< 1 Yohane 1 >

1 Tikukulalikirani za Mawu a moyo amene analipo kuyambira pachiyambi, amene tinawamva, amene tinawaona ndi maso athu, amene tinawapenyetsetsa, ndipo tinawakhudza ndi manja athu.
That which was from the beginning, that which we have heard, that which we have witnessed with our eyes, that which we contemplated and our hands handled with reference to the word of the Life
2 Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios g166)
—oh yes, the Life was manifested, and we have seen and testify and declare to you that eternal Life who was in the presence of the Father and was manifested to us— (aiōnios g166)
3 Tikukulalikirani chimene tinachiona ndi kumva, kuti inuyo muyanjane nafe. Kuyanjana kwathu, tikuyanjana ndi Atate ndiponso ndi Mwana wawo, Yesu Khristu.
that which we have seen and heard we declare to you, so that you also may have fellowship with us; indeed, our fellowship is with the Father and with His Son, Jesus Christ.
4 Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.
Yes, we write these things to you so that our joy may be fulfilled.
5 Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse.
Now this is the message that we have heard from Him and declare to you, that God is light and there is no darkness at all in Him.
6 Tikanena kuti timayanjana naye, koma nʼkumayendabe mu mdima, tikunama ndipo sitikuchita choonadi.
If we claim that we have fellowship with Him while walking in the darkness, we are lying and not living the truth.
7 Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.
But if we walk in the light just as He is in the light, we have fellowship with one another, and the blood of Jesus Christ His Son cleanses us from all sin.
8 Tikanena kuti tilibe tchimo, tikudzinyenga tokha ndipo mwa ife mulibe choonadi.
If we claim that we have no sin, we are deceiving ourselves and the Truth is not in us.
9 Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.
If we confess our sins, He is faithful and righteous so as to forgive us those sins and to cleanse us from all unrighteousness.
10 Ife tikanena kuti sitinachimwe, tikumutenga Mulungu kukhala wonama, ndipo Mawu ake sali mwa ife.
If we claim that we have not sinned, we call Him a liar and His Word is not in us.

< 1 Yohane 1 >