< 1 Akorinto 11 >
1 Tsatirani chitsanzo changa, monga inenso nditsatira chitsanzo cha Khristu.
Taa Krstosi tiartsok'o itwere taan arore.
2 Ndikukuyamikani chifukwa chondikumbukira pa zonse ndiponso posunga ziphunzitso monga ndinakuphunzitsirani.
Jam aawo taan it gawirwonat itsh t imts dano kúp'idek'at dets itdek'tsotse, itn údiruwe.
3 Tsopano ndikufuna muzindikire kuti Khristu ndiye mutu wa munthu aliyense, ndipo mwamuna ndiye mutu wamkazi, ndipo mutu wa Khristu ndi Mulungu.
Ernmó nungush jami tooko Krstosi, mááts tooko nungusho, Krstos tokonwere Ik'o niho b́wottsok'o it danetwok'o shunfee.
4 Mwamuna aliyense wopemphera kapena kunenera ataphimba mutu wake akunyoza mutu wakewo.
Tooko p'urdek't Ik' k'oniruwo wee bek'i aap'o keewiru nungush jamo b́ tookoniye b́ketiyiri.
5 Ndipo mkazi aliyense wopemphera kapena kunenera asanaphimbe mutu wake sakulemekeza mutu wakewo. Kuli chimodzimodzi kumeta mutu wake.
Mank'owere btooko p'ur bde'awon Ik' k'oniru wee bek'i aap'o keewiru máátsu b tookoniye bketiri, btooko p'ureraw máátsu bs'ageetsok'owe b́taaweti.
6 Ngati mkazi saphimba kumutu kwake, ndiye kuti amete tsitsi lake. Ngati nʼchamanyazi kwa mkazi kungoyepula kapena kumeta mpala, ndiye kuti aphimbe kumutu kwake.
Máátsu b tooko p'ureratsane wotiyal b took s'iiro k'ut'ewiye, ernmó btook s'iiro k'ut'ewo wee s'ageyo bin ketit keewa wotiyal b tooko p'urowiye.
7 Mwamuna sayenera kuphimba kumutu popeza ndi chifaniziro ndi ulemerero wa Mulungu; pamene mkazi ndi ulemerero wa mwamuna.
Nungusho Ik'o ariyetsonat Ik' mango bín b́ be'etk b́ wottsotse b́ tooko p'uro geyiratse, máátsunmó nungushi mangiye.
8 Pakuti mwamuna sachokera kwa mkazi, koma mkazi kwa mwamuna.
Máátsuni nungushatse daatseyi bako nungusho máátsatse daatseratse.
9 Ndipo mwamuna sanalengedwe chifukwa cha mkazi, koma mkazi analengedwera mwamuna.
Mank'were máátsu nungushosha bi azeeyi bako nungusho máátsush azeratse
10 Pa chifukwa ichi, ndiponso pa chifukwa cha angelo, mkazi akuyenera kukhala ndi chizindikiro cha ulamuliro wake.
Hanatse tutsonat melakiwots shinatse alishirootse b́fa'ok'o kitsitwo, p'uro b tookats gerde'iye.
11 Komabe mwa Ambuye, mkazi amadalira mwamuna ndipo mwamuna amadalira mkazi.
Doonzoke no detsts beyon máátsu nungushalo beratsane, nungushonu máátsalo beeratse.
12 Pakuti monga mkazi anachokera kwa mwamuna, momwemonso mwamuna anabadwa mwa mkazi. Koma zonse zichokera kwa Mulungu.
Máátsu nungushatse b datetsok'o nungushonu b́ shuwet máátsatsne, ernmó nungusha wotowa mááts wotowa k'osh jamkeewonu Ik'okne b́ daatseti.
13 Dziweruzeni. Kodi nʼchabwino kuti mkazi apemphere kwa Mulungu wopanda chophimba kumutu?
Aab it tookon anghsuwere, máátsu btooko b p'urerawo Ik'o k'ono bish wotituwa?
14 Kodi chikhalidwe chathu sichitiphunzitsa kuti nʼchamanyazi kuti mwamuna akhale ndi tsitsi lalitali,
Nungusho b́ took s'iiro b́genziyal bísh keeti mit b́ wotok'o hank'on azeyon danekosha?
15 koma mkazi akakhala ndi tsitsi lalitali ndi ulemerero wake? Pakuti mkazi anapatsidwa tsitsi lalitali monga chophimba kumutu.
Máátsunmó bish took s'iiro ime btooko bín ipbdek'etuwok'o b́wottsotse btook s'iiro bgeenziyal bish bmangee.
16 Ngati wina akufuna kutsutsapo pa zimenezi, ife ndiponso mipingo ya Mulungu tilibe machitidwe ena apadera koma ndi omwewa.
Han jangatse moosh geyiru asho fa'ewotiyal noon wotowa Ik'i maa k'oshuwots wotowa hank'o doyo deshatsone.
17 Koma popereka malangizo awa sindikufuna kukuyamikirani popeza mʼmisonkhano yanu mumachita zoyipa kuposa zabwino.
It ko'ewor it k'aliruwo gonda bako sheeng keew b́woterawotse and itsh ti imiru dananatse iti úderatse.
18 Choyamba, ndikumva kuti mukasonkhana mu mpingo mumasankhana ndipo ndikukhulupirira kuti zimenezi kwinaku nʼzoona.
Jamoniyere shino ikwotdek'at it kakuwewor it dagotse k'osh k'oshewo b́beyo shishre, t shishts keewonwere badooko arik b́wottsok'o amaniruwe.
19 Nʼzosakayikitsa kuti pali kugawikana pakati panu kuti adziwike amene ndi ovomerezeka ndi Mulungu.
Ar keewetsuwots konotsi bowottsok'o galeyar bodanetwok'o ititse k'osh k'oshewo b́beyo jinatse.
20 Tsono, mukasonkhana pamodzi, chimene mumadya si Mgonero wa Ambuye.
Ikok it kakuwewor it meeyir doonzo kooc'i mishaliye.
21 Pakuti mukamadya, aliyense amangodzidyera zomwe anakonza. Wina amakhala ndi njala pamene wina amaledzera.
It móór iko iko b́ korááwo bíyaailye b́meyiri, mank'oon iko b́ k'ak'efere iko mashe b́mashiri.
22 Kodi mulibe nyumba zanu kumene mungamadyere ndi kumwa? Kapena mumapeputsa mpingo wa Mulungu ndi kuchititsa manyazi amene alibe kalikonse? Ndikunena chiyani kwa inu? Moti ndikuyamikireni pa zimenezi? Ayi, pa zinthu izi sindingakuyamikireni.
Eshe it meetuwoknat it úshet moo deshatsteya? Himó Ik' moone it gac'iri? Himó eegoru bo meetu deshawwotsne it jiitsiri? Eshe eege itsh tieteti? Keewansh iten údota? B́ jamon úderatse!
23 Pakuti zimene ndinalandira kwa Ambuye ndi zomwe ndinakupatsani. Ambuye Yesu, usiku umene anaperekedwa uja, anatenga buledi.
Doonzoke t dek'tsonat itsh tbeshits dano haniye, doonzo besheyat b́ imewots t'ú manots misho k'aúb́dek'i,
24 Atayamika ndi kumunyema ananena kuti, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”
Ik'o b́ údiyakon tiitsdek't, «[nahere móóre, ] han itsh wotituwo tiaatsoniye, han taan bín itgawitwo wosh de'ere» bíeti
25 Chimodzimodzi, atatha kudya, anatenga chikho, nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga; imwani nthawi zonse pokumbukira Ine.”
Mank'o kooc' mishoniyre il úshi wanc'o k'aaúdek't «Úshi wanc'an t s'atson finet handr taaroniye, jam aawo han itúshor bín taan gawosh wosh de'ere» bí eti.
26 Pakuti nthawi zonse pamene mudya bulediyu ndikumwa chikhochi, mukulalikira imfa ya Ambuye mpaka Iye adzabweranso.
Mishan itmooronat úshi wanc'an it úshor jam aawo doonzo b́ wafetsosh b́ k'iro keewitute.
27 Chifukwa chake, aliyense amene adya buledi kapena kumwa chikho cha Ambuye mʼnjira yosayenera adzachimwira thupi ndi magazi a Ambuye.
Konuworu asho bísh wot geyirawo doonzo tusho b́ móónat doonzo úshi wanc'an b́ úshal doonzo atsonat s'atso k'awunts bí ats wotituwe.
28 Munthu adzisanthule yekha asanadye buledi kapena kumwa chikhochi.
Eshe konworu asho tushan b́ mooniyere shinonat wanc'an b́ úshoneyere shino b́ tooko shú s'iilo bísh geyife.
29 Popeza aliyense amene adya kapena kumwa mosazindikira thupi la Ambuye, amadya ndi kumwa chiweruzo chake chomwe.
Asho konworu doonzo atso eeg b́ wotok'o galde'er b́ dananiyere doonzo tusho b́ maal doonzo úshi wanc'o b́ úshal b́ tookats angshe b́ doweti.
30 Nʼchifukwa chake pakati panu ambiri mwa inu ndi ofowoka ndi odwala, ndipo ambirinso agona tulo.
It dagotsere ayuwots bomawutsonat boshodu ik ikuwotsu bok'iriye han jangatsne.
31 Koma tikanadziyesa tokha sitikaweruzidwanso.
Noo notokats angshrone wotink'e no ats angsherawunk'ee b́teshi.
32 Pamene tiweruzidwa ndi Ambuye, ndiye kuti akukonza khalidwe lathu kupewa kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi anthu osakhulupirira.
Ernmó il datsunton noats angsherawok'o and angshiru doonzo noon b́ seziri.
33 Ndiye tsono abale anga, pamene musonkhana pa chakudya, mudikirirane.
Eshe t eshuwotso! Doonzo kooc' mishosh it ko'eyor it ats atseyo korewere.
34 Ngati wina ali ndi njala, adye ku nyumba kwake kuti pamene musonkhana pamodzi zisafike poti muweruzidwe nazo. Ndipo ndikabwera ndidzakupatsani malangizo ena owonjezera.
It ko'ewo angshosh b́ woterawok'o ititse k'ak'ts asho b́ beyal b́ meyitse moowe. Oorts keewosh taa manok twoor dabr bín jiishetwo itsh imetuwe.