdima.
کسی‌که می‌گوید که در نور است و از برادرخود نفرت دارد، تا حال در تاریکی است.۹
10 Aliyense amene amakonda mʼbale wake amakhalanso mʼkuwunika, ndipo mwa iye mulibe chokhumudwitsa.
وکسی‌که برادر خود را محبت نماید، در نور ساکن است و لغزش در وی نیست.۱۰
11 Koma aliyense wodana ndi mʼbale wake ali mu mdima ndipo akuyenda mu mdima. Iyeyo sakudziwa kumene akupita, chifukwa mdima wamudetsa mʼmaso mwake.
اما کسی‌که ازبرادر خود نفرت دارد، در تاریکی است و درتاریکی راه می‌رود و نمی داند کجا می‌رود زیرا که تاریکی چشمانش را کور کرده است.۱۱
12 Inu ana okondedwa, ndikukulemberani popeza kuti machimo anu akhululukidwa chifukwa cha dzina la Yesu.
‌ای فرزندان، به شما می‌نویسم زیرا که گناهان شما بخاطر اسم او آمرزیده شده است.۱۲
13 Inu abambo, ndikukulemberani popeza kuti munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi. Inu anyamata, ndikukulemberani popeza kuti munagonjetsa woyipayo.
‌ای پدران، به شما می‌نویسم زیرا او را که ازابتدا است می‌شناسید. ای جوانان، به شمامی نویسم از آنجا که بر شریر غالب شده‌اید. ای بچه‌ها به شما نوشتم زیرا که پدر را می‌شناسید.۱۳
14 Ana okondedwa, ndikukulemberani chifukwa mumawadziwa Atate. Abambo, ndikukulemberani chifukwa munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi. Inu anyamata, ndikukulemberani chifukwa ndinu amphamvu. Mawu a Mulungu amakhala mwa inu ndipo mumamugonjetsa woyipayo.
‌ای پدران، به شما نوشتم زیرا او را که ازابتداست می‌شناسید. ای جوانان، به شما نوشتم از آن جهت که توانا هستید و کلام خدا در شماساکن است وبر شریر غلبه یافته‌اید.۱۴
15 Musamakonde dziko lapansi kapena chilichonse cha dziko lapansi. Ngati munthu wina aliyense akonda dziko lapansi, mwa iyeyo mulibe chikondi chokonda Atate.
دنیا را وآنچه در دنیاست دوست مدارید زیرا اگر کسی دنیا را دوست دارد، محبت پدر در وی نیست.۱۵
16 Pakuti zonse za mʼdziko lapansi, zilakolako za thupi, zinthu zimene maso amakhumbira ndiponso kuyandikira zinthu za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi.
زیرا که آنچه در دنیاست، از شهوت جسم وخواهش چشم و غرور زندگانی از پدر نیست بلکه از جهان است.۱۶
17 Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya. (aiōn g165)
و دنیا و شهوات آن در گذراست لکن کسی‌که به اراده خدا عمل می‌کند، تا به ابد باقی می‌ماند. (aiōn g165)۱۷
18 Ana anga, ino ndi nthawi yotsiriza, ndipo monga munamva kale kuti anthu okana Khristu akubwera, ngakhale tsopano okana Khristu ambiri afika kale. Zimenezi zikutisonyeza kuti ino ndi nthawi yotsiriza.
‌ای بچه‌ها، این ساعت آخر است و چنانکه شنیده‌اید که دجال می‌آید، الحال هم دجالان بسیار ظاهر شده‌اند و از این می‌دانیم که ساعت آخر است.۱۸
19 Anthu amenewa anachoka pakati pathu, komatu sanali a mʼgulu lathu. Pakuti akanakhala a mʼgulu lathu, akanakhalabe nafe, koma kuchoka kwawo kunatisonyeza kuti sanali a mʼgulu lathu.
از ما بیرون شدند، لکن از ما نبودند، زیرا اگر از ما می‌بودند با ما می‌ماندند؛ لکن بیرون رفتند تا ظاهر شود که همه ایشان از ما نیستند.۱۹
20 Koma inu muli ndi kudzoza kochokera kwa Woyerayo, ndipo nonsenu mukudziwa choonadi.
و اما شما از آن قدوس، مسح را یافته‌اید وهرچیز را می‌دانید.۲۰
21 Sindikukulemberani chifukwa choti simudziwa choonadi ayi, koma chifukwa choti mumadziwa choonadicho, ndipo mukudziwanso kuti bodza silichokera pa choonadi.
ننوشتم به شما از این جهت که راستی را نمی دانید، بلکه از اینرو که آن رامی دانید و اینکه هیچ دروغ از راستی نیست.۲۱
22 Wabodzayo ndani? Ndi munthu aliyense amene amanena kuti Yesu si Mpulumutsi. Munthu woteroyo ndi wokana Khristu, ndiponso amakana Atate, ndi Mwana.
دروغگو کیست جز آنکه مسیح بودن عیسی راانکار کند. آن دجال است که پدر و پسر را انکارمی نماید.۲۲
23 Aliyense wokana Mwana alibenso Atate. Wovomereza Mwana alinso ndi Atate.
کسی‌که پسر را انکار کند، پدر را هم ندارد و کسی‌که اعتراف به پسر نماید، پدر را نیزدارد.۲۳
24 Onetsetsani kuti zimene munazimva kuyambira pachiyambi zikhalebe mwa inu. Ngati zikhala mwa inu, inunso mudzakhala mwa Mwana ndiponso mwa Atate.
و اما شما آنچه از ابتدا شنیدید در شماثابت بماند، زیرا اگر آنچه از اول شنیدید، در شماثابت بماند، شما نیز در پسر و در پدر ثابت خواهید ماند.۲۴
25 Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha. (aiōnios g166)
و این است آن وعده‌ای که او به ما داده است، یعنی حیات جاودانی. (aiōnios g166)۲۵
26 Ine ndikukulemberani zimenezi kuti ndikuwuzeni za amene akufuna kukusocheretsani.
و این را به شما نوشتم درباره آنانی که شما را گمراه می‌کنند.۲۶
27 Koma za inu, kudzoza kumene munalandira kwa Khristu kuli mwa inu, ndipo sipafunika wina aliyense kuti akuphunzitseni. Koma kudzozako kumakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo popeza kudzoza kwakeko nʼkoona osati konama, monga munaphunzira, khalani mwa Iyeyo.
و اما در شما آن مسح که از او یافته‌اید ثابت است و حاجت ندارید که کسی شما را تعلیم دهدبلکه چنانکه خود آن مسح شما را از همه‌چیزتعلیم می‌دهد و حق است و دروغ نیست، پس بطوری که شما را تعلیم داد در او ثابت می‌مانید.۲۷
28 Tsopano ana okondedwa, khalani mwa Yesu, kuti pamene adzaonekera, ife tidzakhale otsimikizika mu mtima ndi wopanda manyazi pamaso pake akamadzabwera.
الان‌ای فرزندان در او ثابت بمانید تا چون ظاهر شود، اعتماد داشته باشیم و در هنگام ظهورش از وی خجل نشویم.۲۸
29 Popeza mukudziwa kuti Khristu ndi wolungama, choncho mukudziwanso kuti aliyense amene amachita chilungamo ndi mwana wa Mulungu.
اگر فهمیده ایدکه او عادل است، پس می‌دانید که هر‌که عدالت رابه‌جا آورد، از وی تولد یافته است.۲۹

< 1 Yohane 2 >