< 1 Yohane 1 >

1 Tikukulalikirani za Mawu a moyo amene analipo kuyambira pachiyambi, amene tinawamva, amene tinawaona ndi maso athu, amene tinawapenyetsetsa, ndipo tinawakhudza ndi manja athu.
WE announce to you that, which was from the beginning, which we have heard, and have seen with our eyes, looked upon, and handled with our hands, that which is the word of life.
2 Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios g166)
And the life was manifested, and we have seen and do testify and announce to you, the life which is eternal; which was with the Father, and was revealed to us. (aiōnios g166)
3 Tikukulalikirani chimene tinachiona ndi kumva, kuti inuyo muyanjane nafe. Kuyanjana kwathu, tikuyanjana ndi Atate ndiponso ndi Mwana wawo, Yesu Khristu.
And what we have seen and heard, we make known to you also, that ye may have fellowship with us; and our fellowship is with the Father, and with his Son Jesus the Messiah.
4 Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.
And these things we write to you, that our joy in you may be complete.
5 Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse.
And this is the announcement, which we have heard from him and declare to you, that God is light, and no darkness at all is in him.
6 Tikanena kuti timayanjana naye, koma nʼkumayendabe mu mdima, tikunama ndipo sitikuchita choonadi.
And if we say that we have fellowship with him, and we walk in the darkness, we are liars, and walk not in the truth.
7 Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.
But if we walk in the light, as he is in the light, we have fellowship with each other and the blood of Jesus his Son cleanseth us from all our sins.
8 Tikanena kuti tilibe tchimo, tikudzinyenga tokha ndipo mwa ife mulibe choonadi.
And if we say that we have no sin, we deceive ourselves, and the truth is not in us.
9 Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.
But if we confess our sins, he is faithful and righteous, to forgive us our sins, and to cleanse us from all our iniquity.
10 Ife tikanena kuti sitinachimwe, tikumutenga Mulungu kukhala wonama, ndipo Mawu ake sali mwa ife.
If we say that we have not sinned, we make him a liar, and his word is not with us.

< 1 Yohane 1 >