< 1 Akorinto 6 >
1 Pamene wina wa inu ali ndi mlandu ndi mnzake, nʼchifukwa chiyani amatengera nkhaniyo kwa anthu akunja kuti akawaweruze mʼmalo mopita nayo kwa oyera mtima?
If any of you has a dispute against another, does he dare go to court before the unrighteous, instead of the saints?
2 Kodi inu simukudziwa kuti anthu a Mulungu adzaweruza dziko lapansi? Ndipo ngati inu mungaweruze dziko lapansi, kodi sindinu oyenera kuweruza milandu ingʼonoyingʼono?
Do you not know that the saints will judge the world? And if the world is judged by you, are you unworthy to judge the smallest matters?
3 Kodi simukudziwa kuti mudzaweruza angelo? Nanga bwanji zinthu za mʼmoyo uno!
Do you not know that we will judge angels? How much more, things that pertain to this life?
4 Nʼchifukwa chake, ngati pali milandu pa zinthu zotere, sankhani anthu ena kuti akhale oweruza ngakhale alibe udindo mu mpingo.
If then, you have to judge things pertaining to this life, do you set them to judge who have no standing in the church?
5 Ndikunena izi kuti ndikuchititseni manyazi. Moti nʼkutheka kuti pakati panu palibe wina wanzeru zokwanira kuti aziweruza mlandu pakati pa Akhristu?
I say this to move you to shame. Is not there even one wise person among you who would be able to decide between a brother and his brother?
6 Koma mʼmalo mwake mʼbale atengera ku bwalo la mlandu mʼbale mnzake kukaweruzidwa. Zonsezi pamaso pa akunja!
But brother goes to law with brother, and that before unbelievers.
7 Chokha choti mwakasumirana chikuonetseratu kuti mwagonjetsedwa kale. Bwanji osangolola kuti ena akulakwireni? Bwanji osangolola kuti ena akubereni?
Actually, it is already a defeat for you, that you have lawsuits among yourselves. Why not rather be wronged? Why not rather be cheated?
8 Mʼmalo mwake, inuyo ndiye mumabera ena ndi kuwalakwira, ndipo mumachita izi kwa abale anu.
No, but you yourselves do wrong, and cheat, and that against your brothers.
9 Kodi simukudziwa kuti munthu woyipa sadzalowa mu ufumu wa Mulungu? Musanyengedwe: achigololo, kapena opembedza mafano, kapena achiwerewere, kapena amuna adama, kapena ogonana ndi amuna okhaokha;
Or do you not know that the unrighteous will not inherit the Kingdom of God? Do not be deceived. Neither the sexually immoral, nor idolaters, nor adulterers, nor effeminate, nor men who have sexual relations with men,
10 kapena akuba, kapena aumbombo, kapena oledzera, kapena achipongwe, kapena opeza ndalama mwachinyengo sadzalowa mu ufumu wa Mulungu.
nor thieves, nor covetous, nor drunkards, nor slanderers, nor swindlers, will inherit the Kingdom of God.
11 Ndipo umu ndi mmene ena mwa inu munalili. Koma munatsukidwa, munayeretsedwa, munalungamitsidwa mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu ndi Mzimu wa Mulungu wathu.
Such were some of you, but you were washed. But you were sanctified. But you were justified in the name of the Lord Jesus (the) Messiah, and in the Spirit of our God.
12 Inu mumati, “Ine ndili ndi ufulu wochita chilichonse.” Komatu si zonse zimene nʼzothandiza. “Ndili ndi ufulu wochita chilichonse.” Koma sindidzagonjetsedwa ndi chilichonse.
"All things are lawful for me," but not all things are expedient. "All things are lawful for me," but I will not be brought under the power of anything.
13 Inu mumati, “Chakudya, kwake nʼkulowa mʼmimba ndipo mimba ntchito yake nʼkulandira chakudyacho.” Koma Mulungu adzawononga zonsezi. Thupi silochitira chigololo, koma la Ambuye, ndipo Ambuye ndiye mwini thupilo.
"Foods for the belly, and the belly for foods," but God will bring to nothing both it and them. But the body is not for sexual immorality, but for the Lord; and the Lord for the body.
14 Mwamphamvu zake Mulungu anaukitsa Ambuye kwa akufa, ndipo ifenso adzatiukitsa.
Now God raised up the Lord, and will also raise us up by his power.
15 Kodi simukudziwa kuti matupi anuwo ndi ziwalo za Khristu mwini? Kodi tsono ndingatenge ziwalo za Khristu nʼkuzisandutsa ziwalo za mkazi wadama? Zosatheka!
Do you not know that your bodies are members of Messiah? Should I then take the members of Messiah, and make them members of a prostitute? Absolutely not.
16 Kodi simukudziwa kuti amene amadzipereka kwa mkazi wadama, iyeyo ndi mkaziyo amasanduka thupi limodzi? Paja kunalembedwa kuti, “Awiriwo adzakhala thupi limodzi.”
Or do you not know that he who is joined to a prostitute is one body? For he says, "The two will become one flesh."
17 Koma amene amadzipereka kwa Ambuye, iyeyo ndi Ambuye amakhala mzimu umodzi.
But he who is joined to the Lord is one spirit.
18 Thawani dama. Machimo onse amene munthu amachita amakhala kunja kwa thupi lake, koma amene amachita machimo okhudza chigololo, amachimwira thupi lake lomwe.
Flee sexual immorality. "Every sin that a person does is outside the body," but he who commits sexual immorality sins against his own body.
19 Kodi simukudziwa kuti thupi lanu ndi Nyumba ya Mzimu Woyera, amene ali mwa inu, amene mwalandira kuchokera kwa Mulungu? Inu simuli panokha ayi.
Or do you not know that your body is a temple of the Holy Spirit which is in you, which you have from God? You are not your own,
20 Ndinu ochita kugulidwa. Nʼchifukwa chake lemekezani Mulungu mʼthupi lanu.
for you were bought with a price. Therefore glorify God in your body.