< 1 Akorinto 16 >

1 Tsopano za zopereka zothandiza anthu a Ambuye a ku Yerusalemu. Muchite zomwe ndinawuza mipingo ya ku Galatiya kuti ichite.
Maintenant, en ce qui concerne la collecte pour les saints: comme j'ai ordonné aux assemblées de Galatie, faites de même.
2 Pa tsiku loyamba la sabata lililonse, aliyense wa inu azipatula ndalama molingana ndi zomwe wapezera. Asunge, kuti ndikabwera pasadzakhalenso msonkhamsonkha.
Le premier jour de chaque semaine, que chacun de vous fasse l'épargne qui lui convient, afin qu'il n'y ait pas de collecte à mon arrivée.
3 Pamenepo, ndikadzafika, ndidzawapatsa makalata a umboni anthu amene mudzawasankhe ndi kuwatuma kuti akapereka mphatso zanu ku Yerusalemu.
À mon arrivée, j'enverrai celui que vous approuverez avec des lettres pour porter à Jérusalem le don que vous m'avez fait.
4 Ngati kutaoneka kuti nʼkoyenera kuti ndipite nawo, adzapita nane limodzi.
S'il convient que j'y aille aussi, ils iront avec moi.
5 Ndidzafika kwanuko nditadutsa ku Makedoniya pakuti ndikuyembekezera kudzera ku Makedoniyako.
Je viendrai chez vous quand j'aurai traversé la Macédoine, car je passe par la Macédoine.
6 Mwina ndidzakhala nanu kanthawi kochepa kapenanso nyengo yonse yozizira, kuti mudzandithandize kupitiriza ulendo wanga kulikonse kumene ndingapite.
Mais il se peut que je reste chez vous, ou même que j'hiverne chez vous, afin que vous m'envoyiez en voyage, où que j'aille.
7 Sindikufuna kuti ndikuoneni tsopano mongodutsa chabe, koma ndikuyembekezera kudzakhala nanu kwa kanthawi, ngati Ambuye alola.
Car je ne veux pas vous voir maintenant en passant, mais j'espère rester quelque temps avec vous, si le Seigneur le permet.
8 Koma ndikhala ndili ku Efeso mpaka nthawi ya Pentekosite,
Mais je resterai à Éphèse jusqu'à la Pentecôte,
9 pakuti mwayi waukulu wapezeka woti nʼkugwira ntchito yaphindu, koma pali ambiri amene akutsutsana nane.
car une porte grande et efficace s'est ouverte à moi, et les adversaires sont nombreux.
10 Ngati Timoteyo afike kwanuko, onetsetsani kuti pasakhale zina zomuchititsa mantha pamene ali pakati panu, pakuti iye akugwira ntchito ya Ambuye monga ine.
Or, si Timothée vient, veillez à ce qu'il soit avec vous sans crainte, car il fait l'œuvre du Seigneur, comme moi aussi.
11 Wina aliyense asamunyoze. Muthandizeni kupitiriza ulendo wake mwamtendere kubwereranso kuli ine. Ndikumuyembekeza pamodzi ndi abale ena.
Que personne ne le méprise donc. Mais faites-le avancer en paix dans son voyage, afin qu'il vienne vers moi; car je l'attends avec les frères.
12 Tsono kunena za mʼbale wathu, Apolo, ndinamuwumiriza kwambiri kuti abwere kwa inu abale, ndipo iye sanafune kupita tsopano. Koma akadzapeza mpata wabwino adzabwera.
Pour ce qui est du frère Apollos, je l'ai fortement incité à venir chez vous avec les frères, mais il n'a pas du tout voulu venir maintenant; mais il viendra quand il en aura l'occasion.
13 Khalani tcheru; khazikikani mʼchikhulupiriro chanu; limbani mtima; khalani amphamvu.
Regardez! Restez fermes dans la foi! Soyez courageux! Soyez forts!
14 Chitani zonse mwachikondi.
Que tout ce que vous faites soit fait dans l'amour.
15 Mukudziwa kuti a mʼbanja la Stefano ndiye anali oyamba kutembenuka mtima ku Akaya, ndipo akhala akudzipereka kutumikira oyera mtima. Choncho ndikukudandaulirani, inu abale,
Or, je vous prie, frères - vous connaissez la maison de Stéphanas, qui est la première de l'Achaïe, et qui s'est mise au service des saints -
16 kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka.
de leur être également soumis, ainsi qu'à tous ceux qui participent à l'œuvre et travaillent.
17 Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane.
Je me réjouis de la venue de Stéphanas, de Fortunatus et d'Achaicus, car ils ont comblé ce qui vous manquait.
18 Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu womwe. Anthu a mtundu oterewa ngofunika kuwalemekeza.
Car ils ont rafraîchi mon esprit et le vôtre. Reconnaissez donc ceux qui agissent ainsi.
19 Mpingo wa mʼchigawo cha ku Asiya ukupereka moni. Akula ndi Prisila akuperekanso moni wachisangalalo, mwa Ambuye, ndiponso mpingo umene umakumana mʼnyumba mwawo ukupereka moni.
Les assemblées d'Asie vous saluent. Aquila et Priscille vous saluent chaleureusement dans le Seigneur, ainsi que l'assemblée qui est dans leur maison.
20 Abale onse kuno akupereka moni wawo. Patsanani moni wachikondi chenicheni.
Tous les frères vous saluent. Saluez-vous les uns les autres par un saint baiser.
21 Ineyo Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa mawu awa akuti moni.
Cette salutation est de moi, Paul, de ma propre main.
22 Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!
Si quelqu'un n'aime pas le Seigneur Jésus-Christ, qu'il soit maudit. Viens, Seigneur!
23 Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi inu.
Que la grâce du Seigneur Jésus-Christ soit avec vous!
24 Chikondi changa chikhale ndi nonsenu mwa Khristu Yesu.
Je vous salue tous en Jésus-Christ. Amen.

< 1 Akorinto 16 >