< 1 Akorinto 3 >

1 Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
And I, brethren, was not able to speak unto you as unto spiritual, but as unto carnal, even babes in Christ.
2 Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
I have fed you with milk, not with meat; for you were not yet able. But ye are not now yet able:
3 Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
for ye are yet carnal. For where there are envy and strife among you, are you not carnal, and walking about according to man?
4 Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
For when one may say, I am indeed of Paul; another, I am of Apollos; are you not men?
5 Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
Then what is Apollos? and what is Paul? But ministers through whom ye believed; even as the Lord gave to each one.
6 Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
I planted, Apollos watered; but God gave the increase.
7 Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
So neither is the one planting, nor the one watering anything, but God the one giving the increase.
8 Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
But he that planteth and he that watereth are one: and each one shall receive his own reward according to his own labor.
9 Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
For we are God's fellow-laborers; ye are God's farm; ye are God's building.
10 Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
According to the grace of God which was given unto me, I as a wise architect, laid the foundation; and another builds on it. Let each one take heed how he builds.
11 Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
For other foundation no one is able to lay beside the one which is laid, who is Jesus Christ.
12 Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
But if any one builds upon the foundation, gold, silver, precious stones, wood, hay, stubble;
13 ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
the work of each will be made manifest: for the day will reveal it, because it is revealed by fire; and the same fire will try the work of each what soil it is.
14 Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
And if the work of any one which he builds, abides, he will receive a reward:
15 Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
But if the work of any one shall be burnt up, he shall suffer loss; but himself shall be saved, but as through the fire.
16 Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
Do you not know that you are the temple of God, and the Spirit of God dwells in you?
17 Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
If any one destroys the temple of God, him will God destroy; for the temple of God is holy, which ye are.
18 Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
Let no one deceive himself. If any one seems to be wise among you in this age, let him become a fool, that he may be wise. (aiōn g165)
19 Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
For the wisdom of this world is foolishness with God. For it has been written. He taketh the wise in their own craftiness.
20 ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
And again, The Lord knows the thoughts of the wise, that they are vain.
21 Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
So let no one boast among men; for all things are yours;
22 kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
whether Paul, or Apollos, or Cephas, or the world, or life, or death, or things present, or things to come.
23 ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.
All things are yours; and ye are Christ's; and Christ is God's.

< 1 Akorinto 3 >