< 1 Akorinto 11 >
1 Tsatirani chitsanzo changa, monga inenso nditsatira chitsanzo cha Khristu.
Luwuru timna, mana kaka an bende aluwo tim Kristo.
2 Ndikukuyamikani chifukwa chondikumbukira pa zonse ndiponso posunga ziphunzitso monga ndinakuphunzitsirani.
Agoyonu erokamano nikech usiko upara e yore duto, kendo nikech umako puonj duto mane amiyou.
3 Tsopano ndikufuna muzindikire kuti Khristu ndiye mutu wa munthu aliyense, ndipo mwamuna ndiye mutu wamkazi, ndipo mutu wa Khristu ndi Mulungu.
To adwaro mondo ungʼe ni Kristo ewi dichwo ka dichwo, kendo ni dichwo ewi dhako, to Nyasaye ewi Kristo.
4 Mwamuna aliyense wopemphera kapena kunenera ataphimba mutu wake akunyoza mutu wakewo.
Kuom mano, dichwo malemo kata makoro e chokruok koumo wiye ochayo Kristo.
5 Ndipo mkazi aliyense wopemphera kapena kunenera asanaphimbe mutu wake sakulemekeza mutu wakewo. Kuli chimodzimodzi kumeta mutu wake.
Kamano bende dhako malemo kata makoro e chokruok, ka ok otweyo kitamba okuodo wi chwore, nikech onge pogruok e kinde gi dhako moliel yie wiye.
6 Ngati mkazi saphimba kumutu kwake, ndiye kuti amete tsitsi lake. Ngati nʼchamanyazi kwa mkazi kungoyepula kapena kumeta mpala, ndiye kuti aphimbe kumutu kwake.
Ka dhako ok dwar tweyo kitamba, to ber kata mondo oliel yie wiye. To kaka en wichkuot ka dhako olielo yie wiye mapoth, to ber otwe kitamba.
7 Mwamuna sayenera kuphimba kumutu popeza ndi chifaniziro ndi ulemerero wa Mulungu; pamene mkazi ndi ulemerero wa mwamuna.
Dichwo to ok owinjore oum wiye nikech en ranyisi mar Nyasaye gi duongʼne; dhako to en ranyisi mar duongʼ mar dichwo.
8 Pakuti mwamuna sachokera kwa mkazi, koma mkazi kwa mwamuna.
Dichwo ne ok oa kuom dhako, to dhako ema ne oa kuom dichwo.
9 Ndipo mwamuna sanalengedwe chifukwa cha mkazi, koma mkazi analengedwera mwamuna.
To bende, dichwo ne ok ochwe ne dhako, to dhako ema ne ochwe ni dichwo.
10 Pa chifukwa ichi, ndiponso pa chifukwa cha angelo, mkazi akuyenera kukhala ndi chizindikiro cha ulamuliro wake.
Nikech wachni kendo nikech malaike, dhako mondo oum wiye kaka ranyisi ni en e bwo loch.
11 Komabe mwa Ambuye, mkazi amadalira mwamuna ndipo mwamuna amadalira mkazi.
Kata kamano, kuom Ruoth, dhako ok nyal dak maonge dichwo mana kaka dichwo bende ok nyal dak maonge dhako.
12 Pakuti monga mkazi anachokera kwa mwamuna, momwemonso mwamuna anabadwa mwa mkazi. Koma zonse zichokera kwa Mulungu.
Nimar, mana kaka dhako nochwe koa kuom dichwo, e kaka dichwo bende inywolo gi dhako, to gik moko duto oa kuom Nyasaye.
13 Dziweruzeni. Kodi nʼchabwino kuti mkazi apemphere kwa Mulungu wopanda chophimba kumutu?
Penjreuru un uwegi ni: Bende en gima kare mondo dhako olam Nyasaye ka ok otweyo kitamba e wiye?
14 Kodi chikhalidwe chathu sichitiphunzitsa kuti nʼchamanyazi kuti mwamuna akhale ndi tsitsi lalitali,
Donge en gima ongʼere ne ji duto ni wich maboyo en wichkuot ni dichwo?
15 koma mkazi akakhala ndi tsitsi lalitali ndi ulemerero wake? Pakuti mkazi anapatsidwa tsitsi lalitali monga chophimba kumutu.
To ka dhako yie wiye boyo, to en duongʼ mare, nikech yie wich maboyo omiye kaka raum.
16 Ngati wina akufuna kutsutsapo pa zimenezi, ife ndiponso mipingo ya Mulungu tilibe machitidwe ena apadera koma ndi omwewa.
Ka ngʼato kuomu dwaro kwedo ma, to ongʼe ni waonge gi tim mopogore gi mwapuonjoni, kendo kata kanise duto mag Nyasaye ongego.
17 Koma popereka malangizo awa sindikufuna kukuyamikirani popeza mʼmisonkhano yanu mumachita zoyipa kuposa zabwino.
Puonj makoro amiyou sani to ok anyal pakoue, nikech kinde duto ma uchokoru kaachiel to chokruoku kelo mana rach kar kelo ber.
18 Choyamba, ndikumva kuti mukasonkhana mu mpingo mumasankhana ndipo ndikukhulupirira kuti zimenezi kwinaku nʼzoona.
Mokwongo awinjo ni ka uchokoru kaachiel kaka kanisa, to nitie pogruok e kindu, kendo anyalo yie ni wachno en adier.
19 Nʼzosakayikitsa kuti pali kugawikana pakati panu kuti adziwike amene ndi ovomerezeka ndi Mulungu.
Mano emomiyo nitiere pogruok e kindu mondo joma Nyasaye oyiego ongʼere maler.
20 Tsono, mukasonkhana pamodzi, chimene mumadya si Mgonero wa Ambuye.
Ka uchokoru kanyakla, to nenore ni ok ucham Sap Ruoth;
21 Pakuti mukamadya, aliyense amangodzidyera zomwe anakonza. Wina amakhala ndi njala pamene wina amaledzera.
nikech ka uchiemo to ngʼato ka ngʼato rikni gichamo chiembe owuon, ma ok orito jowetene; omiyo jomoko kuomu denyo, to jomoko kuomu to mer.
22 Kodi mulibe nyumba zanu kumene mungamadyere ndi kumwa? Kapena mumapeputsa mpingo wa Mulungu ndi kuchititsa manyazi amene alibe kalikonse? Ndikunena chiyani kwa inu? Moti ndikuyamikireni pa zimenezi? Ayi, pa zinthu izi sindingakuyamikireni.
Donge un gi miechu munyalo chiemoe kendo methoe? Koso uchayo kanisa Nyasaye, momiyo ukuodo wi joma ochando? Angʼo ma dawachnu? Uparo ni dapaku kuom wachni? Ok kamano ngangʼ!
23 Pakuti zimene ndinalandira kwa Ambuye ndi zomwe ndinakupatsani. Ambuye Yesu, usiku umene anaperekedwa uja, anatenga buledi.
Puonj mane ayudo kuom Ruoth mi amiyou chal kama: Ruoth Yesu nokawo makati e otienono mane ondhogee,
24 Atayamika ndi kumunyema ananena kuti, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”
kendo bangʼ kosegoyo erokamano nongʼingo, kowacho niya, “Ma en ringra mochiw nikech un, timuru ma ka uparago.”
25 Chimodzimodzi, atatha kudya, anatenga chikho, nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga; imwani nthawi zonse pokumbukira Ine.”
Kamano bende bangʼ chiemo nokawo kikombe, mi owacho niya, “Kikombeni en singruok manyien motim gi remba; timuru ma, kinde duto mumadhee, mondo uparago.”
26 Pakuti nthawi zonse pamene mudya bulediyu ndikumwa chikhochi, mukulalikira imfa ya Ambuye mpaka Iye adzabweranso.
Nikech ka usiko uchamo makatini kendo umadho kikombeni, to unyiso tho mar Ruoth nyaka chop oduogi.
27 Chifukwa chake, aliyense amene adya buledi kapena kumwa chikho cha Ambuye mʼnjira yosayenera adzachimwira thupi ndi magazi a Ambuye.
Emomiyo ngʼama ochamo makatini kata ometho e kikombeni e yo ma ok owinjore, bura biro loyo kodoko jaketho kuom ringre Ruoth gi rembe.
28 Munthu adzisanthule yekha asanadye buledi kapena kumwa chikhochi.
Ngʼato ka ngʼato nyaka nonre mokwongo, kapok ochamo makati kata ometho e kikombe.
29 Popeza aliyense amene adya kapena kumwa mosazindikira thupi la Ambuye, amadya ndi kumwa chiweruzo chake chomwe.
Nikech ngʼato angʼata mochiemo kendo ometho, ma ok odewo ni gin ringre Ruoth, kelo bura kuome owuon.
30 Nʼchifukwa chake pakati panu ambiri mwa inu ndi ofowoka ndi odwala, ndipo ambirinso agona tulo.
Mano emomiyo ji mathoth kuomu ool kendo tuo; kendo moko kuomu osetho.
31 Koma tikanadziyesa tokha sitikaweruzidwanso.
To ka dine wanonre wawegi mokwongo, to bura ok doloyowa.
32 Pamene tiweruzidwa ndi Ambuye, ndiye kuti akukonza khalidwe lathu kupewa kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi anthu osakhulupirira.
To ka Ruoth ngʼadonwa bura to orieyowa mondo kik bura lowa kaachiel gi jopinyni.
33 Ndiye tsono abale anga, pamene musonkhana pa chakudya, mudikirirane.
Kuom mano, jowetena, ka uchokoru kaachiel mondo uchiem, to ngʼato ka ngʼato mondo orit nyawadgi.
34 Ngati wina ali ndi njala, adye ku nyumba kwake kuti pamene musonkhana pamodzi zisafike poti muweruzidwe nazo. Ndipo ndikabwera ndidzakupatsani malangizo ena owonjezera.
To ka ngʼato odenyo, to ber mondo ochiem dala, mondo kik chokruok ma ubedogo kelnu kum. Weche modongʼ anawachnu ka abiro.