< 1 Akorinto 4 >

1 Choncho tsono anthu atione ife monga atumiki a Khristu, ndiponso ngati osunga zinsinsi za Mulungu.
Eshe ash jámo noon Krstos guutswotsi nowottsok'o Ik'oke aashtso kitso adaro boosh imetswotsk'o woshde noon taawwe.
2 Chofunika kwambiri nʼchakuti amene apatsidwa udindo oyangʼanira aonetse kukhulupirika.
Adar dek'tswotswere amanetswotsi wotar daatsewo boosh geyife.
3 Ine ndilibe nazo kanthu ngati ndiweruzidwa ndi inu kapena khothi lina lililonse. Ndithu, inenso sindidziweruza ndekha.
T jangosh b́wotitka wotiyal itwoor tiyats itangshiyal wee k'osh asho tiyats b́angshiyal eegonor kic'eratse, arikon taawor dab ttookats angsho falatse.
4 Chikumbumtima changa sichikunditsutsa, koma sikuti ndine wolungama. Wondiweruza ine ndi Ambuye.
Taa tdantsok'oyi wotiyal tnibo taan gac'eratse, hanuwere taa s'ayin twottsok'owo kitsratse, ernmó tiyats angshituwo doonzo s'uziye.
5 Chomwecho musaweruze nthawi yoweruza isanakwane. Dikirani mpaka Ambuye atabwera. Iye adzaonetsa poyera zimene zabisika mu mdima ndipo adzaonetsa maganizo a mʼmitima ya anthu. Pa nthawi imeneyo aliyense adzalandira kwa Mulungu chiyamiko.
Mansh bíaawo b́ borawo, doonzo angshosh b́waftsere shino konatsor angshk'ayere, bí b́woor t'aluwotse ááshtso mist'iriyo shanomaants kishituwe, ashuwots nibotse ááshts hasabiyo kishituwe, manoor ik ikon Ik'oke bísh wotit údono daatsituwe.
6 Tsono abale, ndapereka chitsanzo cha ine mwini ndi Apolo kuti mupindule. Phunzirani kwa ife tanthauzo la mawu akuti, “Musamapitirire zimene Malemba akunena,” kuti musamanyade pamene wina aposa mnzake.
Eshuwwotso! iti t'ak'amosha etaat keewanats taanat Ap'losi aridek'at tkeewi, hanowere tk'al «Guut'etsatse beshk'aye» etiru izi biitso no atse it danetuwok'wa etaatniye, mansh ash ikon it'o k'oshonowere gac'o geyiratse itsha.
7 Pakuti ndani amakusiyanitsani ndi wina aliyense? Nʼchiyani muli nacho chimene simunalandire? Ndipo ngati munalandira, bwanji mumadzitukumula ngati kuti simunalandire?
Nee k'oshuwotsiyere eegneya nbogi? K'oshoke nde'aw keewo eebi fa'oni? Eshe jam keewo k'oshoke ndek'ka wotiyal de'aw ashok'o eegoshe n it'iri?
8 Inu muli nazo kale zonse zimene mufuna! Inu mwalemera kale! Inu mwayamba kale kulamulira ife! Ndilakalaka mukanakhaladi mafumu kuti ife tikhale nawo mafumu pamodzi ndi inu.
Andere itsh geyiru keew jamo daatsrte, andere galetswotsi wotertee, no atse k'aleyat naashwtserte, arikon it naashka wotink'ere, noowere itnton toowar nonaashitwotse it naashonuwere sheenge b́wotiyank'oni,
9 Pakuti kwa ine zikuoneka ngati kuti Mulungu watiyika ife atumwi pachionetsero, kumapeto kwa mndandanda, monga anthu oweruzidwa kuti akaphedwe mʼmabwalo. Ife tayikidwa kuti tionekere ku dziko lonse, kwa angelo ndi anthu.
Ik'o noon b́woshtswotsi k'iro boatsats angshr bo úd'etuwoki beewok de'amet ashuwotsitse shutstsuwotsi noon b́wooshtsok'o arefee, manatse tuutso dats jamatse melakiwotsnat ashuwots shinatse miis'i mit wotatniye nobe'eyiri,
10 Ife ndife opusa chifukwa cha Khristu, koma inu ndinu anzeru mwa Khristu! Ife ndife ofowoka koma inu ndinu amphamvu! Inu ndinu olemekezeka koma ife ndife opeputsidwa!
Noo Krstos jangosha etaat dogwotsi woterone, itmó Krstosn ayidek'at dantsuwotsi wotwutserte, mank'owere noo mawtswotsi woterone, itmó kup'uwotsi woterte, it mangiyeyirwotsi woterte, noomó keteyeyiruwotsi woterone.
11 Mpaka pano tili ndi njala ndi ludzu, tili ndi sanza, tikuzunzidwa, tilibe nyumba.
And b́ wotiyaloru and sa'atansh b́ borfetso nok'ak'iri, no shashúwiri, no aratsiri, no jot'eyiri beyoko t'út'at hake bako nojawriri.
12 Timagwira ntchito molimbika ndi manja athu. Akamatitemberera, ife timadalitsa; tikasautsidwa, ife timapirira.
No kishon finat ango nomaawiri, noon bo c'ashor noderiri, noon bo gishor no k'amiri,
13 Pamene atilalatira timayankha mwachifundo. Mpaka pano takhala ngati zinyalala za dziko, monga zakudzala za dziko lapansi.
noon boc'ashonat noshútso bot'afiyor maac' nefon boosh no aaniri, andish b́ borfetso datsanatse juwetsok'onat datsatse fokets kímo woterone.
14 Sindikulemba izi kuti ndikuchititseni manyazi, koma kukuchenjezani monga ana anga okondedwa.
Taa han itsh tguut'ir shuneets tnana'úwotsk'o woshdek'at izosh gawatni bako iti jiitsiyo geyatniyaliyee.
15 Ngakhale muli ndi anthu 10,000 okutsogolerani mwa Khristu, mulibe abambo ambiri, popeza mwa Khristu Yesu, ine ndakhala abambo anu kudzera mu Uthenga Wabwino.
Krstosn jishiru ayuwotsi it detsalor nih ayuwotsi deshatste, taayere itn Iyesus Krstos doo shishiyon shuure.
16 Chifukwa chake ndikukupemphani kuti munditsanze ine.
Mansh tjafro sha'ar taan it arituwok'o iti k'oniruwe.
17 Chifukwa cha ichi ndikutumiza kwa inu Timoteyo, mwana wanga amene ndimamukonda, amene ndi wokhulupirika mwa Ambuye. Adzakukumbutsani inuyo za moyo wanga mwa Khristu Yesu, umene ukugwirizana ndi zimene ndimaphunzitsa paliponse mu mpingo uliwonse.
Hanatse tuutson shuneetsonat amanets doonzon t naayi wottso T'imotiyosi itsh woshere, b́ be beyokenowere Ik'i maa mooke t daniyirwok'o bí taa Krstosn t daatsts handr beyon bín it jishetuwo itsh gawituwe.
18 Ena mwa inu mukudzitukumula, ngati kuti sindingabwere kwanu.
Ernmó ititse ik ikuwots taa itn s'iilo twarawok'o boosh bí arere kofangon s'eenwtserne.
19 Koma ndibwera kwanuko posachedwapa, ngati Ambuye alola, ndipo ndi pamene ndidzadziwe osati zimene anthu odzitukumulawa akuyankhula, koma kuti mphamvu zawo nʼzotani.
Ernmó doonzon tooh karn aawotse itok weetuwe, manoor kofangirwanots bo noon keew s'uzi b́woterawo bokúp' kúp'onor dano geefe.
20 Pakuti ufumu wa Mulungu si mawu chabe koma mphamvu.
Ik'i mengsto noon keewi kis' b́ woterawo Ik'i kúp'e.
21 Kodi musankha chiyani? Kodi ndidzabwere ndi chikwapu, kapena mu chikondi ndiponso mwa mzimu wofatsa?
It geyirwo eebi? Sezi gumbo de'er it maants twoo geeftee? Himo shunonat tooko dashan detsi shayiron twoone it geyi?

< 1 Akorinto 4 >