< 1 Akorinto 14 >

1 Funafunani chikondi, ndikufunitsitsa mphatso zauzimu, makamaka mphatso ya uneneri.
Be eager in your pursuit of this Love, and be earnestly ambitious for spiritual gifts, but let it be chiefly so in order that you may prophesy.
2 Pakuti aliyense amene amayankhula malilime sayankhula kwa anthu, koma kwa Mulungu. Zoonadi, palibe amene amamva zimene akunena chifukwa Mzimu ndiye amamuyankhulitsa zachinsinsi.
For he who speaks in an unknown tongue is not speaking to men, but to God; for no one understands him. Yet in the Spirit he is speaking secret truths.
3 Koma amene amanenera amayankhula kwa anthu kuti awapatse mphamvu, awalimbikitse ndi kuwakhazikitsa mtima pansi.
But he who prophesies speaks to men words of edification, encouragement and comfort.
4 Iye amene amayankhula malilime amadzilimbikitsa yekha, koma amene amanenera amalimbikitsa mpingo.
He who speaks in an unknown tongue does good to himself, but he who prophesies does good to the Church.
5 Nʼkanakonda kuti aliyense mwa inu atamayankhula malilime, koma ndi bwino kuti muzinenera. Amene amanenera amaposa amene amayankhula malilime, pokhapokha atatanthauzira kuti mpingo upindule.
I should be right glad were you all to speak in 'tongues,' but yet more glad were you all to prophesy. And, in fact, the man who prophesies is superior to him who speaks in 'tongues,' except when the latter can interpret in order that the Church may get a blessing.
6 Tsono, abale, mudzapindula chiyani nditabwera kwa inu ndi kukuyankhulani mʼmalilime? Koma mudzapindula ngati nditakubweretserani vumbulutso lina lake, kapena chidziwitso, kapena chiphunzitso.
But, brethren, as things are, if I come to you speaking in 'tongues,' what benefit shall I confer on you, if the utterance is neither in the form of a revelation nor of additional knowledge nor of prophecy nor of teaching?
7 Ngakhale mu zinthu zopanda moyo monga chitoliro kapena gitala, zimene zimatulutsa liwu; kodi munthu akhoza kudziwa bwanji nyimbo imene ikuyimbidwa ngati mawu sakumveka mogwirizana bwino?
Even inanimate things--flutes or harps, for instance--when yielding a sound, if they make no distinction in the notes, how shall the tune which is played on the flute or the harp be known?
8 Komanso ngati lipenga silimveka bwino, ndani angakonzekere nkhondo?
If the bugle--to take another example--gives an uncertain sound, who will prepare for battle?
9 Chimodzimodzinso inu. Ngati simungayankhule mawu omveka bwino mʼchiyankhulo chanu, wina angadziwe bwanji chimene mukunena? Muzingodziyankhulira nokha.
And so with you; if with the living voice you fail to utter intelligible words, how will people know what you are saying? You will be talking to the winds.
10 Mosakayika, pali ziyankhulo zosiyanasiyana pa dziko lapansi, koma palibe nʼchimodzi chomwe chimene chilibe tanthauzo.
There are, we will suppose, a great number of languages in the world, and no creature is without a language.
11 Tsono ngati sindingatolepo tanthauzo la zimene wina akuyankhula, ndiye kuti ndine mlendo kwa oyankhulayo ndipo iyeyo ndi mlendo kwa ine.
If, however, I do not know the meaning of the particular language, I shall seem to the speaker of it, and he to me, to be merely talking some foreign tongue.
12 Chimodzimodzinso inu. Popeza mumafunitsitsa mphatso za Mzimu, yesetseni kuchita bwino pa mphatso zimene zimamanga mpingo.
Therefore, seeing that you are ambitious for spiritual gifts, seek to excel in them so as to benefit the Church.
13 Pa chifukwa ichi munthu amene amayankhula malilime apemphere kuti azitha kutanthauzira zimene akunena.
Therefore let a man who has the gift of tongues pray for the power of interpreting them.
14 Popeza ngati ndipemphera mʼmalilime, ndi mzimu wanga umene ukupemphera, koma nzeru zanga sizikupindula kanthu.
For if I pray in an unknown tongue, my spirit prays, but my understanding is barren.
15 Tsono pamenepa nʼkutani? Ndidzapemphera ndi mzimu wanga, komanso ndidzapemphera ndi nzeru zanga. Ndidzayimba ndi mzimu wanga, komanso ndidzayimba ndi nzeru zanga.
How then does the matter stand? I will pray in spirit, and I will pray with my understanding also. I will praise God in spirit, and I will praise Him with my understanding also.
16 Ngati mutamanda Mulungu mu mzimu, kodi munthu amene wapezeka pakati pa amene akuyankhula zomwe sakumva, adzavomereza bwanji kuti “Ameni” pa pemphero lanu loyamikalo popeza sakumva chimene mukunena?
Otherwise, if you bless God in spirit only, how shall he who is in the position of an ungifted man say the 'Amen' to your giving of thanks, when he does not know what your words mean?
17 Mukhoza kumathokoza mokwanira, koma munthu winayo sanathandizikepo.
Rightly enough you are giving thanks, and yet your neighbor is not benefited.
18 Ndikuyamika Mulungu chifukwa ndimayankhula malilime kuposa nonsenu.
I speak in a tongue, thank God, more than all of you;
19 Koma mu mpingo ndi kwabwino kuti ndiyankhule mawu asanu okha omveka bwino kuti ndilangize bwino ena kusiyana ndikuyankhula mawu ambirimbiri mʼmalilime.
but in the Church I would rather speak five words with my understanding--so as to instruct others also--than ten thousand words in an unknown tongue.
20 Abale, lekani kuganiza ngati ana. Mukhale ana pa nkhani ya zoyipa koma mʼmaganizo anu mukhale okhwima.
Brethren, do not prove yourselves to be children in your minds. As regards evil, indeed, be utter babes, but as regards your minds prove yourselves to be men of ripe years.
21 Zinalembedwa mʼMalamulo kuti, “Ndidzayankhula kwa anthu awa, kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo ndiponso ndi milomo yachilendo. Koma ngakhale nthawi imeneyo sadzandimvera Ine, akutero Ambuye.”
In the Law it stands written, "'By men of unknown tongues and by the lips of an unknown nation will I speak to this People, but even then they will not listen to Me', says the Lord."
22 Kotero, malilime ndi chizindikiro, osati cha kwa okhulupirira koma kwa osakhulupirira. Koma kunenera ndi chizindikiro kwa okhulupirira osati kwa osakhulupirira.
This shows that the gift of tongues is intended as a sign not to those who believe but to unbelievers, but prophecy is intended not for unbelievers but for those who believe.
23 Kotero kuti ngati mpingo wonse utasonkhana pamodzi ndipo aliyense namayankhula malilime, ndipo wina amene sangazindikire kapena ena osakhulupirira nabwerapo, kodi sadzanena kuti mwachita misala?
Accordingly if the whole Church has assembled and all are speaking in 'tongues,' and there come in ungifted men, or unbelievers, will they not say that you are all mad?
24 Koma ngati wosakhulupirira kapena wina amene sakuzindikira abwera pamene aliyense akunenera, adzatsutsika mu mtima ndi zonse zimene akumva ndipo adzaweruzidwa ndi onse
If, on the other hand, every one is prophesying and an unbeliever or an ungifted man comes in, he is convicted by all and closely examined by all,
25 ndipo zinsinsi za mu mtima mwake zidzawululika. Kotero kuti adzadzigwetsa pansi ndi kupembedza Mulungu akufuwula kuti, “Mulungu ali pakati panudi!”
and the hidden evils of his heart are brought to light. And, as the result, he will fall on his face and worship God, and will report to others that of a truth God is among you.
26 Kodi tsono abale, tinene chiyani? Pamene musonkhana pamodzi, aliyense amakhala ali ndi nyimbo yoti ayimbe, kapena mawu oti alangize, vumbulutso, malilime, kapena kumasulira kwake. Zonsezi cholinga chake chikhale kulimbikitsa mpingo.
What then, brethren? Whenever you assemble, there is not one of you who is not ready either with a song of praise, a sermon, a revelation, a 'tongue,' or an interpretation. Let everything be done with a view to the building up of faith and character.
27 Ngati wina ayankhula malilime, awiri kapena akachulukapo atatu ndiye ayankhule mmodzimmodzi, ndipo wina ayenera kutanthauzira zimene ayankhulazo.
If there is speaking in an unknown tongue, only two or at the most three should speak, and they should do so one at a time, and one should interpret;
28 Ngati palibe wotanthauzira, woyankhulayo akhale chete mu mpingo ndipo adziyankhulire iye mwini ndi Mulungu.
or if there is no interpreter, let the man with the gift be silent in the Church, speaking to himself and to God.
29 Aneneri awiri kapena atatu anenere, ndipo enawo asanthule mosamalitsa zimene anenerazo.
But if there are Prophets, let two or three speak and let the rest judge.
30 Ndipo ngati vumbulutso labwera kwa munthu amene wakhala pansi, amene akuyankhulayo akhale chete.
And if anything is revealed to some one else who is seated there, let the first be silent.
31 Pakuti nonse mukhoza kunenera mmodzimmodzi motsatana kuti aliyense alangizidwe ndi kulimbikitsidwa.
For you can all prophesy one by one, so that all may learn and all be encouraged:
32 Mizimu ya aneneri imamvera ulamuliro wa aneneri.
and the spirits of Prophets yield submission to Prophets.
33 Pakuti Mulungu si Mulungu wachisokonezo koma wamtendere. Monga mwa mipingo yonse ya oyera mtima.
For God is not a God of disorder, but of peace, as He is in all the Churches of His people.
34 Amayi akhale chete mʼmisonkhano ya mpingo. Iwo asaloledwe kuyankhula, koma azikhala omvera monga mmene lamulo linenera.
Let married women be silent in the Churches, for they are not permitted to speak. They must be content with a subordinate place, as the Law also says;
35 Ngati ali ndi mafunso, akafunse amuna awo ku nyumba. Nʼchochititsa manyazi kuti mkazi ayankhule mu msonkhano wa mpingo.
and if they wish to ask questions, they should ask their own husbands at home. For it is disgraceful for a married woman to speak at a Church assembly.
36 Kodi kapena mawu a Mulungu anachokera kwa inu? Kapena anafika kwa inu nokha?
Was it from you that God's Message first went forth, or is it to you only that it has come?
37 Ngati wina aliyense akuganiza kuti ndi mneneri kapena kuti ali ndi mphatso za Mzimu, ayenera kudziwa kuti zimene ndikukulemberanizi ndi lamulo la Ambuye.
If any one deems himself to be a Prophet or a man with spiritual gifts, let him recognize as the Lord's command all that I am now writing to you.
38 Ngati munthu savomereza zimenezi, iyeyonso sadzavomerezedwa.
But if any one is ignorant, let him be ignorant.
39 Nʼchifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse anthu kuyankhula malilime.
The conclusion, my brethren, is this. Be earnestly ambitious to prophesy, and do not check speaking with tongues;
40 Koma chilichonse chichitike moyenera ndi mwadongosolo.
only let everything be done in a becoming and orderly manner.

< 1 Akorinto 14 >