< 1 Akorinto 6 >

1 Pamene wina wa inu ali ndi mlandu ndi mnzake, nʼchifukwa chiyani amatengera nkhaniyo kwa anthu akunja kuti akawaweruze mʼmalo mopita nayo kwa oyera mtima?
Smutné je i to, že mezi sebou vedete spory před světskými soudy. Není vám hanba?
2 Kodi inu simukudziwa kuti anthu a Mulungu adzaweruza dziko lapansi? Ndipo ngati inu mungaweruze dziko lapansi, kodi sindinu oyenera kuweruza milandu ingʼonoyingʼono?
Cožpak křesťané, kterým jednou bude svěřen soud nad celým světem, nejsou schopni dohodnout se sami mezi sebou?
3 Kodi simukudziwa kuti mudzaweruza angelo? Nanga bwanji zinthu za mʼmoyo uno!
Nevíte, že jednou máte soudit i anděly?
4 Nʼchifukwa chake, ngati pali milandu pa zinthu zotere, sankhani anthu ena kuti akhale oweruza ngakhale alibe udindo mu mpingo.
Co jsou proti tomu nějaké obchodní záležitosti? Styďte se, že vám tohle musím vytýkat.
5 Ndikunena izi kuti ndikuchititseni manyazi. Moti nʼkutheka kuti pakati panu palibe wina wanzeru zokwanira kuti aziweruza mlandu pakati pa Akhristu?
To se mezi vámi nenajde ani jeden, kdo by vás rozsoudil? Není v takovém případě lepší nést křivdu než žalovat na svého bratra u nekřesťanů? Určitě tím uděláte svému Pánu větší čest.
6 Koma mʼmalo mwake mʼbale atengera ku bwalo la mlandu mʼbale mnzake kukaweruzidwa. Zonsezi pamaso pa akunja!
7 Chokha choti mwakasumirana chikuonetseratu kuti mwagonjetsedwa kale. Bwanji osangolola kuti ena akulakwireni? Bwanji osangolola kuti ena akubereni?
8 Mʼmalo mwake, inuyo ndiye mumabera ena ndi kuwalakwira, ndipo mumachita izi kwa abale anu.
9 Kodi simukudziwa kuti munthu woyipa sadzalowa mu ufumu wa Mulungu? Musanyengedwe: achigololo, kapena opembedza mafano, kapena achiwerewere, kapena amuna adama, kapena ogonana ndi amuna okhaokha;
Myslíte, že do Božího království se dostane někdo hříšný? Neklamte sami sebe. Žádný chamtivec a požitkář, ani cizoložník nebo homosexuál,
10 kapena akuba, kapena aumbombo, kapena oledzera, kapena achipongwe, kapena opeza ndalama mwachinyengo sadzalowa mu ufumu wa Mulungu.
ani zloděj, opilec a hrubián do Božího království nevkročí!
11 Ndipo umu ndi mmene ena mwa inu munalili. Koma munatsukidwa, munayeretsedwa, munalungamitsidwa mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu ndi Mzimu wa Mulungu wathu.
I vy jste takoví bývali ale byli jste očištěni, prohlášeni za bezúhonné a odděleni pro Boha prostřednictvím jeho Ducha, a to zásluhou Ježíše Krista.
12 Inu mumati, “Ine ndili ndi ufulu wochita chilichonse.” Komatu si zonse zimene nʼzothandiza. “Ndili ndi ufulu wochita chilichonse.” Koma sindidzagonjetsedwa ndi chilichonse.
Křesťanství – to není žádný seznam „smíš – nesmíš“. Nic nám není zakázáno, ne všechno nám však prospívá. Ke všemu smíme přistupovat svobodně – ale ne tak, aby nás to nakonec ovládlo.
13 Inu mumati, “Chakudya, kwake nʼkulowa mʼmimba ndipo mimba ntchito yake nʼkulandira chakudyacho.” Koma Mulungu adzawononga zonsezi. Thupi silochitira chigololo, koma la Ambuye, ndipo Ambuye ndiye mwini thupilo.
Bůh nám dal chuť k jídlu a žaludek pro přijímání potravy; ovšem ani jedno ani druhé tu nebude věčně. Smilstvo je však problém daleko vážnější. Tělo nám nebylo dáno k tomu, abychom ho zneužívali, ale aby sloužilo Kristu.
14 Mwamphamvu zake Mulungu anaukitsa Ambuye kwa akufa, ndipo ifenso adzatiukitsa.
A stejnou mocí, jakou vzkřísil Bůh Krista, vzkřísí také nás.
15 Kodi simukudziwa kuti matupi anuwo ndi ziwalo za Khristu mwini? Kodi tsono ndingatenge ziwalo za Khristu nʼkuzisandutsa ziwalo za mkazi wadama? Zosatheka!
Naše těla jsou vlastně buňkami těla Kristova.
16 Kodi simukudziwa kuti amene amadzipereka kwa mkazi wadama, iyeyo ndi mkaziyo amasanduka thupi limodzi? Paja kunalembedwa kuti, “Awiriwo adzakhala thupi limodzi.”
Jak bychom mohli něco takového spojovat s prodejnou ženou? Mojžíš říká, že „dva se stanou jedním tělem“. Je myslitelné a lze si vůbec představit jedno tělo ze dvou tak rozdílných „materiálů“?
17 Koma amene amadzipereka kwa Ambuye, iyeyo ndi Ambuye amakhala mzimu umodzi.
My přece máme usilovat o jinou jednotu – o jednotu s Kristem!
18 Thawani dama. Machimo onse amene munthu amachita amakhala kunja kwa thupi lake, koma amene amachita machimo okhudza chigololo, amachimwira thupi lake lomwe.
Proto se varujte smilstva. Ostatní přestupky se těla přímo nedotýkají, ale smilstvem se proviňujete na svém vlastním těle.
19 Kodi simukudziwa kuti thupi lanu ndi Nyumba ya Mzimu Woyera, amene ali mwa inu, amene mwalandira kuchokera kwa Mulungu? Inu simuli panokha ayi.
Mějte na paměti, že vaše tělo je chrámem svatého Ducha, který v něm bydlí a kterého vám dal Bůh.
20 Ndinu ochita kugulidwa. Nʼchifukwa chake lemekezani Mulungu mʼthupi lanu.
Nepatříte už sami sobě, byli jste koupeni – a velmi draze koupeni. Ať tedy i vaše tělo dělá Bohu čest!

< 1 Akorinto 6 >