< 1 Akorinto 3 >
1 Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
And I, brethren, could not speak to you as to spiritual, but as to carnal, even as to babes in Christ.
2 Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
I have fed you with milk, and not with meat: for until now ye were not able to bear it, neither yet now are ye able.
3 Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
For ye are yet carnal: for though there is among you envying, and strife, and divisions, are ye not carnal, and walk as men?
4 Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
For while one saith, I am of Paul; and another, I am of Apollos; are ye not carnal?
5 Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
Who then is Paul, and who is Apollos, but ministers by whom ye believed, even as the Lord gave to every man?
6 Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
I have planted, Apollos watered; but God hath given the increase.
7 Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
So then neither is he that planteth any thing, neither he that watereth; but God that giveth the increase.
8 Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
Now he that planteth and he that watereth are one: and every man shall receive his own reward according to his own labour.
9 Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
For we are labourers together with God: ye are God’s field, ye are God’s building.
10 Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
According to the grace of God which is given to me, as a wise masterbuilder, I have laid the foundation, and another buildeth upon it. But let every man take heed how he buildeth upon it.
11 Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
For other foundation can no man lay than that which is laid, which is Jesus Christ.
12 Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
Now if any man buildeth upon this foundation gold, silver, precious stones, wood, hay, stubble;
13 ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
Every man’s work shall be made manifest: for the day shall declare it, because it shall be revealed by fire; and the fire shall try every man’s work of what sort it is.
14 Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
If any man’s work abideth which he hath built upon it, he shall receive a reward.
15 Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
If any man’s work shall be burned, he shall suffer loss: but he himself shall be saved; yet so as by fire.
16 Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
Know ye not that ye are the temple of God, and that the Spirit of God dwelleth in you?
17 Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
If any man defileth the temple of God, him shall God destroy; for the temple of God is holy, which temple ye are.
18 Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn )
Let no man deceive himself. If any man among you seemeth to be wise in this world, let him become a fool, that he may be wise. (aiōn )
19 Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
For the wisdom of this world is foolishness with God. For it is written, He taketh the wise in their own craftiness.
20 ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
And again, The Lord knoweth the thoughts of the wise, that they are vain.
21 Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
Therefore let no man glory in men. For all things are yours;
22 kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
Whether Paul, or Apollos, or Cephas, or the world, or life, or death, or things present, or things to come; all are yours;
23 ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.
And ye are Christ’s; and Christ is God’s.