< 1 Akorinto 14 >

1 Funafunani chikondi, ndikufunitsitsa mphatso zauzimu, makamaka mphatso ya uneneri.
Držite se ljubavi, a starajte se za duhovne dare, a osobito da prorokujete.
2 Pakuti aliyense amene amayankhula malilime sayankhula kwa anthu, koma kwa Mulungu. Zoonadi, palibe amene amamva zimene akunena chifukwa Mzimu ndiye amamuyankhulitsa zachinsinsi.
Jer koji govori jezike, ne govori ljudima nego Bogu: jer niko ne sluša, a on duhom govori tajne.
3 Koma amene amanenera amayankhula kwa anthu kuti awapatse mphamvu, awalimbikitse ndi kuwakhazikitsa mtima pansi.
A koji prorokuje govori ljudima za popravljanje i utjehu i utvrðenje.
4 Iye amene amayankhula malilime amadzilimbikitsa yekha, koma amene amanenera amalimbikitsa mpingo.
Jer koji govori jezike sebe popravlja, a koji prorokuje crkvu popravlja.
5 Nʼkanakonda kuti aliyense mwa inu atamayankhula malilime, koma ndi bwino kuti muzinenera. Amene amanenera amaposa amene amayankhula malilime, pokhapokha atatanthauzira kuti mpingo upindule.
Ali ja bih htio da vi svi govorite jezike, a još više da prorokujete: jer je veæi onaj koji prorokuje negoli koji govori jezike, veæ ako ko kazuje, da se crkva popravlja.
6 Tsono, abale, mudzapindula chiyani nditabwera kwa inu ndi kukuyankhulani mʼmalilime? Koma mudzapindula ngati nditakubweretserani vumbulutso lina lake, kapena chidziwitso, kapena chiphunzitso.
A sad, braæo, ako doðem k vama jezike govoreæi, kaku æu korist uèiniti ako vam ne govorim ili u otkrivenju, ili u razumu, ili u proroštvu, ili u nauci?
7 Ngakhale mu zinthu zopanda moyo monga chitoliro kapena gitala, zimene zimatulutsa liwu; kodi munthu akhoza kudziwa bwanji nyimbo imene ikuyimbidwa ngati mawu sakumveka mogwirizana bwino?
Kao neke stvari bezdušne koje daju glas, bila svirala ili gusle, ako razlièna glasa ne daju, kako æe se razumjeti šta se svira ili gudi?
8 Komanso ngati lipenga silimveka bwino, ndani angakonzekere nkhondo?
Jer ako truba da nerazgovijetan glas, ko æe se pripraviti na boj?
9 Chimodzimodzinso inu. Ngati simungayankhule mawu omveka bwino mʼchiyankhulo chanu, wina angadziwe bwanji chimene mukunena? Muzingodziyankhulira nokha.
Tako i vi ako nerazumljivu rijeè reèete jezikom, kako æe se razumjeti šta govorite? Jer æete govoriti u vjetar.
10 Mosakayika, pali ziyankhulo zosiyanasiyana pa dziko lapansi, koma palibe nʼchimodzi chomwe chimene chilibe tanthauzo.
Ima na svijetu Bog zna koliko razliènijeh glasova, ali nijedan nije bez znaèenja.
11 Tsono ngati sindingatolepo tanthauzo la zimene wina akuyankhula, ndiye kuti ndine mlendo kwa oyankhulayo ndipo iyeyo ndi mlendo kwa ine.
Ako dakle ne znam sile glasa, biæu nijemac onome kome govorim, i onaj koji govori biæe meni nijemac.
12 Chimodzimodzinso inu. Popeza mumafunitsitsa mphatso za Mzimu, yesetseni kuchita bwino pa mphatso zimene zimamanga mpingo.
Tako i vi, buduæi da se starate za duhovne darove, gledajte da budete onima bogati koji su na popravljanje crkve.
13 Pa chifukwa ichi munthu amene amayankhula malilime apemphere kuti azitha kutanthauzira zimene akunena.
Zato koji govori jezikom neka se moli Bogu da kazuje.
14 Popeza ngati ndipemphera mʼmalilime, ndi mzimu wanga umene ukupemphera, koma nzeru zanga sizikupindula kanthu.
Jer ako se jezikom molim Bogu, moj se duh moli, a um je moj bez ploda.
15 Tsono pamenepa nʼkutani? Ndidzapemphera ndi mzimu wanga, komanso ndidzapemphera ndi nzeru zanga. Ndidzayimba ndi mzimu wanga, komanso ndidzayimba ndi nzeru zanga.
Šta æe se dakle èiniti? Moliæu se Bogu duhom, a moliæu se i umom; hvaliæu Boga duhom, a hvaliæu i umom.
16 Ngati mutamanda Mulungu mu mzimu, kodi munthu amene wapezeka pakati pa amene akuyankhula zomwe sakumva, adzavomereza bwanji kuti “Ameni” pa pemphero lanu loyamikalo popeza sakumva chimene mukunena?
Jer kad blagosloviš duhom kako æe onaj koji stoji mjesto prostaka reæi amin po tvome blagoslovu, kad ne zna šta govoriš?
17 Mukhoza kumathokoza mokwanira, koma munthu winayo sanathandizikepo.
Ti dobro zahvaljuješ, ali se drugi ne popravlja.
18 Ndikuyamika Mulungu chifukwa ndimayankhula malilime kuposa nonsenu.
Hvala Bogu mojemu što govorim jezike veæma od sviju vas.
19 Koma mu mpingo ndi kwabwino kuti ndiyankhule mawu asanu okha omveka bwino kuti ndilangize bwino ena kusiyana ndikuyankhula mawu ambirimbiri mʼmalilime.
Ali u crkvi volim pet rijeèi umom svojijem reæi, da se i drugi pomognu, negoli hiljadu rijeèi jezikom.
20 Abale, lekani kuganiza ngati ana. Mukhale ana pa nkhani ya zoyipa koma mʼmaganizo anu mukhale okhwima.
Braæo! ne budite djeca umom, nego pakošæu djetinjite, a umom budite savršeni.
21 Zinalembedwa mʼMalamulo kuti, “Ndidzayankhula kwa anthu awa, kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo ndiponso ndi milomo yachilendo. Koma ngakhale nthawi imeneyo sadzandimvera Ine, akutero Ambuye.”
U zakonu piše: drugijem jezicima i drugijem usnama govoriæu narodu ovome, i ni tako me neæe poslušati, govori Gospod.
22 Kotero, malilime ndi chizindikiro, osati cha kwa okhulupirira koma kwa osakhulupirira. Koma kunenera ndi chizindikiro kwa okhulupirira osati kwa osakhulupirira.
Zato su jezici za znak ne onima koji vjeruju, nego koji ne vjeruju; a proroštvo ne onima koji ne vjeruju, nego koji vjeruju.
23 Kotero kuti ngati mpingo wonse utasonkhana pamodzi ndipo aliyense namayankhula malilime, ndipo wina amene sangazindikire kapena ena osakhulupirira nabwerapo, kodi sadzanena kuti mwachita misala?
Ako se dakle skupi crkva sva na jedno mjesto, i svi uzgovorite jezicima, a doðu i prostaci, ili nevjernici, neæe li reæi da ste poludjeli?
24 Koma ngati wosakhulupirira kapena wina amene sakuzindikira abwera pamene aliyense akunenera, adzatsutsika mu mtima ndi zonse zimene akumva ndipo adzaweruzidwa ndi onse
A ako svi prorokuju, i doðe kakav nevjernik ili prostak, bude pokaran od sviju i suðen od sviju.
25 ndipo zinsinsi za mu mtima mwake zidzawululika. Kotero kuti adzadzigwetsa pansi ndi kupembedza Mulungu akufuwula kuti, “Mulungu ali pakati panudi!”
I tako tajne srca njegova bivaju javljene, i tako padnuvši nièice pokloniæe se Bogu, i kazaæe da je zaista Bog s vama.
26 Kodi tsono abale, tinene chiyani? Pamene musonkhana pamodzi, aliyense amakhala ali ndi nyimbo yoti ayimbe, kapena mawu oti alangize, vumbulutso, malilime, kapena kumasulira kwake. Zonsezi cholinga chake chikhale kulimbikitsa mpingo.
Šta æe se dakle èiniti, braæo? Kad se sabirate svaki od vas ima psalam, ima nauku, ima jezik, ima otkrivenje, ima kazivanje; a sve da biva na popravljanje.
27 Ngati wina ayankhula malilime, awiri kapena akachulukapo atatu ndiye ayankhule mmodzimmodzi, ndipo wina ayenera kutanthauzira zimene ayankhulazo.
Ako govori ko jezikom, ili po dvojica, ili najviše po trojica, i to poredom; a jedan da kazuje.
28 Ngati palibe wotanthauzira, woyankhulayo akhale chete mu mpingo ndipo adziyankhulire iye mwini ndi Mulungu.
Ako li ne bude nikoga da kazuje, neka æuti u crkvi, a sebi neka govori i Bogu.
29 Aneneri awiri kapena atatu anenere, ndipo enawo asanthule mosamalitsa zimene anenerazo.
A proroci dva ili tri neka govore, i drugi neka rasuðuju.
30 Ndipo ngati vumbulutso labwera kwa munthu amene wakhala pansi, amene akuyankhulayo akhale chete.
Ako li se otkrije što drugome koji sjedi, neka èeka dok prvi uæuti.
31 Pakuti nonse mukhoza kunenera mmodzimmodzi motsatana kuti aliyense alangizidwe ndi kulimbikitsidwa.
Jer možete prorokovati svi, jedan po jedan, da se svi uèe, i svi da se tješe.
32 Mizimu ya aneneri imamvera ulamuliro wa aneneri.
I duhovi proroèki pokoravaju se prorocima;
33 Pakuti Mulungu si Mulungu wachisokonezo koma wamtendere. Monga mwa mipingo yonse ya oyera mtima.
Jer Bog nije Bog bune, nego mira, kao po svima crkvama svetijeh.
34 Amayi akhale chete mʼmisonkhano ya mpingo. Iwo asaloledwe kuyankhula, koma azikhala omvera monga mmene lamulo linenera.
Žene vaše da æute u crkvama; jer se njima ne dopusti da govore, nego da slušaju, kao što i zakon govori.
35 Ngati ali ndi mafunso, akafunse amuna awo ku nyumba. Nʼchochititsa manyazi kuti mkazi ayankhule mu msonkhano wa mpingo.
Ako li hoæe èemu da se nauèe, kod kuæe muževe svoje neka pitaju; jer je ružno ženi da govori u crkvi.
36 Kodi kapena mawu a Mulungu anachokera kwa inu? Kapena anafika kwa inu nokha?
Eda li od vas rijeè Božija iziðe? ili samijem vama doðe?
37 Ngati wina aliyense akuganiza kuti ndi mneneri kapena kuti ali ndi mphatso za Mzimu, ayenera kudziwa kuti zimene ndikukulemberanizi ndi lamulo la Ambuye.
Ako ko misli da je prorok ili duhovan, neka razumije što vam pišem, jer su Gospodnje zapovijesti.
38 Ngati munthu savomereza zimenezi, iyeyonso sadzavomerezedwa.
Ako li ko ne razumije, neka ne razumije.
39 Nʼchifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse anthu kuyankhula malilime.
Zato, braæo moja, starajte se da prorokujete, i ne zabranjujte govoriti jezicima.
40 Koma chilichonse chichitike moyenera ndi mwadongosolo.
A sve neka biva pošteno i uredno.

< 1 Akorinto 14 >