< 1 Yohane 1 >

1 Tikukulalikirani za Mawu a moyo amene analipo kuyambira pachiyambi, amene tinawamva, amene tinawaona ndi maso athu, amene tinawapenyetsetsa, ndipo tinawakhudza ndi manja athu.
Det, som var fra Begyndelsen, det, vi have hørt, det, vi have set med vore Øjne, det, vi skuede og vore Hænder følte på, nemlig om Livets Ord; -
2 Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios g166)
og Livet blev åbenbaret, og vi have set og vidne og forkynde eder det evige Liv, som jo var hos Faderen og blev åbenbaret for os; - (aiōnios g166)
3 Tikukulalikirani chimene tinachiona ndi kumva, kuti inuyo muyanjane nafe. Kuyanjana kwathu, tikuyanjana ndi Atate ndiponso ndi Mwana wawo, Yesu Khristu.
hvad vi have set og hørt, forkynde vi også eder, for at også I må have Samfund med os; men vort Samfund er med Faderen og med hans Søn Jesus Kristus.
4 Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.
Og dette skrive vi til eder, for at eders Glæde må være fuldkommen.
5 Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse.
Og dette er det Budskab, som vi have hørt af ham og forkynde eder, at Gud er Lys, og der er slet intet Mørke i ham.
6 Tikanena kuti timayanjana naye, koma nʼkumayendabe mu mdima, tikunama ndipo sitikuchita choonadi.
Dersom vi sige, at vi have Samfund med ham, og vandre i Mørket, da lyve vi og gøre ikke Sandheden.
7 Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.
Men dersom vi vandre i Lyset, ligesom han er i Lyset, have vi Samfund med hverandre, og Jesu, hans Søns, Blod renser os fra al Synd.
8 Tikanena kuti tilibe tchimo, tikudzinyenga tokha ndipo mwa ife mulibe choonadi.
Dersom vi sige, at vi ikke have Synd, bedrage vi os selv, og Sandheden er ikke i os.
9 Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.
Dersom vi bekende vore Synder, er han trofast og retfærdig, så at han forlader os Synderne og renser os fra al Uretfærdighed.
10 Ife tikanena kuti sitinachimwe, tikumutenga Mulungu kukhala wonama, ndipo Mawu ake sali mwa ife.
Dersom vi sige, at vi ikke have syndet, gøre vi ham til en Løgner, og hans Ord er ikke i os.

< 1 Yohane 1 >