< 1 Akorinto 14 >

1 Funafunani chikondi, ndikufunitsitsa mphatso zauzimu, makamaka mphatso ya uneneri.
Suivez l'amour et désirez ardemment les dons spirituels, mais surtout celui de prophétiser.
2 Pakuti aliyense amene amayankhula malilime sayankhula kwa anthu, koma kwa Mulungu. Zoonadi, palibe amene amamva zimene akunena chifukwa Mzimu ndiye amamuyankhulitsa zachinsinsi.
Car celui qui parle dans une autre langue ne parle pas aux hommes, mais à Dieu; car personne ne comprend, mais c'est par l'Esprit qu'il dit des mystères.
3 Koma amene amanenera amayankhula kwa anthu kuti awapatse mphamvu, awalimbikitse ndi kuwakhazikitsa mtima pansi.
Mais celui qui prophétise parle aux hommes pour les édifier, les exhorter et les consoler.
4 Iye amene amayankhula malilime amadzilimbikitsa yekha, koma amene amanenera amalimbikitsa mpingo.
Celui qui parle en langue étrangère s'édifie lui-même, mais celui qui prophétise édifie l'assemblée.
5 Nʼkanakonda kuti aliyense mwa inu atamayankhula malilime, koma ndi bwino kuti muzinenera. Amene amanenera amaposa amene amayankhula malilime, pokhapokha atatanthauzira kuti mpingo upindule.
Or, je désire que vous parliez tous en d'autres langues, mais plus encore que vous prophétisiez. Car celui qui prophétise est plus grand que celui qui parle en d'autres langues, à moins qu'il n'interprète, afin que l'assemblée soit édifiée.
6 Tsono, abale, mudzapindula chiyani nditabwera kwa inu ndi kukuyankhulani mʼmalilime? Koma mudzapindula ngati nditakubweretserani vumbulutso lina lake, kapena chidziwitso, kapena chiphunzitso.
Mais maintenant, frères, si je viens à vous en parlant d'autres langues, que vous servirai-je, si je ne vous parle pas par révélation, ou par connaissance, ou par prophétie, ou par enseignement?
7 Ngakhale mu zinthu zopanda moyo monga chitoliro kapena gitala, zimene zimatulutsa liwu; kodi munthu akhoza kudziwa bwanji nyimbo imene ikuyimbidwa ngati mawu sakumveka mogwirizana bwino?
Même les choses sans vie qui font du bruit, soit la flûte, soit la harpe, si elles ne donnaient pas une distinction dans les sons, comment saurait-on ce qui est flûté ou harpé?
8 Komanso ngati lipenga silimveka bwino, ndani angakonzekere nkhondo?
Car si la trompette émettait un son incertain, qui se préparerait à la guerre?
9 Chimodzimodzinso inu. Ngati simungayankhule mawu omveka bwino mʼchiyankhulo chanu, wina angadziwe bwanji chimene mukunena? Muzingodziyankhulira nokha.
De même vous, si vous ne prononciez pas par la langue des paroles faciles à comprendre, comment saurait-on ce qui est dit? Car vous parleriez en l'air.
10 Mosakayika, pali ziyankhulo zosiyanasiyana pa dziko lapansi, koma palibe nʼchimodzi chomwe chimene chilibe tanthauzo.
Il y a peut-être tant de langues différentes dans le monde, et aucune n'est dépourvue de sens.
11 Tsono ngati sindingatolepo tanthauzo la zimene wina akuyankhula, ndiye kuti ndine mlendo kwa oyankhulayo ndipo iyeyo ndi mlendo kwa ine.
Si donc je ne connais pas le sens de la langue, je serais pour celui qui parle un étranger, et celui qui parle serait pour moi un étranger.
12 Chimodzimodzinso inu. Popeza mumafunitsitsa mphatso za Mzimu, yesetseni kuchita bwino pa mphatso zimene zimamanga mpingo.
Ainsi vous aussi, puisque vous êtes zélés pour les dons spirituels, cherchez à abonder pour l'édification de l'assemblée.
13 Pa chifukwa ichi munthu amene amayankhula malilime apemphere kuti azitha kutanthauzira zimene akunena.
Que celui qui parle une autre langue prie donc pour qu'il puisse interpréter.
14 Popeza ngati ndipemphera mʼmalilime, ndi mzimu wanga umene ukupemphera, koma nzeru zanga sizikupindula kanthu.
Car si je prie dans une autre langue, mon esprit prie, mais mon intelligence est infructueuse.
15 Tsono pamenepa nʼkutani? Ndidzapemphera ndi mzimu wanga, komanso ndidzapemphera ndi nzeru zanga. Ndidzayimba ndi mzimu wanga, komanso ndidzayimba ndi nzeru zanga.
Que dois-je faire? Je prierai par l'esprit, et je prierai aussi par l'intelligence. Je chanterai avec l'esprit, et je chanterai aussi avec l'intelligence.
16 Ngati mutamanda Mulungu mu mzimu, kodi munthu amene wapezeka pakati pa amene akuyankhula zomwe sakumva, adzavomereza bwanji kuti “Ameni” pa pemphero lanu loyamikalo popeza sakumva chimene mukunena?
Sinon, si tu bénis par l'esprit, comment celui qui remplit la place des ignorants dira-t-il « Amen » à ton action de grâces, puisqu'il ne sait pas ce que tu dis?
17 Mukhoza kumathokoza mokwanira, koma munthu winayo sanathandizikepo.
Car toi, tu rends certainement bien grâce, mais l'autre n'est pas édifié.
18 Ndikuyamika Mulungu chifukwa ndimayankhula malilime kuposa nonsenu.
Je rends grâce à mon Dieu, je parle d'autres langues plus que vous tous.
19 Koma mu mpingo ndi kwabwino kuti ndiyankhule mawu asanu okha omveka bwino kuti ndilangize bwino ena kusiyana ndikuyankhula mawu ambirimbiri mʼmalilime.
Cependant, dans l'assemblée, j'aime mieux dire cinq mots avec mon intelligence, afin d'instruire aussi les autres, que dix mille mots dans une autre langue.
20 Abale, lekani kuganiza ngati ana. Mukhale ana pa nkhani ya zoyipa koma mʼmaganizo anu mukhale okhwima.
Frères, ne soyez pas des enfants dans vos pensées, et ne faites pas preuve de malice, mais soyez mûrs dans vos pensées.
21 Zinalembedwa mʼMalamulo kuti, “Ndidzayankhula kwa anthu awa, kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo ndiponso ndi milomo yachilendo. Koma ngakhale nthawi imeneyo sadzandimvera Ine, akutero Ambuye.”
Il est écrit dans la loi: « C'est par des hommes de langue étrangère et par des lèvres d'étrangers que je parlerai à ce peuple. Ils ne m'écouteront même pas de cette manière, dit le Seigneur. »
22 Kotero, malilime ndi chizindikiro, osati cha kwa okhulupirira koma kwa osakhulupirira. Koma kunenera ndi chizindikiro kwa okhulupirira osati kwa osakhulupirira.
C'est pourquoi les autres langues sont un signe, non pour ceux qui croient, mais pour les incrédules; mais la prophétie est un signe, non pour les incrédules, mais pour ceux qui croient.
23 Kotero kuti ngati mpingo wonse utasonkhana pamodzi ndipo aliyense namayankhula malilime, ndipo wina amene sangazindikire kapena ena osakhulupirira nabwerapo, kodi sadzanena kuti mwachita misala?
Si donc toute l'assemblée est réunie et que tous parlent en d'autres langues, et que des personnes incultes ou non croyantes entrent, ne diront-elles pas que vous êtes fous?
24 Koma ngati wosakhulupirira kapena wina amene sakuzindikira abwera pamene aliyense akunenera, adzatsutsika mu mtima ndi zonse zimene akumva ndipo adzaweruzidwa ndi onse
Mais si tous prophétisent, et que quelqu'un d'incroyant ou d'inculte entre, il est repris par tous, et il est jugé par tous.
25 ndipo zinsinsi za mu mtima mwake zidzawululika. Kotero kuti adzadzigwetsa pansi ndi kupembedza Mulungu akufuwula kuti, “Mulungu ali pakati panudi!”
Et ainsi les secrets de son cœur sont révélés. Alors il se prosternera sur sa face et adorera Dieu, déclarant que Dieu est vraiment au milieu de vous.
26 Kodi tsono abale, tinene chiyani? Pamene musonkhana pamodzi, aliyense amakhala ali ndi nyimbo yoti ayimbe, kapena mawu oti alangize, vumbulutso, malilime, kapena kumasulira kwake. Zonsezi cholinga chake chikhale kulimbikitsa mpingo.
Qu'en est-il donc, frères? Quand vous vous réunissez, chacun de vous a un psaume, un enseignement, une révélation, une autre langue ou une interprétation. Que tout soit fait pour vous édifier mutuellement.
27 Ngati wina ayankhula malilime, awiri kapena akachulukapo atatu ndiye ayankhule mmodzimmodzi, ndipo wina ayenera kutanthauzira zimene ayankhulazo.
Si quelqu'un parle dans une autre langue, qu'il y en ait deux, ou au plus trois, et à tour de rôle, et qu'un seul interprète.
28 Ngati palibe wotanthauzira, woyankhulayo akhale chete mu mpingo ndipo adziyankhulire iye mwini ndi Mulungu.
Mais s'il n'y a pas d'interprète, qu'il se taise dans l'assemblée, et qu'il parle à lui-même et à Dieu.
29 Aneneri awiri kapena atatu anenere, ndipo enawo asanthule mosamalitsa zimene anenerazo.
Que deux ou trois des prophètes parlent, et que les autres discernent.
30 Ndipo ngati vumbulutso labwera kwa munthu amene wakhala pansi, amene akuyankhulayo akhale chete.
Mais si une révélation est faite à un autre assis à côté, que le premier se taise.
31 Pakuti nonse mukhoza kunenera mmodzimmodzi motsatana kuti aliyense alangizidwe ndi kulimbikitsidwa.
Car vous pouvez tous prophétiser un par un, afin que tous apprennent et que tous soient exhortés.
32 Mizimu ya aneneri imamvera ulamuliro wa aneneri.
Les esprits des prophètes sont soumis aux prophètes,
33 Pakuti Mulungu si Mulungu wachisokonezo koma wamtendere. Monga mwa mipingo yonse ya oyera mtima.
car Dieu n'est pas un Dieu de confusion, mais de paix, comme dans toutes les assemblées de saints.
34 Amayi akhale chete mʼmisonkhano ya mpingo. Iwo asaloledwe kuyankhula, koma azikhala omvera monga mmene lamulo linenera.
Que les femmes se taisent dans les assemblées, car il ne leur a pas été permis de parler, si ce n'est avec soumission, comme le dit aussi la loi,
35 Ngati ali ndi mafunso, akafunse amuna awo ku nyumba. Nʼchochititsa manyazi kuti mkazi ayankhule mu msonkhano wa mpingo.
si elles veulent apprendre quelque chose. « Qu'elles interrogent leurs maris à la maison, car il est honteux pour une femme de parler dans l'assemblée. »
36 Kodi kapena mawu a Mulungu anachokera kwa inu? Kapena anafika kwa inu nokha?
Quoi!? Est-ce de vous que la parole de Dieu est sortie? Ou bien est-ce à toi seul qu'elle est parvenue?
37 Ngati wina aliyense akuganiza kuti ndi mneneri kapena kuti ali ndi mphatso za Mzimu, ayenera kudziwa kuti zimene ndikukulemberanizi ndi lamulo la Ambuye.
Si quelqu'un se croit prophète ou spirituel, qu'il reconnaisse les choses que je vous écris, qu'elles sont le commandement du Seigneur.
38 Ngati munthu savomereza zimenezi, iyeyonso sadzavomerezedwa.
Mais si quelqu'un est ignorant, qu'il le soit.
39 Nʼchifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse anthu kuyankhula malilime.
C'est pourquoi, frères, ayez le désir ardent de prophétiser, et n'interdisez pas de parler d'autres langues.
40 Koma chilichonse chichitike moyenera ndi mwadongosolo.
Que tout se passe de manière convenable et ordonnée.

< 1 Akorinto 14 >